< تثنیه 11 >
پس یهوه خدای خود را دوست بدار، وودیعت و فرایض و احکام و اوامر او رادر همه وقت نگاهدار. | ۱ 1 |
Muzikonda Yehova Mulungu wanu ndipo nthawi zonse muzitsata zimene Iyeyo anakulamulani, malangizo, zikhazikitso ndi malamulo ake.
و امروز بدانید، زیرا که به پسران شما سخن نمی گویم که ندانستهاند، وتادیب یهوه خدای شما را ندیدهاند، و نه عظمت و دست قوی و بازوی افراشته او را. | ۲ 2 |
Lero kumbukirani kuti si ana anu amene anaona ndi kulawa chilango cha Yehova Mulungu wanu: ukulu wake, dzanja lake lamphamvu, mkono wake wotambasuka;
و آیات واعمال او را که در میان مصر، به فرعون، پادشاه مصر، و به تمامی زمین او بظهور آورد. | ۳ 3 |
zizindikiro zozizwitsa zimene anazionetsa ndi zinthu zimene anazichita mʼkati mwa Igupto, Farao mfumu ya Igupto ndi kwa dziko lake lonse;
و آنچه راکه به لشکر مصریان، به اسبها و به ارابه های ایشان کرد، که چگونه آب بحر قلزم را برایشان جاری ساخت، وقتی که شما را تعاقب مینمودند، وچگونه خداوند، ایشان را تا به امروز هلاک ساخت. | ۴ 4 |
zimene Iye anachita kwa gulu lankhondo la Aigupto, kwa akavalo ndi magaleta awo, mmene Iye anawamizira ndi madzi a mu Nyanja Yofiira pamene amakuthamangitsani, ndi mmene Yehova anawagonjetsera kufikira lero.
و آنچه را که برای شما در بیابان کرد تاشما به اینجا رسیدید. | ۵ 5 |
Si ana anu amene anaona zimene Iye anakuchitirani mʼchipululu kufikira pamene munafika pa malo anu,
و آنچه را که به داتان و ابیرام پسران الیاب بن روبین کرد، که چگونه زمین دهان خود را گشوده، ایشان را و خاندان وخیمه های ایشان را، و هر ذی حیات را که همراه ایشان بود در میان تمامی اسرائیل بلعید. | ۶ 6 |
ndi zimene anachitira Datani ndi Abiramu, ana aamuna a Eliabu mwana wa Rubeni, pamene nthaka inatsekula pakamwa pake pakati pa Aisraeli onse ndi kuwameza pamodzi ndi katundu wawo, matenti awo ndi chilichonse chawo.
لیکن چشمان شما تمامی اعمال عظیمه خداوند را که کرده بود، دیدند. | ۷ 7 |
Koma ndinuyo amene munaona ntchito zonse zikuluzikulu zimenezi Yehova anakuchitirani.
پس جمیع اوامری را که من امروز برای شماامر میفرمایم نگاه دارید، تا قوی شوید و داخل شده، زمینی را که برای گرفتن آن عبور میکنید، به تصرف آورید. | ۸ 8 |
Tsono muzisunga malamulo onse amene ndikukupatsani lero kuti mukhale ndi mphamvu ndi kuti mupite kukalanda mʼdziko limene mwakhala pangʼono kulowamo mukawoloka Yorodani,
و تا در آن زمینی که خداوندبرای پدران شما قسم خورد که آن را به ایشان وذریت ایشان بدهد، عمر دراز داشته باشید، زمینی که به شیر و شهد جاری است. | ۹ 9 |
ndiponso kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova analumbira kupatsa makolo anu ndi zidzukulu zawo, lomwe ndi dziko loyenda mkaka ndi uchi.
زیرا زمینی که تو برای گرفتن آن داخل میشوی، مثل زمین مصرکه از آن بیرون آمدی نیست، که در آن تخم خودرا میکاشتی و آن را مثل باغ بقول به پای خودسیراب میکردی. | ۱۰ 10 |
Dziko limene mukukalanda ndi kulowamo silokhala ngati dziko la ku Igupto kumene mukuchokera ayi, kuja mumadzala mbewu ndi kumathirira ndi mapazi anu ngati ku dimba.
