< Salmenes 60 >

1 Til sangmesteren; efter Sjusjan edut; en gyllen sang av David til å læres, da han stred mot syrerne fra Mesopotamia og mot syrerne fra Soba, og Joab kom tilbake og slo edomittene i Saltdalen, tolv tusen. Gud! du har forkastet oss, du har sønderslått oss, du var vred; vederkveg oss nu igjen!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere. Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza. Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!
2 Du har rystet jorden, du har fått den til å revne; læg dens skade, for den vakler!
Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba, konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.
3 Du har latt ditt folk se hårde ting, du har gitt oss vin å drikke så vi tumlet.
Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto; inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.
4 Men du har gitt dem som frykter dig, et hærmerke til opreisning, for sannhets skyld. (Sela)
Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera kuti tisonkhanireko pothawa uta.
5 Forat de du elsker, må bli frelst, så hjelp nu med din høire hånd og bønnhør oss!
Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja, kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
6 Gud har talt i sin hellighet. Jeg vil fryde mig; jeg vil utskifte Sikem og opmåle Sukkots dal.
Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwakupambana ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.
7 Mig hører Gilead til, og mig hører Manasse til, og Efra'im er vern for mitt hode, Juda er min herskerstav.
Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu
8 Moab er mitt vaskefat, på Edom kaster jeg min sko; bryt ut i jubel over mig, Filisterland!
Mowabu ndi mbale yanga yosambira, pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga, pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”
9 Hvem vil føre mig til den faste by? Hvem leder mig inn til Edom?
Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
10 Mon ikke du, Gud, som forkastet oss og ikke drog ut med våre hærer, Gud?
Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.
11 Gi oss hjelp mot fienden, for menneskehjelp er tomhet!
Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu, pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.
12 Ved Gud skal vi gjøre storverk, og han skal nedtrede våre fiender.
Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano ndipo tidzapondaponda adani athu.

< Salmenes 60 >