< Salmenes 85 >
1 Til sangmesteren; av Korahs barn; en salme. Du har fordum, Herre, vært nådig mot ditt land, du lot Jakobs fangenskap ophøre.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Yehova munakomera mtima dziko lanu; munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.
2 Du tok bort ditt folks misgjerning, du skjulte all deres synd. (Sela)
Munakhululukira mphulupulu za anthu anu ndi kuphimba machimo awo onse. (Sela)
3 Du tok bort all din harme, du lot din brennende vrede vende om.
Munayika pambali ukali wanu wonse ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.
4 Vend om til oss, vår frelses Gud, og gjør din harme imot oss til intet!
Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.
5 Vil du evindelig være vred på oss? Vil du la din vrede vare fra slekt til slekt?
Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?
6 Vil du ikke gjøre oss levende igjen, så ditt folk kan glede sig i dig?
Kodi simudzatitsitsimutsanso, kuti anthu anu asangalale mwa Inu?
7 Herre, la oss se din miskunnhet, og gi oss din frelse!
Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova, ndipo tipatseni chipulumutso chanu.
8 Jeg vil høre hvad Gud Herren taler; for han taler fred til sitt folk og til sine fromme - bare de ikke vender tilbake til dårskap.
Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena; Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake, koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.
9 Ja, hans frelse er nær hos dem som frykter ham, forat herlighet skal bo i vårt land.
Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye, kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.
10 Nåde og sannhet skal møte hverandre, rettferd og fred kysse hverandre.
Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi; chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.
11 Sannhet skal vokse op av jorden, og rettferd skue ned fra himmelen.
Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi, ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.
12 Herren skal også gi det som godt er, og vårt land gi sin grøde.
Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino, ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.
13 Rettferd skal gå frem for hans åsyn og stadig følge i hans spor.
Wolungama amapita patsogolo pake ndi kukonza njira za mapazi ake.