< Salmenes 12 >

1 Til sangmesteren, efter Sjeminit; en salme av David. Frels, Herre! for de fromme er borte, de trofaste er forsvunnet blandt menneskenes barn.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe seminiti. Salimo la Davide. Thandizeni Yehova pakuti palibe munthu wokhulupirika; okhulupirika akusowa pakati pa anthu.
2 Løgn taler de, hver med sin næste, med falske leber; med tvesinnet hjerte taler de.
Aliyense amanamiza mʼbale wake; ndi pakamwa pawo pabodza amayankhula zachinyengo.
3 Herren utrydde alle falske leber, den tunge som taler store ord,
Inu Yehova tsekani milomo yonse yachinyengo ndi pakamwa paliponse podzikuza.
4 dem som sier: Ved vår tunge skal vi få overhånd, våre leber er med oss, hvem er herre over oss?
Pakamwa pamene pamati, “Ife tidzapambana ndi kuyankhula kwathu; pakamwapa ndi pathupathu, tsono mbuye wathu ndani?”
5 For de elendiges ødeleggelses skyld, for de fattiges sukks skyld vil jeg nu reise mig, sier Herren; jeg vil gi dem frelse som stunder efter den.
“Chifukwa cha kuponderezedwa kwa anthu opanda mphamvu ndi kubuwula kwa anthu osowa, Ine ndidzauka tsopano,” akutero Yehova, “Ndidzawateteza kwa owazunza.”
6 Herrens ord er rene ord, likesom sølv som er renset i en smeltedigel i jorden, syv ganger renset.
Ndipo mawu a Yehova ndi angwiro monga siliva oyengedwa mʼngʼanjo yadothi, oyengedwa kasanu nʼkawiri.
7 Du, Herre, vil bevare dem, du vil vokte dem for denne slekt evindelig.
Inu Yehova mudzatitchinjiriza ndipo mudzatiteteza kwa anthu otere kwamuyaya.
8 Rundt omkring svermer de ugudelige, når skarn er ophøiet blandt menneskenes barn.
Oyipa amangoyendayenda ponseponse anthu akamayamikira zochita zawo.

< Salmenes 12 >