< Jobs 21 >
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 «Å høyr då, høyr på mine ord! Gjev i minsto det til trøyst!
“Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
3 Lat meg få lov å tala ut, so kann du spotta etterpå.
Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
4 Klagar eg vel på menneskje? Og hev eg ikkje grunn til harm?
“Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
5 Vend dykk til meg, og ottast so; legg handi so på dykkar munn.
Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
6 Eg støkk, når eg det kjem i hug; ei bivring gjenom kroppen gjeng.
Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
7 Kvifor fær dei gudlause liva, auka i magt som åri gjeng?
Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
8 Dei ser si ætt stå fast ikring deim, dei hev sitt avkjøme for augo.
Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
9 I fred stend husi deira trygge, Guds svipa råkar ikkje deim;
Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
10 med heppa parast deira fe, og kyrne kastar aldri kalv.
Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
11 Dei slepper borni ut som lamb, og gutarne i leiken hoppar;
Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
12 Dei syng til trumma og til cither og frygdar seg ved fløyteljod.
Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
13 I lukka liver dei si tid og fer so brått til helheim ned. (Sheol )
Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol )
14 Til Gud dei segjer: «Haldt deg burte!» Me vil’kje kjenna dine vegar!
Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
15 Kvi skal me tena den Allsterke? Kva gagnar det å be til honom?»
Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
16 «Dei hev’kje lukka si i handi» - Langt burt frå meg med gudlaus råd!
Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
17 Når sloknar lampa for gudlause? Når kjem ulukka yver deim? Gjev han deim straff i vreidesmod?
“Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
18 Fer dei vel burt som strå for vind, lik agner som i stormen fyk?
Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
19 «Gud gøymer straffi til hans born.» Nei, sjølv skal mannen straffi kjenna!
Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
20 Lat han få sjå sitt eige fall og drikka harm frå den Allsterke!
Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
21 Kva bryr han seg vel um sitt hus, når månadstalet hans er fullt?
Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
22 Vil nokon hjelpa Gud til kunnskap, han som er domar for dei høgste?
“Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
23 Den eine døyr på velmagts høgd, fullkomleg trygg og fredeleg;
Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
24 hans fat er fulle utav mjølk, og i hans bein er mergen frisk;
thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
25 den andre døyr so beisk i hug, hev ingenting av lukka smaka.
Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
26 Dei båe vert i moldi lagde, og deira klednad makkar er.
Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
27 Sjå kor eg kjennar dykkar tankar, og dykkar meinkrokar mot meg.
“Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
28 De spør: «Kvar er vel stormannshuset? Kvar er det tjeld der gudlause bur?»
Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
29 Hev de’kje høyrt av ferdafolk - de trur vel det som dei fortel -:
Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
30 «Den vonde frå ulukka slepp; han berga vert på vreidedagen.
Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
31 Kven lastar honom for hans ferd? Og straffar honom for hans gjerd?
Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
32 Han vert til gravi båren burt, og ved hans gravhaug held dei vakt.
Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
33 Søtt søv han under torv i dal, og i hans far all verdi fer, som tallause gjekk fyre honom.
Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
34 Det trøystar meg med tome ord; av dykkar svar er sviket att.»
“Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”