< Salmenes 150 >

1 Halleluja! Lov Gud i hans helligdom, lov ham i hans mektige hvelving!
Tamandani Yehova. Tamandani Mulungu mʼmalo ake opatulika; mutamandeni ku thambo lake lamphamvu.
2 Lov ham for hans veldige gjerninger, lov ham efter hans storhets fylde!
Mutamandeni chifukwa cha machitidwe ake amphamvu; mutamandeni chifukwa cha ukulu wake wopambana.
3 Lov ham med basunklang, lov ham med harpe og citar!
Mutamandeni poyimba malipenga, mutamandeni ndi pangwe ndi zeze.
4 Lov ham med pauke og dans, lov ham med strengelek og fløite!
Mutamandeni ndi matambolini ndi kuvina, mutamandeni ndi zingwe ndi zitoliro.
5 Lov ham med tonende bekkener, lov ham med høit klingende bekkener!
Mutamandeni ndi ziwaya zolira za malipenga, mutamandeni ndi ziwaya zolira kwambiri.
6 Alt som har ånde, love Herren! Halleluja!
Chamoyo chilichonse chopuma chitamande Yehova. Tamandani Yehova.

< Salmenes 150 >