< مزامیر 140 >
برای سالار مغنیان. مزمور داود ای خداوند، مرا از مرد شریر رهایی ده و از مرد ظالم مرا محفوظ فرما! | ۱ 1 |
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Landitseni Yehova kwa anthu oyipa; tetezeni kwa anthu ankhanza,
که در دلهای خود در شرارت تفکر میکنند وتمامی روز برای جنگ جمع میشوند. | ۲ 2 |
amene mu mtima mwawo amakonza zinthu zoyipa ndi kuyambitsa nkhondo tsiku lililonse.
دندانهای خود را مثل مار تیز میکنند و زهرافعی زیر لب ایشان است، سلاه. | ۳ 3 |
Iwo amanola malilime awo kukhala akuthwa ngati a njoka; pa milomo yawo pali ululu wa mamba. (Sela)
ای خداوند مرااز دست شریر نگاه دار، از مرد ظالم مرا محافظت فرما که تدبیر میکنند تا پایهای مرا بلغزانند. | ۴ 4 |
Tetezeni Inu Yehova, kwa anthu oyipa; tchinjirizeni kwa anthu ankhanza amene amakonza zokola mapazi anga.
متکبران برای من تله و ریسمانها پنهان کرده ودام بهسر راه گسترده، و کمندها برای من نهادهاند، سلاه. | ۵ 5 |
Anthu odzikuza anditchera msampha mobisika; iwo atchera zingwe za maukonde awo ndipo anditchera misampha pa njira yanga. (Sela)
به خداوند گفتم: «تو خدای من هستی. ای خداوند آواز تضرع مرا بشنو!» | ۶ 6 |
Inu Yehova, ine ndikuti, “Ndinu Mulungu wanga.” Imvani kupempha kwanga Yehova.
ای یهوه خداوندکه قوت نجات من هستی، تو سر مرا در روز جنگ پوشانیدهای. | ۷ 7 |
Inu Ambuye Wamphamvuzonse, Mpulumutsi wanga wamphamvu, mumateteza mutu wanga tsiku lankhondo.
ای خداوند، آرزوهای شریر رابرایش برمیاور و تدابیر ایشان را به انجام مرسان مبادا سرافراشته شوند، سلاه. | ۸ 8 |
Musawapatse anthu oyipa zokhumba zawo, Inu Yehova; musalole kuti zokonza zawo zitheke, mwina iwo adzayamba kunyada. (Sela)
و اما سرهای آنانی که مرا احاطه میکنند، شرارت لبهای ایشان، آنها را خواهد پوشانید. | ۹ 9 |
Mitu ya amene andizungulira iphimbidwe ndi masautso amene milomo yawo yayambitsa.
اخگرهای سوزنده را برایشان خواهند ریخت، ایشان را درآتش خواهند انداخت و در ژرفیها که دیگرنخواهند برخاست. | ۱۰ 10 |
Makala amoto agwere pa iwo; aponyedwe pa moto, mʼmaenje amatope, asatulukemonso.
مرد بدگو در زمین پایدارنخواهد شد. مرد ظالم را شرارت صید خواهدکرد تا او را هلاک کند | ۱۱ 11 |
Musalole kuti anthu achipongwe akhazikike mʼdziko; choyipa chilondole anthu ankhanza.
میدانم که خداونددادرسی فقیر را خواهد کرد و داوری مسکینان راخواهد نمود. | ۱۲ 12 |
Ndikudziwa kuti Yehova amapereka chiweruzo cholungama kwa anthu osauka, ndipo amateteza zolinga za anthu osowa.
هر آینه عادلان نام تو را حمدخواهند گفت و راستان به حضور تو ساکن خواهند شد. | ۱۳ 13 |
Zoonadi anthu olungama adzatamanda dzina lanu, ndipo anthu owongoka mtima adzakhala pamaso panu.