< خروج 21 >
«و این است احکامی که پیش ایشان می گذاری: | ۱ 1 |
“Uwawuze Aisraeli malamulo awa:
اگر غلام عبری بخری، شش سال خدمت کند، و در هفتمین، بیقیمت، آزاد بیرون رود. | ۲ 2 |
“Mukagula kapolo wa Chihebri, azikugwirirani ntchito zaka zisanu ndi chimodzi. Koma mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri muzimumasula, ndipo asalipire kanthu.
اگر تنها آمده، تنها بیرون رود. واگر صاحب زن بوده، زنش همراه او بیرون رود. | ۳ 3 |
Ngati anabwera yekha, amasulidwenso yekha. Koma ngati anali ndi mkazi pamene ankabwera, mkaziyo apite nayenso.
اگر آقایش زنی بدو دهد و پسران یا دختران برایش بزاید، آنگاه زن و اولادش از آن آقایش باشند، و آن مرد تنها بیرون رود. | ۴ 4 |
Ngati bwana wake amupatsa mkazi ndipo mkaziyo anabereka ana aamuna kapena aakazi, mkazi ndi anawo adzakhala a bwanayo ndipo mwamuna yekhayo ndiye adzamasulidwe.
لیکن هرگاه آن غلام بگوید که هرآینه آقایم و زن و فرزندان خودرا دوست میدارم و نمی خواهم که آزاد بیرون روم، | ۵ 5 |
“Koma ngati kapoloyo alengeza kuti, ‘Ine sindikufuna kumasulidwa chifukwa ndimakonda mbuye wanga, mkazi wanga ndi ana,’
آنگاه آقایش او را به حضور خدا بیاورد، واو را نزدیک در یا قایمه در برساند، و آقایش گوش او را با درفشی سوراخ کند، و او وی راهمیشه بندگی نماید. | ۶ 6 |
mbuye wakeyo abwere naye kwa Yehova. Abwere naye pa chitseko kapena pa mphuthu zachitseko ndipo abowole khutu lake ndi chitsulo. Ndipo iye adzakhala kapolo wake moyo wake wonse.
اما اگر شخصی، دخترخود را به کنیزی بفروشد، مثل غلامان بیرون نرود. | ۷ 7 |
“Ngati munthu agulitsa mwana wake wamkazi kukhala mdzakazi, mwanayo asamasulidwe monga achitira ndi akapolo aamuna.
هر گاه به نظر آقایش که او را برای خودنامزد کرده است ناپسند آید، بگذارد که او را فدیه دهند، اما هیچ حق ندارد که او را به قوم بیگانه بفروشد، زیرا که بدو خیانت کرده است. | ۸ 8 |
Koma ngati mkaziyo sakukondweretsa bwana wake amene wamusankha kuti amukwatire, amulole kuti awomboledwe. Bwanayo alibe mphamvu zomugulitsa kwa anthu achilendo, chifukwa iyeyo waphwanya pangano lake lomukwatira iye.
و هرگاه او را به پسر خود نامزد کند، موافق رسم دختران بااو عمل نماید. | ۹ 9 |
Ngati anamusankha kuti akhale mkazi wa mwana wake, ayenera kumusunga ngati mwana wake wamkazi.
اگر زنی دیگر برای خود گیرد، آنگاه خوراک و لباس و مباشرت او را کم نکند. | ۱۰ 10 |
Ngati akwatira mkazi wina, asamumane woyambayo chakudya ngakhale chovala ndipo apiritirize kugona naye ngati mkazi wake.
و اگر این سه چیز را برای او نکند، آنگاه بیقیمت و رایگان بیرون رود. | ۱۱ 11 |
Koma ngati sangathe kumuchitira zonsezi, ndiye amuleke apite popanda kulipira kanthu.
«هرکه انسانی را بزند و او بمیرد، هر آینه کشته شود. | ۱۲ 12 |
“Munthu aliyense amene amenya mnzake namupha, iyenso ayenera kuphedwa.
اما اگر قصد او نداشت، بلکه خداوی را بدستش رسانید، آنگاه مکانی برای تو معین کنم تا بدانجا فرار کند. | ۱۳ 13 |
Koma ngati sanachite dala, ndipo Mulungu analola kuti zichitike, iyeyo athawire ku malo kumene ndidzakupatsani.
