< Salmenes 79 >

1 En salme av Asaf. Gud! Hedninger har trengt inn i din arv, de har gjort ditt hellige tempel urent, de har gjort Jerusalem til grushoper.
Salimo la Asafu. Inu Mulungu, anthu a mitundu ina alowerera mʼcholowa chanu; ayipitsa Nyumba yanu yoyera, asandutsa Yerusalemu kukhala bwinja.
2 De har gitt dine tjeneres lik til føde for himmelens fugler, dine helliges kjøtt til ville dyr.
Iwo anapereka mitembo ya atumiki anu kwa mbalame zamlengalenga ngati chakudya, matupi a oyera mtima anu kwa zirombo za dziko lapansi.
3 De har utøst deres blod som vann rundt omkring Jerusalem, og der var ingen som la dem i graven.
Akhetsa magazi monga madzi kuzungulira Yerusalemu yense, ndipo palibe wina woti ayike mʼmanda anthu akufa.
4 Vi er blitt til skam for våre naboer, til spott og hån for dem som er omkring oss.
Ife ndife chinthu chonyozeka kwa anansi athu, choseketsa ndi cholalatiridwa kwa iwo amene atizungulira.
5 Hvor lenge, Herre, vil du være vred evindelig? Hvor lenge skal din nidkjærhet brenne som ild?
Mpaka liti Inu Yehova? Kodi mudzakwiya mpaka muyaya? Kodi mpaka liti nsanje yanu idzayaka ngati moto?
6 Utøs din harme over hedningene, som ikke kjenner dig, og over de riker som ikke påkaller ditt navn!
Khuthulirani ukali wanu pa anthu a mitundu ina amene sakudziwani Inu, pa maufumu amene sayitana pa dzina lanu;
7 For de har fortært Jakob og lagt hans bolig øde.
pakuti iwo ameza Yakobo ndi kuwononga dziko lawo.
8 Tilregn oss ikke våre forfedres misgjerninger! La din miskunn snarlig komme oss i møte, for vi er såre elendige!
Musatilange chifukwa cha machimo a makolo athu chifundo chanu chibwere msanga kukumana nafe, pakuti tili ndi chosowa chachikulu.
9 Hjelp oss, vår frelses Gud, for ditt navns æres skyld, og fri oss og forlat oss våre synder for ditt navns skyld!
Tithandizeni Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, chifukwa cha ulemerero wa dzina lanu; tipulumutseni ndi kutikhululukira machimo athu chifukwa cha dzina lanu.
10 Hvorfor skal hedningene si: Hvor er deres Gud? La det for våre øine kjennes blandt hedningene at dine tjeneres utøste blod blir hevnet,
Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akuti, “Ali kuti Mulungu wawo?” Ife tikuona, zidziwike pakati pa anthu a mitundu ina kuti mumabwezera chilango chifukwa cha magazi amene anakhetsedwa a atumiki anu.
11 la den fangnes sukk komme for ditt åsyn, la dødens barn bli i live efter din arms styrke,
Kubuwula kwa anthu a mʼndende kufike pamaso panu; ndi mphamvu ya dzanja lanu muwasunge amene aweruzidwa kuti aphedwe.
12 og betal våre naboer syvfold i deres fang den hån som de har hånet dig med, Herre!
Mubwezere kwa anansi athu kasanu nʼkawiri kunyoza kumene ananyoza Inu Ambuye.
13 Og vi, ditt folk og den hjord du før, vi vil love dig evindelig; fra slekt til slekt vil vi fortelle din pris.
Pamenepo ife anthu anu, nkhosa za pabusa panu, tidzakutamandani kwamuyaya, kuchokera mʼbado ndi mʼbado tidzafotokoza za matamando anu.

< Salmenes 79 >