< Salmenes 66 >

1 Til songmeisteren; ein song, ein salme. Ropa fagnadrop for Gud, all jordi!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
2 Syng ut hans namns æra, gjev honom æra til hans pris!
Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
3 Seg til Gud: «Kor skræmelege dine verk er! For di store magt skuld må dine fiendar gjøla for deg.
Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
4 All jordi skal tilbeda deg og syngja deg lov, dei skal syngja um ditt namn.» (Sela)
Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
5 Kom og sjå Guds gjerningar! Skræmeleg er han i gjerning mot menneskjeborni.
Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
6 Han gjorde havet um til turrlende, gjenom elvi gjekk dei til fots; der gledde me oss i honom.
Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
7 Han råder med sitt velde æveleg, hans augo gjæter heidningarne; dei tråssuge må ikkje upphøgja seg. (Sela)
Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
8 De folk, lova vår Gud, og lat røysti av hans lovsong verta høyrd!
Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
9 han som heldt vår sjæl i live, og ikkje let vår fot vera ustød.
Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
10 For du prøvde oss, Gud, du reinsa oss, som dei reinsar sylv.
Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
11 Du førde oss inn i eit garn, du lagde ei tyngjande byrd på våre lender.
Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
12 Du let menneskje fara yver vårt hovud, me kom i eld og vatn - men du førde oss ut til uppkveikjing.
Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
13 Eg vil ganga inn i ditt hus med brennoffer; eg vil gjeva deg det eg hev lova,
Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
14 det som gjekk yver mine lippor, og som munnen min tala ut då eg var i naud.
Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
15 Brennoffer av feite sauer vil eg ofra til deg med eim av verar, eg vil ofra både uksar og bukkar. (Sela)
Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
16 Kom og høyr, so vil eg fortelja, alle de som ottast Gud, kva han hev gjort for mi sjæl.
Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
17 Til honom ropa eg med min munn, og lovsong var på tunga mi.
Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
18 Hadde eg stila på urett i mitt hjarta, vilde Herren ikkje høyra.
Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
19 Men Gud hev høyrt, han lydde på mi bønerøyst.
koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
20 Lova vere Gud, som ikkje viste mi bøn ifrå seg og ikkje tok frå meg si miskunn!
Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!

< Salmenes 66 >