< Filippenserne 1 >

1 Paulus og Timoteus, Kristi Jesu tjenere - til alle de hellige i Kristus Jesus som er i Filippi, tillikemed tilsynsmenn og menighetstjenere:
Paulo ndi Timoteyo, atumiki a Khristu Yesu. Kulembera anthu onse oyera mtima a ku Filipi amene ali mwa Khristu Yesu, pamodzi ndi oyangʼanira ndi atumiki awo.
2 Nåde være med eder og fred fra Gud vår Fader og den Herre Jesus Kristus!
Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale kwa inu.
3 Jeg takker min Gud så ofte jeg kommer eder i hu,
Ndimayamika Mulungu wanga nthawi zonse ndikakumbukira inu.
4 idet jeg alltid når jeg beder, gjør min bønn for eder alle med glede,
Mʼmapemphero anga onse opempherera inu, nthawi zonse ndimapemphera ndi chimwemwe
5 på grunn av eders samfund med mig i arbeidet for evangeliet fra den første dag inntil nu.
chifukwa mwakhala mukundithandiza polalikira Uthenga Wabwino kuyambira tsiku loyamba mpaka tsopano.
6 Og jeg er fullt viss på dette at han som begynte en god gjerning i eder, vil fullføre den inntil Jesu Kristi dag,
Sindikukayika konse kuti Iye amene anayamba ntchito yabwino mwa inu adzayipitiriza ndi kuyimaliza mpaka pa tsiku la kubweranso kwa Khristu Yesu.
7 likesom det jo er rimelig for mig å tenke således om eder alle, eftersom jeg bærer eder i mitt hjerte, både i mine lenker og når jeg forsvarer og stadfester evangeliet, siden I alle har del med mig i nåden.
Kwa ine ndi bwino kuti ndiziganiza zotere za nonsenu, popeza ndimakukondani, ngakhale ndikhale mʼndende, kapena pamene ndikuteteza ndi kukhazikitsa Uthenga Wabwino, inu nonse mumagawana nane chisomo cha Mulungu.
8 For Gud er mitt vidne hvorledes jeg lenges efter eder alle med Kristi Jesu hjertelag.
Mulungu angandichitire umboni kuti ndimakulakalakani ndi chikondi cha Khristu Yesu.
9 Og dette beder jeg om at eders kjærlighet ennu må bli alt rikere og rikere på kunnskap og all skjønnsomhet,
Ndipo pemphero langa ndi lakuti chikondi chanu chipitirire kukulirakulira pa chidziwitso ndi kuzama mʼmaganizo,
10 forat I må kunne dømme om de forskjellige ting, så I kan være rene og uten anstøt til Kristi dag,
kuti mukhoza kuzindikira chabwino koposa zonse ndi chiti kuti muthe kukhala wopanda chodetsa ndi wopanda chilema kufikira tsiku la Khristu.
11 fylt med rettferdighets frukt, som virkes ved Jesus Kristus, Gud til ære og lov.
Ndipo moyo wanu udzakhala odzazidwa ndi chipatso cha chilungamo chimene chimachokera mwa Yesu Khristu. Pakuti zimenezi zidzapereka ulemerero ndi matamando kwa Mulungu.
12 Jeg vil at I skal vite, brødre, at det jeg har oplevd, heller har tjent til evangeliets fremme,
Tsopano abale, ndikufuna mudziwe kuti chimene chandichitikira ine chathandiza kwambiri kupititsa patsogolo Uthenga Wabwino.
13 så at det er blitt vitterlig for hele livvakten og for alle de andre at det er for Kristi skyld jeg er i lenker,
Chotsatira chake nʼchakuti zadziwika bwino lomwe kwa onse amene ali ku nyumba yaufumu kuti ine ndili mʼmaunyolo chifukwa cha Khristu.
14 og så at de fleste av brødrene i Herren har fattet tiltro til mine lenker og derved enn mere har fått mot til å tale ordet uten frykt.
Moti chifukwa cha maunyolo angawa, abale ambiri alimbikitsidwa kuyankhula Mawu a Mulungu molimbika ndi mopanda mantha.
15 Vel forkynner også somme Kristus av avind og for kivs skyld, men andre dog også av velvilje;
Nʼzoonadi kuti ena amalalikira Khristu chifukwa cha kaduka ndi mikangano, koma ena chifukwa cha zolinga zabwino.
16 disse forkynner Kristus av kjærlighet, idet de vet at jeg er satt til å forsvare evangeliet,
Olalikira ndi zolinga zabwinowa amachita izi mwachikondi, podziwa kuti ine ndili muno chifukwa cha kuteteza Uthenga Wabwino.
17 men hine gjør det av trettesyke, ikke med ren hu, idet de mener å legge trengsel til mine lenker.
