< Salomos Ordsprog 29 >

1 En mann som er ofte straffet og allikevel gjør sin nakke stiv, vil i et øieblikk bli sønderbrutt, og der er ingen lægedom.
Munthu amene amawumitsabe khosi lake atadzudzulidwa kwambiri, adzawonongeka mwadzidzidzi popanda chomuchiritsa.
2 Når de rettferdige kommer til makten, gleder folket sig; men når en ugudelig mann hersker, sukker folket.
Anthu olungama akamalamulira mʼdziko anthu amakondwa, koma ngati dziko lilamulidwa ndi anthu oyipa mtima anthu amadandaula.
3 En mann som elsker visdom, gleder sin far; men den som holder vennskap med skjøger, øder sitt gods.
Munthu amene amakonda nzeru amasangalatsa abambo ake, koma woyenda ndi akazi achiwerewere amasakaza chuma chake.
4 En konge trygger sitt land ved rett; men en mann som tar imot gaver, bryter det ned.
Mfumu imalimbitsa dziko poweruza mwachilungamo, koma mfumu imene imawumiriza anthu kuti ayipatse mphatso imawononga dziko.
5 En mann som smigrer for sin næste, setter op et garn for hans fot.
Munthu woshashalika mnzake, akudziyalira ukonde mapazi ake.
6 En ond manns misgjerning er en snare for ham, men den rettferdige skal juble og glede sig.
Munthu woyipa amakodwa ndi machimo ake, koma wochita chilungamo amayimba lokoma.
7 Den rettferdige tar sig av småfolks sak; den ugudelige skjønner sig ikke på noget.
Munthu wolungama amasamalira anthu osauka, koma woyipa salabadira zimenezi.
8 Spottere egger op byen, men vismenn stiller vreden.
Anthu onyoza atha kuwutsa ziwawa mu mzinda, koma anthu anzeru amaletsa ukali.
9 Når en vismann går i rette med en dåre, så blir dåren vred og ler, og der blir ingen ro.
Ngati munthu wanzeru atsutsana ndi chitsiru, chitsirucho chimachita phokoso ndi kumangoseka ndipo sipakhala mtendere.
10 De blodtørstige hater den ustraffelige, men de rettsindige søker å redde hans liv.
Anthu okhetsa magazi amadana ndi munthu wangwiro koma anthu olungama amasamalira moyo wake.
11 All sin vrede lar dåren strømme ut, men den vise holder vreden tilbake og stiller den.
Munthu wopusa amaonetsa mkwiyo wake, koma munthu wanzeru amadzigwira.
12 Når en hersker akter på løgnens ord, blir alle hans tjenere ugudelige.
Ngati wolamulira amvera zabodza, akuluakulu ake onse adzakhala oyipa.
13 Den fattige og den som undertrykker ham, møtes; Herren gir begges øine deres lys.
Munthu wosauka ndi munthu wopondereza anzake amafanana pa kuti: Yehova ndiye anawapatsa maso onsewa.
14 En konge som dømmer småfolk rettferdig, hans trone står fast for alle tider.
Ngati mfumu iweruza osauka moyenera, mpando wake waufumu udzakhazikika nthawi zonse.
15 Ris og tukt gir visdom; men en gutt som er overlatt til sig selv, gjør sin mor skam.
Ndodo ndi chidzudzulo zimapatsa nzeru koma mwana womulekerera amachititsa amayi ake manyazi.
16 Når de ugudelige får makt, får synden makt; men de rettferdige skal se deres fall med glede.
Oyipa akamalamulira zoyipa zimachuluka, koma anthu olungama adzaona kugwa kwa anthu oyipawo.
17 Tukt din sønn, så skal han bli dig til glede og vederkvege din sjel!
Umulange mwana wako ndipo adzakupatsa mtendere ndi kusangalatsa mtima wako.
18 Uten åpenbaring blir folket tøilesløst; men lykkelig er den som holder loven.
Ngati uthenga wochokera kwa Yehova supezeka anthu amangochita zofuna zawo; koma wodala ndi amene amasunga malamulo.
19 Ved ord lar en træl sig ikke tukte; for han skjønner dem nok, men adlyder dem ikke.
Munthu wantchito sangalangizidwe ndi mawu okha basi; ngakhale awamvetse mawuwo sadzatha kuchitapo kanthu.
20 Har du sett en mann som forhaster sig i sine ord - det er mere håp for dåren enn for ham.
Ngakhale munthu wa uchitsiru nʼkuti ndiponi popeza chikhulupiriro chilipo kuposa munthu wodziyesa yekha kuti ndi wanzeru poyankhula.
21 Forkjæler en sin træl fra ungdommen av, så vil han til sist være sønn i huset.
Ngati munthu asasatitsa wantchito wake kuyambira ali mwana, potsirizira adzapeza kuti wantchitoyo wasanduka mlowachuma wake.
22 Den som er snar til vrede, vekker trette, og en hastig mann gjør ofte det som er ondt.
Munthu wamkwiyo amayambitsa mikangano, ndipo munthu waukali amachita zolakwa zambiri.
23 Et menneskes stolthet fører ham til fall, men den ydmyke vinner ære.
Kunyada kwa munthu kudzamutsitsa, koma munthu wodzichepetsa amalandira ulemu.
24 Den som deler med en tyv, hater sitt liv; han hører opropet til ed og gir allikevel ingen oplysning.
Woyenda ndi munthu wakuba ndi mdani wa moyo wake womwe; amalumbira koma osawulula kanthu.
25 Menneskefrykt fører i snare, men den som setter sin lit til Herren, han blir berget.
Kuopa munthu kudzakhala ngati msampha, koma aliyense amene amadalira Yehova adzatetezedwa.
26 Mange søker en herskers yndest, men fra Herren kommer en manns rett.
Anthu ambiri amafunitsitsa kuti wolamulira awakomere mtima, koma munthu amaweruzidwa mwachilungamo ndi thandizo la Yehova basi.
27 En urettferdig mann er en vederstyggelighet for de rettferdige, og en vederstyggelighet for den ugudelige er den som lever rett.
Anthu olungama amanyansidwa ndi anthu achinyengo; koma anthu oyipa amanyansidwa ndi anthu a mtima wowongoka.

< Salomos Ordsprog 29 >