< Salmenes 44 >

1 Til songmeisteren; av Korahs born; ein salme til lærdom. Gud, me hev høyrt med våre øyro, våre feder hev fortalt oss den gjerning du gjorde i deira dagar, i forne dagar.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu; makolo athu atiwuza zimene munachita mʼmasiku awo, masiku akalekalewo.
2 Du dreiv ut heidningarne med di hand, men deim planta du; du øydelagde folkeslag, men deim breidde du ut.
Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena ndi kudzala makolo athu; Inu munakantha mitundu ya anthu, koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
3 For ikkje med sitt sverd vann dei landet, og deira arm gav deim ikkje siger, men di høgre hand og din arm og ditt andlits ljos; for du hadde hugnad i deim.
Sanalande dziko ndi lupanga lawo, si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso, koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu, pakuti munawakonda.
4 Du, Gud, er min konge; byd at Jakob skal verta frelst!
Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
5 Ved deg skal me støyta ned våre fiendar, ved ditt namn skal me treda under føter deim som reiser seg imot oss.
Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu; kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
6 For min boge lit eg ikkje på, og mitt sverd gjev meg ikkje siger.
Sindidalira uta wanga, lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
7 Men du gjev oss siger yver våre fiendar, og deim som hatar oss, gjer du til skammar.
koma Inu mumatigonjetsera adani athu, mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
8 Av Gud rosar me oss all dagen og lovar ditt namn til æveleg tid. (Sela)
Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse, ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.
9 Og endå hev du støytt oss burt og gjort oss til skam, og du dreg ikkje ut med våre herar.
Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa; Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
10 Du let oss vika attende for fienden, og dei som hatar oss, fær seg herfang.
Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
11 Du gjev oss burt som sauer til å eta upp, og spreider oss ikring millom heidningarne.
Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
12 Du sel ditt folk for ingen ting, og ikkje set du høg pris på deim.
Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika, osapindulapo kanthu pa malondawo.
13 Du gjer oss til hæding for våre grannar, til spott og spe for deim som bur ikring oss.
Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina, chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
14 Du gjer oss til eit ordtøke millom heidningarne; dei rister på hovudet åt oss millom folki.
Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina; anthu amapukusa mitu yawo akationa.
15 Heile dagen stend mi skam for mine augo, og blygsl breider seg yver mitt andlit,
Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
16 ved røysti av spottaren og hædaren, ved syni av fienden og den hemngiruge.
chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe, chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.
17 Alt dette er kome yver oss, endå me ikkje hev gløymt deg og ikkje svike di pakt.
Zonsezi zinatichitikira ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
18 Vårt hjarta veik ikkje frå deg, og våre stig sveiv ikkje ut av din veg,
Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo; mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
19 at du skulde slå oss sund der sjakalar bur, og breida oss ned i daudeskugge.
Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.
20 Hadde me gløymt vår Guds namn og rett våre hender ut til ein framand gud,
Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
21 skulde Gud då ikkje ransaka det? for han kjenner hjartans løyndomar.
kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi, pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
22 Men for di skuld vert me drepne all dagen, me er rekna som slagtesauer.
Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse, tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.
23 Vakna upp! Kvi søv du, Herre? Vakna då, støyt ikkje burt for alltid!
Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona! Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
24 Kvi løyner du di åsyn, gløymer vår armodsdom og vår trengsla?
Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu, ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?
25 For vår sjæl er nedbøygd i moldi, vår likam nedtrykt til jordi.
Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi; matupi athu amatirira pa dothi.
26 Statt upp til hjelp for oss, og løys oss ut for din nåde skuld!
Imirirani ndi kutithandiza, tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.

< Salmenes 44 >