لیکن زمینی که شما برای گرفتنش به آن عبور میکنید، زمین کوهها ودره هاست که از بارش آسمان آب مینوشد، | ۱۱ 11 |
Koma dziko limene mukalande mukawoloka Yorodani ndi dziko la mapiri ndi zigwa, dziko limene limalandira mvula kuchokera kumwamba.
زمینی است که یهوه خدایت برآن التفات داردو چشمان یهوه خدایت از اول سال تا آخر سال پیوسته بر آن است. | ۱۲ 12 |
Ili ndi dziko limene Yehova Mulungu wanu amalisamalira. Maso a Yehova Mulungu wanu amaliyangʼanira nthawi zonse kuchokera ku mayambiriro a chaka mpaka kumapeto kwake.
و چنین خواهد شد که اگر اوامری را که من امروز برای شما امر میفرمایم، بشنوید، و یهوه خدای خود را دوست بدارید، و او را به تمامی دل و به تمامی جان خود عبادت نمایید، | ۱۳ 13 |
Choncho mukasunga mokhulupirika malamulo amene ndikukupatsani lero lino, kukonda Yehova Mulungu wanu ndi kumutumikira Iyeyo ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse,
آنگاه باران زمین شما یعنی باران اولین و آخرین را درموسمش خواهم بخشید، تا غله و شیره و روغن خود را جمع نمایی. | ۱۴ 14 |
pamenepo ndidzatumiza mvula mʼdziko mwanu pa nthawi yake mʼnyengo ya dzinja ndi chilimwe, kuti mudzakolole tirigu wambiri ndi kuti mudzakhale ndi vinyo watsopano ndi mafuta.
و در صحرای تو برای بهایمت علف خواهم داد تا بخوری و سیر شوی. | ۱۵ 15 |
Ndidzakupatsani udzu mʼminda mwanu woti muzidzadyetsera ngʼombe zanu ndipo inuyo mudzadya ndi kukhuta.
باحذر باشید مبادا دل شما فریفته شود وبرگشته، خدایان دیگر را عبادت و سجده نمایید. | ۱۶ 16 |
Dzisamalireni nokha, kuopa kuti mungakopeke mtima ndi kubwerera mʼmbuyo kuyamba kutumikira milungu ina ndi kumayigwadira.
و خشم خداوند برشما افروخته شود، تاآسمان را مسدود سازد، و باران نبارد، و زمین محصول خود را ندهد و شما از زمین نیکویی که خداوند به شما میدهد، بزودی هلاک شوید. | ۱۷ 17 |
Mukatero Yehova Mulungu wanu adzakukwiyirani kwambiri, nadzaletsa thambo kuti lisabweretsenso mvula ndipo dziko silidzapereka zokolola. Choncho mudzawonongeka msanga mʼdziko limene Yehova akukupatsani.
پس این سخنان مرا در دل و جان خود جادهید، و آنها را بر دستهای خود برای علامت ببندید، و در میان چشمان شما عصابه باشد. | ۱۸ 18 |
Sungani mawu amenewa mu mtima mwanu ndi mʼmaganizo mwanu, muwamangirire pa mikono yanu ndipo muwayike pamphumi panu.
وآنها را به پسران خود تعلیم دهید، و حین نشستنت در خانه خود، و رفتنت به راه، و وقت خوابیدن و برخاستنت از آنها گفتگو نمایید. | ۱۹ 19 |
Mawuwa muziphunzitsa ana anu, muzikamba za iwo pamene mukhala pansi mʼnyumba zanu, pamene mukuyenda mʼnjira, pamene mugona ndi pamene mukudzuka.
وآنها را بر باهوهای در خانه خود و بر دروازه های خود بنویسید. | ۲۰ 20 |
Muwalembe pa mphuthu za nyumba zanu ndi pa zipata zanu,
تا ایام شما و ایام پسران شما برزمینی که خداوند برای پدران شما قسم خورد که به ایشان بدهد، کثیر شود، مثل ایام افلاک بر بالای زمین. | ۲۱ 21 |
kuti inu ndi ana anu mukhale mʼdziko limene Yehova analumbira kupatsa makolo anu mpaka kalekale monga umakhalira mlengalenga pamwamba pa dziko.
