< مزامیر 82 >
مزمور آساف خدا در جماعت خدا ایستاده است. درمیان خدایان داوری میکند: | ۱ 1 |
Salimo la Asafu. Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu; Iye akuweruza pakati pa “milungu.”
«تا به کی به بیانصافی داوری خواهید کرد و شریران راطرفداری خواهید نمود؟ سلاه. | ۲ 2 |
“Mudzateteza osalungama mpaka liti, ndi kukondera anthu oyipa?
فقیران و یتیمان را دادرسی بکنید. مظلومان و مسکینان را انصاف دهید. | ۳ 3 |
Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye; mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
مظلومان و فقیران را برهانید و ایشان را ازدست شریران خلاصی دهید. | ۴ 4 |
Landitsani anthu ofowoka ndi osowa; apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.
«نمی دانند و نمی فهمند و در تاریکی راه میروند و جمیع اساس زمین متزلزل میباشد. | ۵ 5 |
“Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse. Amayendayenda mu mdima; maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.
من گفتم که شما خدایانید و جمیع شما فرزندان حضرت اعلی. | ۶ 6 |
“Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu, nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
لیکن مثل آدمیان خواهید مرد وچون یکی از سروران خواهید افتاد!» | ۷ 7 |
Koma mudzafa ngati anthu wamba; mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”
ای خدا برخیز و جهان را داوری فرما زیراکه تو تمامی امتها را متصرف خواهی شد. | ۸ 8 |
Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi, pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.