لیکن اگر شخصی عمد بر همسایه خود آید، تا او را به مکر بکشد، آنگاه او را از مذبح من کشیده، به قتل برسان. | ۱۴ 14 |
Koma ngati munthu akonza chiwembu ndi kupha mnzake mwadala, ameneyo muchotseni ngakhale ku guwa langa lansembe ndipo aphedwe.
و هرکه پدر یا مادر خود را زند، هرآینه کشته شود. | ۱۵ 15 |
“Munthu aliyense amene amenya abambo ake kapena mayi ake ayenera kuphedwa.
وهرکه آدمی را بدزدد و او را بفروشد یا در دستش یافت شود، هرآینه کشته شود. | ۱۶ 16 |
“Munthu aliyense amene aba munthu mnzake, ndi kukamugulitsa, kapena kumangomusunga, ayenera kuphedwa.
و هرکه پدر یامادر خود را لعنت کند، هرآینه کشته شود. | ۱۷ 17 |
“Aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa.
واگر دو مرد نزاع کنند، و یکی دیگری را به سنگ یابه مشت زند، و او نمیرد لیکن بستری شود، | ۱۸ 18 |
“Ngati anthu awiri akangana ndipo wina amenya mnzake ndi mwala kapena nkhonya koma wosamupha, womenyedwayo akadwala nagona pa bedi,
اگربرخیزد و با عصا بیرون رود، آنگاه زننده او بیگناه شمرده شود، اما عوض بیکاریش را ادا نماید، وخرج معالجه او را بدهد. | ۱۹ 19 |
kenaka nachira ndi kuyamba kuyenda ndi ndodo kutuluka kunja kwa nyumba yake, ndiye kuti womenya mnzakeyo sadzayimbidwa mlandu. Komabe adzayenera kulipira womenyedwayo chifukwa cha nthawi imene anagona pa bedi ija, ndiponso ayenera kumusala mpaka atachiritsitsa.
و اگر کسی غلام یاکنیز خود را به عصا بزند، و او زیر دست او بمیرد، هرآینه انتقام او گرفته شود. | ۲۰ 20 |
“Ngati munthu amenya kapolo wake wamwamuna kapena mdzakazi ndi ndodo, kapolo uja ndikufa chifukwa cha kumenyedwako, munthuyo ayenera kulangidwa.
لیکن اگر یک دوروز زنده بماند، از او انتقام کشیده نشود، زیرا که زرخرید اوست. | ۲۱ 21 |
Koma ngati kapolo uja akhala ndi moyo tsiku lonse kapena masiku awiri, ndiye kuti mbuye uja asalangidwe chifukwa kapolo ndi chuma chake.
و اگر مردم جنگ کنند، و زنی حامله را بزنند، و اولاد او سقط گردد، و ضرری دیگر نشود، البته غرامتی بدهد موافق آنچه شوهرزن بدو گذارد، و به حضور داوران ادا نماید. | ۲۲ 22 |
“Ngati anthu akumenyana ndi kupweteka mayi woyembekezera, mayiyo napita padera, koma osavulala, wolakwayo ayenera kulipira chilichonse chimene mwamuna wake wa mkaziyo adzalamula ndipo bwalo lamilandu lavomereza.
واگر اذیتی دیگر حاصل شود، آنگاه جان به عوض جان بده. | ۲۳ 23 |
Koma ngati wavulazidwa kwambiri, ndiye malipiro ake adzakhala motere: moyo kulipa moyo,
و چشم به عوض چشم، و دندان به عوض دندان، و دست به عوض دست، و پا به عوض پا. | ۲۴ 24 |
diso kulipira diso, dzino kulipira dzino, mkono kulipa mkono, phazi kulipa phazi.
و داغ به عوض داغ، و زخم به عوض زخم، و لطمه به عوض لطمه. | ۲۵ 25 |
Kutentha ndi moto kulipa kutentha ndi moto, bala kulipa bala, mkwingwirima kulipa mkwingwirima.