Ena aja amalalikira Khristu modzikonda osati moona mtima namaganiza kuti kutero kubweretsa mavuto pamene ndili mʼmaunyolo.
18 Hvad da? Kristus forkynnes dog på enhver måte, enten det skjer for syns skyld eller i sannhet, og det gleder jeg mig over; ja, jeg vil og fremdeles glede mig;
Nanga kodi zimenezo zili ndi ntchito? Chofunika ndi chakuti Khristu alalikidwe, kaya ndi mwachinyengo kapena moona. Ndipo ndikukondwera chifukwa cha chimenechi. Ndithu, ndidzapitirira kukondwera,
19 for jeg vet at dette skal bli mig til frelse ved eders bønn og Jesu Kristi Ånds hjelp,
pakuti ndikudziwa kuti chifukwa cha mapemphero anu ndi thandizo lochokera kwa Mzimu wa Yesu Khristu, zimene zandionekera zidzathandiza kuti ndimasulidwe.
20 efter min inderlige lengsel og mitt håp om at jeg ikke skal bli til skamme i nogen ting, men at Kristus, som alltid, så og nu, med all frimodighet skal bli forherliget ved mitt legeme, enten det blir ved liv eller ved død.
Ndili ndi chiyembekezo chonse kuti sindidzachita manyazi ndi pangʼono pomwe, koma ndidzakhala ndi chilimbikitso chokwanira kuti monga mwa nthawi zonse, tsopano Khristu adzakwezedwa mʼthupi langa kaya ndi mʼmoyo kapena mu imfa.
21 For mig er livet Kristus og døden en vinning;
Pakuti kwa ine kukhala moyo ndi Khristu ndipo kufa ndi phindu.
22 men dersom det å leve i kjødet gir mig frukt av min gjerning, så vet jeg ikke hvad jeg skal velge,
Ngati nditi ndipitirire kukhala ndi moyo mʼthupi ndiye kuti kwa ine ndi kugwira ntchito yopindulitsa. Kodi ndisankhe chiyani? Sindikudziwa.
23 men står rådvill mellem de to ting, idet jeg har lyst til å fare herfra og være med Kristus for dette er meget, meget bedre;
Ndathinidwa ndi zinthu ziwirizi: Ndikulakalaka kunyamuka kuti ndikakhale ndi Khristu, chimene ndi chinthu chabwino kwambiri.
24 men å bli i kjødet er nødvendigere for eders skyld.
Komanso nʼkofunika kwambiri kuti ndikhalebe mʼthupi chifukwa cha inu.
25 Og da jeg er fullt viss på dette, vet jeg at jeg skal bli i live og være hos eder alle til eders fremgang og glede i troen,
Ndili ndi chitsimikizo, ndikudziwa kuti ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzapitirira nanu kuti nonse mupite mʼtsogolo ndi kukhala ndi chimwemwe mu chikhulupiriro
26 forat eders ros kan bli rik i Kristus Jesus ved mig, når jeg kommer til eder igjen.
kuti pokhala nanunso, kudzitamandira kwanu mwa Khristu Yesu kudzasefukire chifukwa cha ine.
27 Bare før eders liv således som verdig er for Kristi evangelium, forat jeg, enten jeg kommer og ser eder, eller jeg er fraværende, må få høre om eder at I står fast i én Ånd, så I med én sjel kjemper sammen for troen på evangeliet
Chilichonse chimene chingachitike, chachikulu nʼchakuti mukhale moyo ofanana ndi Uthenga Wabwino wa Khristu. Tsono ngati ndingabwere kudzakuonani kapena kumangomva za inu ndili kutali, ndidzadziwa kuti mwayima mwamphamvu mwa Mzimu mmodzi, kulimbika pamodzi ngati munthu mmodzi chifukwa cha chikhulupiriro cha Uthenga Wabwino
28 og ikke i nogen ting lar eder skremme av motstanderne; det er for dem et varsel om undergang, men om eders frelse, og det fra Gud.
osachita mantha ndi pangʼono pomwe ndi amene akutsutsana nanu. Ichi ndi chizindikiro kwa iwo kuti adzawonongedwa, koma inu mudzapulumutsidwa ndi Mulungu.
29 For eder blev det unt, for Kristi skyld - ikke bare å tro på ham, men og å lide for hans skyld,
Pakuti inu mwapatsidwa mwayi osati ongokhulupirira Khristu kokha, koma wakumva zowawa mʼmalo mwa Khristu.
30 idet I har den samme strid som I så på mig og nu hører om mig.
Inunso mukudutsa mʼzowawa zomwe zija munaona ndikudutsamo inenso ndipo pano mukumva kuti ndikukumana nazobe.

< Filippenserne 1 >