< Salmenes 112 >
1 Halleluja! Salig er den mann som frykter Herren, som har sin store lyst i hans bud.
Tamandani Yehova. Wodala munthu amene amaopa Yehova, amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.
2 Hans avkom skal være mektig på jorden; de opriktiges slekt skal velsignes.
Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko; mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.
3 Det er velstand og rikdom i hans hus, og hans rettferdighet står fast evindelig.
Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4 Det går op et lys i mørket for de opriktige, for den som er nådig og barmhjertig og rettferdig.
Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima; wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.
5 Lykkelig er den mann som forbarmer sig og låner ut; han hevder all sin sak i dommen.
Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu, amene amachita ntchito yake mwachilungamo.
6 For han skal ikke rokkes evindelig; den rettferdige skal være i evig minne.
Ndithu sadzagwedezeka; munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.
7 Han skal ikke frykte for nogen ond tidende; hans hjerte er fast, det setter sin lit til Herren.
Saopa akamva zoyipa zimene zachitika; mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.
8 Hans hjerte er trygt; han frykter ikke, inntil han ser med lyst på sine fiender.
Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha; potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.
9 Han har strødd ut, han har gitt de fattige; hans rettferdighet står fast evindelig, hans horn skal ophøies med ære.
Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka, chilungamo chake chimanka mpaka muyaya; nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.
10 Den ugudelige skal se det og harmes, han skal skjære tenner og optæres; de ugudeliges attrå blir til intet.
Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima; adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka. Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.