زیرا اگر تمامی این اوامر را که من به جهت عمل نمودن به شما امر میفرمایم، نیکو نگاه دارید، تا یهوه خدای خود را دوست دارید، و درتمامی طریقهای او رفتار نموده، به او ملصق شوید، | ۲۲ 22 |
Mukatsatira mosamalitsa malamulo amene ndikukupatsaniwa, kukonda Yehova Mulungu wanu, kuyenda mʼnjira zake zonse ndi kumugwiritsitsa Iye
آنگاه خداوند جمیع این امتها را ازحضور شما اخراج خواهد نمود، و شما امتهای بزرگتر و قویتر از خود را تسخیر خواهید نمود. | ۲۳ 23 |
Yehova adzapirikitsa mitundu ina yonseyi inu musanafike ndipo mudzagonjetsa mitundu ikuluikulu ndi yamphamvu kuposa inu.
هرجایی که کف پای شما برآن گذارده شود، ازآن شما خواهد بود، از بیابان و لبنان و از نهر، یعنی نهر فرات تا دریای غربی، حدود شماخواهد بود. | ۲۴ 24 |
Malo aliwonse amene mudzaponda adzakhala anu: dziko lanu lidzachokera ku chipululu mpaka ku Lebanoni, ndi ku Mtsinje wa Yufurate mpaka ku nyanja ya kumadzulo.
و هیچکس یارای مقاومت با شمانخواهد داشت، زیرا یهوه خدای شما ترس و خوف شما را بر تمامی زمین که به آن قدم میزنیدمستولی خواهد ساخت، چنانکه به شما گفته است. | ۲۵ 25 |
Palibe munthu amene adzalimbana nanu. Monga analonjezera, Yehova adzachititsa kuti anthu onse mʼdziko limene mukupitalo adzachite nanu mantha ndi kukuopani.
اینک من امروز برکت و لعنت پیش شمامی گذارم. | ۲۶ 26 |
Taonani, lero ndikuyika dalitso ndi temberero pakati panu,
اما برکت، اگر اوامر یهوه خدای خود را که من امروز به شما امر میفرمایم، اطاعت نمایید. | ۲۷ 27 |
dalitso ngati mumvera malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero.
و اما لعنت، اگر اوامر یهوه خدای خودرا اطاعت ننموده، از طریقی که من امروز به شماامر میفرمایم برگردید، و خدایان غیر را که نشناختهاید، پیروی نمایید. | ۲۸ 28 |
Temberero ngati simumvera malamulo a Yehova Mulungu wanu ndi kupatuka pa njira imene ndikulamulirani lero potsata milungu ina imene simunayidziwe.
و واقع خواهد شدکه چون یهوه، خدایت، تو را به زمینی که به جهت گرفتنش به آن میروی داخل سازد، آنگاه برکت را بر کوه جرزیم و لعنت را بر کوه ایبال خواهی گذاشت. | ۲۹ 29 |
Yehova Mulungu wanu akakakufikitsani mʼdziko mukukalandalo kuti mulowemo mukanene za madalitso pa Phiri la Gerizimu, ndi za matemberero pa Phiri la Ebala.
آیا آنها به آنطرف اردن نیستند پشت راه غروب آفتاب، در زمین کنعانیانی که در عربه ساکنند مقابل جلجال نزد بلوطهای موره. | ۳۰ 30 |
Monga mudziwa, mapiriwa ali kutsidya kwa Yorodani, kumadzulo kolowera dzuwa, kufupi ndi mitengo ya thundu ya More, mʼdziko la Akanaani aja okhala ku Araba moyangʼanana ndi Giligala.
زیرا که شما از اردن عبور میکنید تا داخل شده، زمینی را که یهوه خدایت به تو میبخشد به تصرف آورید، و آن را خواهید گرفت و در آن ساکن خواهید شد. | ۳۱ 31 |
Mwatsala pangʼono kuwoloka Yorodani kuti mulowe ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani. Mukadzalitenga dzikolo ndi kukhalamo,
پس متوجه باشید تا جمیع این فرایض و احکامی را که من امروز پیش شمامی گذارم، به عمل آورید. | ۳۲ 32 |
mudzaonetsetse kuti mukumvera malangizo ndi malamulo amene ndikukuwuzani lero.