< Salomos Ordsprog 16 >

1 Hjertets råd hører mennesket til, men fra Herren får tungen sitt svar.
Zolinga za mu mtima ndi za munthu, koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.
2 Alle en manns veier er rene i hans egne øine, men Herren veier åndene.
Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake, koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.
3 Legg dine gjerninger på Herren, så skal dine råd ha fremgang.
Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova, ndipo zolinga zako zidzachitikadi.
4 Herren har gjort hver ting til dens øiemed, også den ugudelige til straffens dag.
Yehova amachita zonse ndi cholinga chake, ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.
5 Enhver overmodig er en vederstyggelighet for Herren; visselig, en slik mann blir ikke ustraffet.
Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova. Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.
6 Ved kjærlighet og trofasthet utsones misgjerning, og den som frykter Herren, holder sig fra det onde.
Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake; chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.
7 Når Herren har behag i en manns ferd, da gjør han at endog hans fiender holder fred med ham.
Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova, ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.
8 Bedre er lite med rettferdighet enn stor vinning med urett.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo, kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.
9 Menneskets hjerte tenker ut sin vei, men Herren styrer hans gang.
Mtima wa munthu umalingalira zochita, koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.
10 Guddoms-ord er på kongens leber; hans munn skal ikke forsynde sig når han dømmer.
Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu; ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.
11 Rett vekt og rette vektskåler hører Herren til; alle vektstener i pungen er hans verk.
Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova; miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.
12 Ugudelige gjerninger er en vederstyggelighet for konger; for ved rettferdighet blir tronen trygget.
Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu, pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.
13 Rettferdige leber er til velbehag for konger, og den som taler det som rett er, elsker de.
Mawu owona amakondweretsa mfumu. Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.
14 En konges vrede er dødens bud, men en vis mann stiller vreden.
Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa, koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.
15 I lyset fra kongens åsyn er det liv, og hans nåde er som en sky med vårregn.
Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo; ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.
16 Å vinne visdom - hvor meget bedre er det ikke enn gull! Og å vinne forstand er mere verdt enn sølv.
Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide. Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.
17 De opriktiges vei er å holde sig fra det onde; den som akter på sin vei, bevarer sitt liv.
Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa; wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.
18 Forut for undergang går overmot, og forut for fall stolt mot.
Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wodzikuza adzagwa.
19 Det er bedre å være ydmyk sammen med dem som er i nød, enn å dele bytte med de overmodige.
Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa, kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.
20 Den som akter på ordet, skal finne lykke, og den som setter sin lit til Herren, er salig.
Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino, ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.
21 Den som er vis i hjertet, blir kalt forstandig, og lebers sødme fremmer lærdom.
A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu, ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.
22 Klokskap er en livsens kilde for dem som eier den, men dårers straff er deres egen dårskap.
Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako, koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.
23 Den vises hjerte gjør hans munn forstandig og legger mere og mere lærdom på hans leber.
Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru, ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.
24 Milde ord er kostelig honning, søt for sjelen og en lægedom for kroppen.
Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi, amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.
25 Mangen vei tykkes en mann rett, men enden på det er dødens veier.
Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.
26 Arbeiderens sult arbeider for ham; for hans munn driver ham frem.
Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira; njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.
27 En niding graver en ulykkesgrav, og på hans leber er det likesom en fortærende ild.
Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.
28 En falsk mann volder trette, og en øretuter skiller venn fra venn.
Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano, ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.
29 En voldsmann forlokker sin næste og fører ham inn på en vei som ikke er god.
Munthu wandewu amakopa mnansi wake, ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.
30 Den som lukker sine øine for å tenke på svik, og den som kniper sine leber sammen, han har allerede fullført det onde.
Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota; amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.
31 Grå hår er en fager krone; den finnes på rettferdighets vei.
Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero; munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.
32 Den langmodige er bedre enn en veldig helt, og den som styrer sitt sinn, er bedre enn den som inntar en by.
Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo, munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.
33 I kappens fold rystes loddet, men avgjørelsen kommer alltid fra Herren.
Maere amaponyedwa pa mfunga, koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.

< Salomos Ordsprog 16 >