و اگر کسی چشم غلام یا چشم کنیز خود را بزند که ضایع شود، او را به عوض چشمش آزاد کند. | ۲۶ 26 |
“Ngati munthu amenya wantchito wake wa mwamuna kapena mdzakazi wake pa diso ndi kuliwononga, wantchitoyo amasulidwe ngati malipiro a diso lake.
و اگردندان غلام یا دندان کنیز خود را بیندازد او را به عوض دندانش آزاد کند. | ۲۷ 27 |
Ndipo ngati agulula dzino la wantchito wamwamuna kapena mdzakazi, wantchitoyo amasulidwe ngati malipiro a dzino lake.
و هرگاه گاوی به شاخ خود مردی یا زنی را بزند که او بمیرد، گاو را البته سنگسار کنند، و گوشتش را نخورند و صاحب گاو بیگناه باشد. | ۲۸ 28 |
“Ngati ngʼombe ipha munthu wamwamuna kapena wamkazi ndi nyanga yake, iponyedwe miyala ndipo nyama yake isadyedwe. Ndipo mwini ngʼombeyo asayimbidwe mlandu.
و لیکن اگر گاو قبل از آن شاخ زن میبود، و صاحبش آگاه بود، و آن را نگاه نداشت، و او مردی یا زنی را کشت، گاو راسنگسار کنند، و صاحبش را نیز به قتل رسانند. | ۲۹ 29 |
Koma ngati ngʼombeyo inali ndi chizolowezi chogunda anthu ndipo mwini wakeyo anachenjezedwa koma iye sanayimange ndipo yapha mwamuna kapena mkazi, ngʼombeyo iponyedwe miyala ndipo mwini wakeyo aphedwenso.
و اگر دیه بر او گذاشته شود، آنگاه برای فدیه جان خود هرآنچه بر او مقرر شود، ادا نماید. | ۳۰ 30 |
Koma ngati wauzidwa kuti alipire, iye apereke zimene wauzidwazo kuti awombole moyo wake.
خواه پسر خواه دختر را شاخ زده باشد، به حسب این حکم با او عمل کنند. | ۳۱ 31 |
Lamulo ili ligwirenso ntchito ngati ngʼombeyo yagunda mwana wamwamuna kapena wamkazi.
اگر گاو، غلامی یا کنیزی را بزند، سی مثقال نقره به صاحب او داده شود، و گاو سنگسار شود. | ۳۲ 32 |
Ngati ngʼombeyo yagunda kapolo wamwamuna kapena mdzakazi, mwini ngʼombeyo apereke masekeli makumi atatu a siliva kwa mwini kapoloyo, ndipo ngʼombeyo iponyedwe miyala.
واگر کسی چاهی گشاید یا کسی چاهی حفر کند، وآن را نپوشاند، و گاوی یا الاغی در آن افتد، | ۳۳ 33 |
“Munthu akasiya dzenje lapululu kapena akakumba dzenje koma wosaphimbapo, ndipo ngʼombe kapena bulu nʼkugweramo,
صاحب چاه عوض او را بدهد، و قیمتش را به صاحبش ادا نماید، و میته از آن او باشد. | ۳۴ 34 |
mwini dzenjelo amulipire mwini chiweto chakufacho koma iye atenge chiwetocho.
و اگرگاو شخصی، گاو همسایه او را بزند، و آن بمیردپس گاو زنده را بفروشند، و قیمت آن را تقسیم کنند، و میته را نیز تقسیم نمایند، | ۳۵ 35 |
“Ngati ngʼombe ya munthu wina ipha ngʼombe ya mnzake, ngʼombe yamoyo ija igulitsidwe ndipo anthu awiriwo agawane pakati ndalama yake. Achite chimodzimodzi ndi ngʼombe yakufa ija.
اما اگر معلوم بوده باشد که آن گاو قبل از آن شاخ زن میبود، وصاحبش آن را نگاه نداشت، البته گاو به عوض گاو بدهد و میته از آن او باشد. | ۳۶ 36 |
Koma zikadziwika kuti ngʼombeyo inali ndi khalidwe logunda, ndipo mwini wake samayitsekera mʼkhola, mwini ngʼombeyo alipire ngʼombe ina yamoyo koma atenge yakufayo.”