< اعداد 2 >
و خداوند موسی و هارون را خطاب کرده، گفت: | ۱ 1 |
Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni:
«هر کس از بنیاسرائیل نزد علم ونشان خاندان آبای خویش خیمه زند، در برابر واطراف خیمه اجتماع خیمه زنند. | ۲ 2 |
“Aisraeli azimanga misasa yawo mozungulira tenti ya msonkhano motalikira pangʼono. Munthu aliyense amange pamene pali mbendera ya fuko lake.”
و بهجانب مشرق به سوی طلوع آفتاب اهل علم محله یهودابرحسب افواج خود خیمه زنند، و رئیس بنی یهودا نحشون بن عمیناداب باشد. | ۳ 3 |
Kummawa, kotulukira dzuwa, magulu a msasa wa Yuda amange pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Ayudawo ndi Naasoni mwana wa Aminadabu.
و فوج اوکه از ایشان شمرده شدند هفتاد و چهار هزار وششصد نفر بودند. | ۴ 4 |
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 74,600.
و سبط یساکار در پهلوی اوخیمه زنند، و رئیس بنی یساکار نتنائیل بن صوغرباشد. | ۵ 5 |
Fuko la Isakara lidzamanga pafupi ndi Yuda. Mtsogoleri wa gulu la Isakara ndi Netanieli mwana wa Zuwara.
و فوج او که از ایشان شمرده شدند پنجاه و چهار هزار و چهارصد نفر بودند. | ۶ 6 |
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 54,400.
و سبطزبولون و رئیس بنی زبولون الیاب بن حیلون باشد. | ۷ 7 |
Lotsatira lidzakhala fuko la Zebuloni. Mtsogoleri wa gulu la Zebuloni ndi Eliabu mwana wa Heloni.
و فوج او که از ایشان شمرده شدند، پنجاه وهفت هزار و چهارصد نفر بودند. | ۸ 8 |
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 57,400.
جمیع شمرده شدگان محله یهودا برحسب افواج ایشان صد و هشتاد و شش هزار و چهارصد نفر بودند. وایشان اول کوچ کنند. | ۹ 9 |
Anthu onse aamuna mʼmisasa ya Yuda, chiwerengero chawo ndi 186,400 monga mwa magulu awo. Iwowo ndiwo aziyamba kusamuka.
و بر جانب جنوب، علم محله روبین برحسب افواج ایشان باشد، و رئیس بنی روبین الیصور بن شدیئور باشد. | ۱۰ 10 |
Kummwera kudzakhala magulu a msasa wa Rubeni pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa gulu la Rubeni ndi Elizuri mwana wa Sedeuri.
و فوج او که از ایشان شمرده شدند چهل و شش هزار و پانصد نفر بودند. | ۱۱ 11 |
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 46,500.
و در پهلوی او سبط شمعون خیمه زنندو رئیس بنی شمعون شلومیئیل بن صوریشدای باشد. | ۱۲ 12 |
Fuko la Simeoni lidzamanga pafupi ndi Rubeni. Mtsogoleri wa gulu la Simeoni ndi Selumieli mwana wa Zurisadai.
و فوج او که از ایشان شمرده شدند، پنجاه و نه هزار و سیصد نفر بودند. | ۱۳ 13 |
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 59,300.
و سبط جادو رئیس بنی جاد الیاساف بن رعوئیل باشد. | ۱۴ 14 |
Lotsatira lidzakhala fuko la Gadi. Mtsogoleri wa gulu la Gadi ndi Eliyasafu mwana wa Deuweli.
وفوج او که از ایشان شمرده شدند، چهل و پنج هزار و ششصد و پنجاه نفر بودند. | ۱۵ 15 |
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 45,650.
جمیع شمرده شدگان محله روبین برحسب افواج ایشان صد و پنجاه و یک هزار و چهارصد و پنجاه نفربودند و ایشان دوم کوچ کنند. | ۱۶ 16 |
Anthu onse aamuna mu msasa wa Rubeni, chiwerengero chawo monga mwa magulu awo, ndi 151,450. Iwowo azikhala achiwiri posamuka.
و بعد از آن خیمه اجتماع با محله لاویان درمیان محلهها کوچ کند، چنانکه خیمه میزنند، همچنان هر کس در جای خود نزد علمهای خویش کوچ کنند. | ۱۷ 17 |
Tsono tenti ya msonkhano ndi msasa wa Alevi zidzakhala pakati pa misasayo. Iwo adzasamuka monga momwe anamangira misasa yawo, aliyense pa malo ake pamene pali mbendera yake.
