< میکا 1 >
کلام خداوند که بر میکاه مورشتی در ایام یوتام و آحاز و حزقیا، پادشاهان یهودانازل شد و آن را درباره سامره و اورشلیم دید. | ۱ 1 |
Yehova anayankhula ndi Mika wa ku Moreseti pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda. Awa ndi masomphenya amene iye anaona onena za Samariya ndi Yerusalemu.
ای جمیع قومها بشنوید وای زمین و هرچه در آن است گوش بدهید، و خداوند یهوه یعنی خداوند از هیکل قدسش بر شما شاهد باشد. | ۲ 2 |
Tamverani, inu anthu a mitundu yonse, mvetsera iwe dziko lapansi ndi okhala mʼmenemo, pakuti Ambuye Yehova achitira umboni wokutsutsani, Ambuye akuyankhula ali mʼnyumba yake yopatulika.
زیرا اینک خداوند از مکان خود بیرون میآید ونزول نموده، بر مکان های بلند زمین میخرامد. | ۳ 3 |
Taonani! Yehova akubwera kuchokera ku malo ake; Iye akutsika ndipo akuponda pa malo okwera a dziko lapansi.
و کوهها زیر او گداخته میشود و وادیها منشق میگردد، مثل موم پیش آتش و مثل آب که به نشیب ریخته شود. | ۴ 4 |
Mapiri akusungunuka pansi pake, ndipo zigwa zikugawikana ngati phula pa moto, ngati madzi ochokera mʼphiri.
این همه بهسبب عصیان یعقوب و گناه خاندان اسرائیل است. عصیان یعقوب چیست؟ آیا سامره نیست؟ و مکان های بلند یهودا چیست؟ آیا اورشلیم نمی باشد؟ | ۵ 5 |
Zonsezi ndi chifukwa cha cholakwa cha Yakobo, chifukwa cha machimo a nyumba ya Israeli. Kodi cholakwa cha Yakobo nʼchiyani? Kodi si Samariya? Kodi malo achipembedzo a Yuda ndi ati? Kodi si Yerusalemu?
پس سامره را به توده سنگ صحرا و مکان غرس نمودن موها مبدل خواهم ساخت و سنگهایش رابه دره ریخته، بنیادش را منکشف خواهم نمود. | ۶ 6 |
“Choncho Ine ndidzasandutsa Samariya kukhala bwinja, malo odzalamo mphesa. Miyala yake ndidzayitaya ku chigwa ndipo ndidzafukula maziko ake.
و همه بتهای تراشیده شده آن خرد و همه مزدهایش به آتش سوخته خواهد شد و همه تماثیلش را خراب خواهم کرد زیرا که از مزدفاحشه آنها را جمع کرد و به مزد فاحشه خواهدبرگشت. | ۷ 7 |
Mafano ake onse ndidzawaphwanyaphwanya; mphatso zake zonse ndidzazitentha ndi moto; ndidzawononga zifanizo zonse za milungu yake. Popeza analandira mphatso zake kuchokera ku malipiro a akazi achiwerewere, mphatsozonso zidzagwiritsidwa ntchito ndi ena ngati malipiro a akazi achiwerewere.”
به این سبب ماتم گرفته، ولوله خواهم نمود و برهنه و عریان راه خواهم رفت و مثل شغالها ماتم خواهم گرفت و مانند شتر مرغها نوحه گری خواهم نمود. | ۸ 8 |
Chifukwa cha zimenezi ine ndidzalira momvetsa chisoni; ndidzayenda wopanda nsapato ndi wamaliseche. Ndidzafuwula ngati nkhandwe ndi kulira ngati kadzidzi.
زیرا که جراحت های وی علاج پذیر نیست چونکه به یهودا رسیده و به دروازه های قوم من یعنی به اورشلیم داخل گردیده است. | ۹ 9 |
Pakuti chilonda cha Samariya nʼchosachizika; chafika ku Yuda. Chafika pa chipata chenicheni cha anthu anga, mpaka mu Yerusalemu mwenimwenimo.
در جت خبر مرسانید و هرگز گریه منمایید. در خانه عفره، در غبار خویشتن راغلطانیدم. | ۱۰ 10 |
Musanene zimenezi ku Gati; musalire nʼkomwe. Mugubuduzike mu fumbi ku Beti-Leafura.
ای ساکنه شافیر عریان و خجل شده، بگذر. ساکنه صانان بیرون نمی آید. ماتم بیت ایصل مکانش را از شما میگیرد. | ۱۱ 11 |
Inu anthu okhala ku Safiro, muzipita ku ukapolo muli amaliseche ndi amanyazi. Iwo amene akukhala ku Zanaani sadzatuluka. Beti-Ezeli akulira mwachisoni; chitetezo chake chakuchokerani.
زیرا که ساکنه ماروت به جهت نیکویی درد زه میکشد، چونکه بلا از جانب خداوند به دروازه اورشلیم فرود آمده است. | ۱۲ 12 |
Anthu amene amakhala ku Maroti akubuwula ndi ululu, akuyembekezera thandizo, chifukwa Yehova wabweretsa tsoka, lafika mpaka pa chipata cha Yerusalemu.
ای ساکنه لاکیش اسب تندرورا به ارابه ببند. او ابتدای گناه دختر صهیون بود، چونکه عصیان اسرائیل در تو یافت شده است. | ۱۳ 13 |
Inu anthu okhala ku Lakisi mangani akavalo ku magaleta. Inu amene munayamba kuchimwitsa mwana wamkazi wa Ziyoni, pakuti zolakwa za Israeli zinapezeka pakati panu.
بنابراین طلاق نامهای به مورشت جت خواهی داد. خانه های اکذیب، چشمه فریبنده برای پادشاهان اسرائیل خواهد بود. | ۱۴ 14 |
Chifukwa chake perekani mphatso zolawirana ndi a ku Moreseti Gati. Mzinda wa Akizibu udzaonetsa kunama kwa mafumu a Israeli.
ای ساکنه مریشه بار دیگر مالکی بر تو خواهم آورد. جلال اسرائیل تا به عدلام خواهد آمد. | ۱۵ 15 |
Ndidzabweretsa mgonjetsi kudzalimbana ndi inu okhala mu Maresa. Ulemerero wa Israeli udzafika ku Adulamu.
خویشتن را برای فرزندان نازنین خود گر ساز وموی خود را بتراش. گری سر خود را مثل کرکس زیاد کن زیرا که ایشان از نزد تو به اسیری رفتهاند. | ۱۶ 16 |
Metani mipala mitu yanu kuonetsa kuti mukulirira ana anu amene mumawakonda; mudzichititse dazi ngati dembo, pakuti anawo adzatengedwa pakati panu kupita ku ukapolo.