< ایّوب 34 >

پس الیهو تکلم نموده، گفت: ۱ 1
Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
«ای حکیمان سخنان مرا بشنوید، و‌ای عارفان، به من گوش گیرید. ۲ 2
“Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
زیرا گوش، سخنان را امتحان می‌کند، چنانکه کام، طعام را ذوق می‌نماید. ۳ 3
Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
انصاف را برای خود اختیار کنیم، و درمیان خود نیکویی را بفهمیم. ۴ 4
Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
چونکه ایوب گفته است که بی‌گناه هستم. و خدا داد مرا از من برداشته است. ۵ 5
“Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
هرچند انصاف با من است دروغگو شمرده شده‌ام، و هرچند بی‌تقصیرم، جراحت من علاج ناپذیر است. ۶ 6
Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
کدام شخص مثل ایوب است که سخریه را مثل آب می‌نوشد ۷ 7
Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
که در رفاقت بدکاران سالک می‌شود، و با مردان شریر رفتار می‌نماید. ۸ 8
Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
زیرا گفته است انسان رافایده‌ای نیست که رضامندی خدا را بجوید. ۹ 9
Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
پس الان‌ای صاحبان فطانت مرا بشنوید، حاشااز خدا که بدی کند. و از قادرمطلق، که ظلم نماید. ۱۰ 10
“Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
زیرا که انسان را به حسب عملش مکافات می‌دهد، و بر هرکس موافق راهش می‌رساند. ۱۱ 11
Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
وبه درستی که خدا بدی نمی کند، و قادر مطلق انصاف را منحرف نمی سازد. ۱۲ 12
Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
کیست که زمین رابه او تفویض نموده، و کیست که تمامی ربع مسکون را به او سپرده باشد. ۱۳ 13
Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
اگر او دل خود رابه وی مشغول سازد، اگر روح و نفخه خویش رانزد خود بازگیرد، ۱۴ 14
Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
تمامی بشر با هم هلاک می‌شوند و انسان به خاک راجع می‌گردد. ۱۵ 15
zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
پس اگر فهم داری این را بشنو، و به آواز کلام من گوش ده. ۱۶ 16
“Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
آیا کسی‌که از انصاف نفرت دارد سلطنت خواهد نمود؟ و آیا عادل کبیر را به گناه اسنادمی دهی؟ ۱۷ 17
Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
آیا به پادشاه گفته می‌شود که لئیم هستی، یا به نجیبان که شریر می‌باشید؟ ۱۸ 18
Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
پس چگونه به آنکه امیران را طرفداری نمی نماید ودولتمند را بر فقیر ترجیح نمی دهد. زیرا که جمیع ایشان عمل دستهای وی‌اند. ۱۹ 19
Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
درلحظه‌ای در نصف شب می‌میرند. قوم مشوش شده، می‌گذرند، و زورآوران بی‌واسطه دست انسان هلاک می‌شوند. ۲۰ 20
Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
«زیرا چشمان او بر راههای انسان می‌باشد، و تمامی قدمهایش را می‌نگرد. ۲۱ 21
“Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
ظلمتی نیست و سایه موت نی، که خطاکاران خویشتن را درآن پنهان نمایند. ۲۲ 22
Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
زیرا اندک زمانی بر احدی تامل نمی کند تا او پیش خدا به محاکمه بیاید. ۲۳ 23
Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
زورآوران را بدون تفحص خرد می‌کند، ودیگران را به‌جای ایشان قرار می‌دهد. ۲۴ 24
Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
هرآینه اعمال ایشان را تشخیص می‌نماید، و شبانگاه ایشان را واژگون می‌سازد تا هلاک شوند. ۲۵ 25
Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
به‌جای شریران ایشان را می‌زند، در مکان نظرکنندگان. ۲۶ 26
Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
از آن جهت که از متابعت اومنحرف شدند، و در همه طریقهای وی تامل ننمودند. ۲۷ 27
Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
تا فریاد فقیر را به او برسانند، و اوفغان مسکینان را بشنود. ۲۸ 28
Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
چون او آرامی دهدکیست که در اضطراب اندازد، و چون روی خودرا بپوشاند کیست که او را تواند دید. خواه به امتی خواه به انسانی مساوی است، ۲۹ 29
Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
تا مردمان فاجرسلطنت ننمایند و قوم را به دام گرفتار نسازند. ۳۰ 30
kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
لیکن آیا کسی هست که به خدا بگوید: سزایافتم، دیگر عصیان نخواهم ورزید. ۳۱ 31
“Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
و آنچه راکه نمی بینم تو به من بیاموز، و اگر گناه کردم باردیگر نخواهم نمود. ۳۲ 32
ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
آیا برحسب رای تو جزاداده، خواهد گفت: چونکه تو رد می‌کنی پس تواختیار کن و نه من. و آنچه صواب می‌دانی بگو. ۳۳ 33
Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
صاحبان فطانت به من خواهند گفت، بلکه هرمرد حکیمی که مرا می‌شنود ۳۴ 34
“Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
که ایوب بدون معرفت حرف می‌زند و کلام او از روی تعقل نیست. ۳۵ 35
‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
کاش که ایوب تا به آخر آزموده شود، زیرا که مثل شریران جواب می‌دهد. ۳۶ 36
Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
چونکه برگناه خود طغیان را مزید می‌کند و در میان مادستک می‌زند و به ضد خدا سخنان بسیارمی گوید.» ۳۷ 37
Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”

< ایّوب 34 >