و به طرف مغرب، علم محله افرایم برحسب افواج ایشان و رئیس بنی افرایم، الیشمع بن عمیهود باشد. | ۱۸ 18 |
Kumadzulo kudzakhala magulu a msasa wa Efereimu pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Aefereimuwo ndi Elisama mwana wa Amihudi.
و فوج او که از ایشان شمرده شدند، چهل هزار و پانصد نفر بودند. | ۱۹ 19 |
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 40,500.
و درپهلوی او سبط منسی، و رئیس بنی منسی جملیئیل بن فدهصور باشد. | ۲۰ 20 |
Fuko la Manase lidzakhala pafupi ndi Efereimu. Mtsogoleri wa Amanase ndi Gamalieli mwana wa Pedazuri.
و فوج او که ازایشان شمرده شدند، سی و دو هزار و دویست نفربودند. | ۲۱ 21 |
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 32,200.
و سبط بنیامین و رئیس بنی بنیامین، ابیدان بن جدعونی باشد. | ۲۲ 22 |
Lotsatira lidzakhala fuko la Benjamini. Mtsogoleri wa Abenjamini ndi Abidani mwana wa Gideoni.
و فوج او که از ایشان شمرده شدند، سی و پنج هزار و چهارصد نفربودند. | ۲۳ 23 |
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 35,400.
جمیع شمرده شدگان محله افرایم برحسب افواج ایشان، صد و هشت هزار و یکصدنفر بودند، و ایشان سوم کوچ کنند. | ۲۴ 24 |
Anthu onse aamuna mu msasa wa Efereimu, chiwerengero chawo ndi 108,100 monga mwa magulu awo. Iwowo azikhala achitatu posamuka.
و به طرف شمال، علم محله دان، برحسب افواج ایشان، و رئیس بنی دان اخیعزر بن عمیشدای باشد. | ۲۵ 25 |
Kumpoto kudzakhala msasa wa magulu a Dani pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Adani ndi Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
و فوج او که از ایشان شمرده شدند، شصت و دو هزاروهفت صد نفر بودند. | ۲۶ 26 |
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 62,700.
ودر پهلوی ایشان سبط اشیر خیمه زنند، و رئیس بنی اشیر فجعیئیل بن عکران باشد. | ۲۷ 27 |
Fuko la Aseri lidzamanga pafupi ndi iwowo. Mtsogoleri wa Aaseri ndi Pagieli mwana wa Okirani.
و فوج او که از ایشان شمرده شدند، چهل و یک هزار و پانصدنفر بودند. | ۲۸ 28 |
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 41,500.
و سبط نفتالی و رئیس بنی نفتالی اخیرع بن عینان باشد. | ۲۹ 29 |
Lotsatira lidzakhala fuko la Nafutali. Mtsogoleri wa Anafutali ndi Ahira mwana wa Enani.
و فوج او که از ایشان شمرده شدند، پنجاه و سه هزار و چهارصد نفربودند. | ۳۰ 30 |
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 53,400.
جمیع شمرده شدگان محله دان، صد وپنجاه و هفت هزار و ششصد نفر بودند. ایشان نزدعلمهای خود در عقب کوچ کنند. | ۳۱ 31 |
Anthu onse aamuna mu msasa wa Dani chiwerengero chawo ndi 157,600. Iwo azidzanyamuka pomaliza, ndi mbendera zawo.
اینانند شمرده شدگان بنیاسرائیل برحسب خاندان آبای ایشان، جمیع شمرده شدگان محلهها موافق افواج ایشان شش صد و سه هزار وپانصد و پنجاه نفر بودند. | ۳۲ 32 |
Amenewa ndi Aisraeli monga mwa mabanja a makolo awo. Chiwerengero cha Aisraeli onse mʼmisasa chinali 603,550, mwa magulu awo.
اما لاویان چنانکه خداوند به موسیامر فرموده بود، در میان بنیاسرائیل شمرده نشدند. | ۳۳ 33 |
Koma Alevi sanawawerenge pamodzi ndi Aisraeli enawo monga momwe Yehova analamulira Mose.
و بنیاسرائیل موافق هرچه خداوند به موسیامر فرموده بود، عمل نمودند، به اینطورنزد علمهای خود خیمه میزدند و به اینطور هرکس برحسب قبایل خود با خاندان آبای خودکوچ میکردند. | ۳۴ 34 |
Choncho Aisraeli anachita zonse zomwe Yehova analamulira Mose. Umo ndi momwe amamangira misasa yawo pamene panali mbendera zawo, ndipo ankasamuka monga mwa mafuko a makolo awo.