< Salomos Ordsprog 3 >
1 Min sønn! Glem ikke min lære og la ditt hjerte bevare mine bud!
Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
2 For langt liv og mange leveår og fred skal de gi dig i rikt mål.
Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
3 La ikke kjærlighet og trofasthet vike fra dig, bind dem om din hals, skriv dem på ditt hjertes tavle!
Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
4 Så skal du finne nåde og få god forstand i Guds og menneskers øine.
Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
5 Sett din lit til Herren av hele ditt hjerte, og stol ikke på din forstand!
Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
6 Tenk på ham på alle dine veier! Så skal han gjøre dine stier rette.
Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
7 Vær ikke vis i egne øine, frykt Herren og vik fra det onde!
Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
8 Det skal være lægedom for din kropp og gi ny styrke til dine ben.
Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
9 Ær Herren med gaver av ditt gods og med førstegrøden av all din avling!
Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
10 Så skal dine lader fylles med overflod og dine persekar flyte over av most.
Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
11 Min sønn! Forakt ikke Herrens tukt og vær ikke utålmodig når han refser dig!
Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
12 For den Herren elsker, ham refser han, som en far refser den sønn han har kjær.
Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
13 Salig er det menneske som har funnet visdom, det menneske som vinner forstand;
Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
14 for det er bedre å vinne den enn å vinne sølv, og det utbytte den gir, er bedre enn gull.
pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
15 Den er kosteligere enn perler, og alle dine skatter kan ikke lignes med den.
Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
16 Langt liv har den i sin høire hånd, rikdom og ære i sin venstre.
Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
17 Dens veier er fagre veier, og alle dens stier fører til lykke.
Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
18 Den er et livsens tre for dem som griper den, og hver den som holder fast på den, må prises lykkelig.
Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
19 Herren grunnfestet jorden med visdom; han bygget himmelen med forstand.
Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
20 Ved hans kunnskap vellet de dype vann frem, og ved den lar skyene dugg dryppe ned.
Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
21 Min sønn! La dem ikke vike fra dine øine, bevar visdom og klokskap!
Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
22 Så skal de være liv for din sjel og pryd for din hals.
Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
23 Da skal du vandre din vei trygt og ikke støte din fot.
Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
24 Når du legger dig, skal du ikke frykte, og når du har lagt dig, skal din søvn være søt.
pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
25 Da trenger du ikke å være redd for uventet skrekk, eller for uværet når det kommer over de ugudelige!
Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
26 For Herren skal være din tillit, og han skal bevare din fot fra å fanges.
pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
27 Nekt ikke de trengende din hjelp, når det står i din makt å gi den!
Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
28 Si ikke til din næste: Gå bort og kom igjen, jeg skal gi dig imorgen - når du kan gjøre det straks!
Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
29 Legg ikke op onde råd mot din næste, når han kjenner sig trygg hos dig!
Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
30 Trett ikke med et menneske uten årsak, når han ikke har gjort dig noget ondt!
Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
31 Misunn ikke en voldsmann, og velg ikke nogen av alle hans veier!
Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
32 For en falsk mann er en vederstyggelighet for Herren, men med de opriktige har han fortrolig samfund.
Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
33 Herrens forbannelse er over den ugudeliges hus, men de rettferdiges bolig velsigner han.
Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
34 Spotterne spotter han, men de ydmyke gir han nåde.
Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
35 De vise arver ære, men dårene får skam til lønn.
Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.