< مزامیر 140 >

برای سالار مغنیان. مزمور داود ای خداوند، مرا از مرد شریر رهایی ده و از مرد ظالم مرا محفوظ فرما! ۱ 1
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Landitseni Yehova kwa anthu oyipa; tetezeni kwa anthu ankhanza,
که در دلهای خود در شرارت تفکر می‌کنند وتمامی روز برای جنگ جمع می‌شوند. ۲ 2
amene mu mtima mwawo amakonza zinthu zoyipa ndi kuyambitsa nkhondo tsiku lililonse.
دندانهای خود را مثل مار تیز می‌کنند و زهرافعی زیر لب ایشان است، سلاه. ۳ 3
Iwo amanola malilime awo kukhala akuthwa ngati a njoka; pa milomo yawo pali ululu wa mamba. (Sela)
‌ای خداوند مرااز دست شریر نگاه دار، از مرد ظالم مرا محافظت فرما که تدبیر می‌کنند تا پایهای مرا بلغزانند. ۴ 4
Tetezeni Inu Yehova, kwa anthu oyipa; tchinjirizeni kwa anthu ankhanza amene amakonza zokola mapazi anga.
متکبران برای من تله و ریسمانها پنهان کرده ودام به‌سر راه گسترده، و کمندها برای من نهاده‌اند، سلاه. ۵ 5
Anthu odzikuza anditchera msampha mobisika; iwo atchera zingwe za maukonde awo ndipo anditchera misampha pa njira yanga. (Sela)
به خداوند گفتم: «تو خدای من هستی. ای خداوند آواز تضرع مرا بشنو!» ۶ 6
Inu Yehova, ine ndikuti, “Ndinu Mulungu wanga.” Imvani kupempha kwanga Yehova.
‌ای یهوه خداوندکه قوت نجات من هستی، تو سر مرا در روز جنگ پوشانیده‌ای. ۷ 7
Inu Ambuye Wamphamvuzonse, Mpulumutsi wanga wamphamvu, mumateteza mutu wanga tsiku lankhondo.
‌ای خداوند، آرزوهای شریر رابرایش برمیاور و تدابیر ایشان را به انجام مرسان مبادا سرافراشته شوند، سلاه. ۸ 8
Musawapatse anthu oyipa zokhumba zawo, Inu Yehova; musalole kuti zokonza zawo zitheke, mwina iwo adzayamba kunyada. (Sela)
و اما سرهای آنانی که مرا احاطه می‌کنند، شرارت لبهای ایشان، آنها را خواهد پوشانید. ۹ 9
Mitu ya amene andizungulira iphimbidwe ndi masautso amene milomo yawo yayambitsa.
اخگرهای سوزنده را برایشان خواهند ریخت، ایشان را درآتش خواهند انداخت و در ژرفیها که دیگرنخواهند برخاست. ۱۰ 10
Makala amoto agwere pa iwo; aponyedwe pa moto, mʼmaenje amatope, asatulukemonso.
مرد بدگو در زمین پایدارنخواهد شد. مرد ظالم را شرارت صید خواهدکرد تا او را هلاک کند ۱۱ 11
Musalole kuti anthu achipongwe akhazikike mʼdziko; choyipa chilondole anthu ankhanza.
می‌دانم که خداونددادرسی فقیر را خواهد کرد و داوری مسکینان راخواهد نمود. ۱۲ 12
Ndikudziwa kuti Yehova amapereka chiweruzo cholungama kwa anthu osauka, ndipo amateteza zolinga za anthu osowa.
هر آینه عادلان نام تو را حمدخواهند گفت و راستان به حضور تو ساکن خواهند شد. ۱۳ 13
Zoonadi anthu olungama adzatamanda dzina lanu, ndipo anthu owongoka mtima adzakhala pamaso panu.

< مزامیر 140 >