< Sakarias 7 >

1 Så var det i kong Darius' fjerde år, da kom Herrens ord til Sakarias på den fjerde dag i den niende måned, i måneden kislev.
Pa chaka chachinayi cha Mfumu Dariyo, pa tsiku lachinayi la Kisilevi, mwezi wachisanu ndi chinayi, Yehova anayankhula ndi Zekariya.
2 For Betel hadde sendt Sareser og Regem-Melek og hans menn for å bønnfalle Herren
Anthu a ku Beteli anali atatuma Sarezeri ndi Regemu-Meleki pamodzi ndi anthu awo, kuti akapemphe chifundo kwa Yehova
3 og spørre prestene i Herrens, hærskarenes Guds hus og profetene: Skal vi gråte og faste i den femte måned, som vi nu har gjort i så mange år?
pokafunsa kwa ansembe a ku Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse ndi aneneri kuti, “Kodi ine ndizilira ndi kusala zakudya pa mwezi wachisanu, monga mmene ndakhala ndikuchitira pa zaka zambiri?”
4 Da kom Herrens, hærskarenes Guds ord til mig, og det lød så:
Pamenepo Yehova Wamphamvuzonse anayankhula nane kuti,
5 Si til alt folket i landet og til prestene: Når I har fastet og klaget i den femte og i den syvende måned, og det nu i sytti år, er det da for min skyld I har fastet?
“Funsa anthu onse a mʼdziko ndi ansembe kuti, ‘Pamene munkasala zakudya pa mwezi wachisanu ndi wachisanu ndi chiwiri pa zaka 70 zapitazi, kodi munkasala chifukwa cha Ine?
6 Og når I eter og drikker, er det da ikke I selv som eter, og I selv som drikker?
Ndipo pamene munkadya ndi kumwa, kodi simunkachita zimenezi podzisangalatsa nokha?
7 Minnes I ikke de ord Herren lot utrope ved de forrige profeter, da Jerusalem lå der i ro og fred med sine byer rundt om, og likeså sydlandet og lavlandet?
Kodi awa si mawu amene Yehova ankanena kudzera mwa aneneri oyamba aja pamene Yerusalemu ndi mizinda yake yozungulira anali pa mtendere ndi pa ulemerero, ndi pamene Negevi ndi ku madera akumadzulo a mʼmbali mwa phiri munali anthu?’”
8 Og Herrens ord kom til Sakarias, og det lød så:
Ndipo Yehova anayankhulanso ndi Zekariya kuti,
9 Så sa Herren, hærskarenes Gud: Døm rettferdige dommer og vis miskunnhet og barmhjertighet mot hverandre,
“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Muziweruza molungama; muzichitirana chifundo ndi kumverana chisoni.
10 og undertrykk ikke enker og farløse, fremmede og arminger, og tenk ikke ut ondt mot hverandre i eders hjerte!
Musamazunze akazi amasiye kapena ana amasiye, alendo kapena osauka. Musamaganizirane zoyipa mʼmitima mwanu.’
11 Men de vilde ikke akte på det, men satte i sin gjenstridighet skulderen imot, og sine ører gjorde de døve, så de ikke hørte,
“Koma makolo anu anakana kumvera uthenga umenewu; anawumitsa mtima nandifulatira, natseka makutu awo kuti asamve.
12 og sitt hjerte gjorde de hårdt som en diamant, så de ikke hørte på loven og de ord Herren, hærskarenes Gud, sendte ved sin Ånd gjennem de forrige profeter; derfor kom det en stor vrede fra Herren, hærskarenes Gud.
Anawumitsa mitima yawo ngati mwala wa sangalabwi ndipo sanamvere lamulo kapena mawu amene Yehova Wamphamvuzonse anawatumiza mwa Mzimu wake kudzera mwa aneneri oyamba aja. Kotero Yehova Wamphamvuzonse anakwiya kwambiri.
13 Og likesom han ropte, og de ikke hørte, således, sa Herren, hærskarenes Gud, skal de rope, og jeg vil ikke høre,
“‘Pamene ndinawayitana, iwo sanamvere; choncho pamene iwo anandiyitana, Ine sindinamverenso,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
14 men jeg vil sprede dem som i en stormvind blandt alle hedningefolkene, som de ikke kjenner, og landet skal ligge øde efter dem, så ingen drar frem eller tilbake der. Og således gjorde de det herlige land til en ørken.
‘Ndinawamwaza ndi kamvuluvulu pakati pa mitundu yonse ya anthu, kumene anali alendo. Dziko lawo linatsala litasakazidwa kwambiri kotero kuti palibe amene amabwera kapena kupitamo. Umu ndi mmene anasandutsira dziko labwino kukhala chipululu.’”

< Sakarias 7 >