< 4 Mosebok 1 >

1 Og Herren talte til Moses i Sinai ørken i sammenkomstens telt på den første dag i den annen måned i det annet år efterat de var gått ut av Egyptens land, og sa:
Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti,
2 Ta op manntall over hele Israels barns menighet efter deres ætter og familier og skriv op deres navn - alle som er av mannkjønn, en for en,
“Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi.
3 fra tyveårsalderen og opover; alle dem i Israel som kan dra ut i krig, skal I mønstre, hær efter hær, du og Aron.
Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali.
4 I skal ha med eder en mann for hver stamme, den som er overhode for stammens familier.
Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi.
5 Dette er navnene på de menn som I skal ha til hjelp: For Ruben: Elisur, Sede'urs sønn,
Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa: Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,
6 for Simeon: Selumiel, Surisaddais sønn,
Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,
7 for Juda: Nahson, Amminadabs sønn,
Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,
8 for Issakar: Netanel, Suars sønn,
Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,
9 for Sebulon: Eliab, Helons sønn,
Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,
10 for Josefs sønner, for Efra'im: Elisama, Ammihuds sønn, for Manasse: Gamliel, Pedasurs sønn,
Mwa ana a Yosefe: kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi; kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;
11 for Benjamin: Abidan, Gideonis sønn,
Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,
12 for Dan: Akieser, Ammisaddais sønn,
Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,
13 for Aser: Pagiel, Okrans sønn,
Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,
14 for Gad: Eljasaf, De'uels sønn,
Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,
15 for Naftali: Akira, Enans sønn.
Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”
16 Dette var menighetens utkårne, høvdingene for sine fedrenestammer, overhodene for Israels tusener.
Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.
17 Da lot Moses og Aron disse menn, som var nevnt ved navn, komme,
Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa,
18 og de samlet hele menigheten på den første dag i den annen måned; og de lot sig innføre i ættelistene med sine navn, efter sine ætter og familier, fra tyveårsalderen og opover, en for en,
ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi
19 således som Herren hadde befalt Moses; og han mønstret dem i Sinai ørken.
monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:
20 Efterkommerne av Rubens sønner - han som var Israels førstefødte - opskrevet efter sine ætter og familier, med sine navn, en for en, alt mannkjønn fra tyveårsalderen og opover, alle som kunde dra ut i krig,
Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
21 så mange som blev mønstret av Rubens stamme, var seks og firti tusen og fem hundre.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.
22 Efterkommerne av Simeons sønner, opskrevet efter sine ætter og familier, med sine navn, så mange av dem som blev mønstret, en for en, alt mannkjønn fra tyveårsalderen og opover, alle som kunde dra ut i krig,
Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
23 så mange som blev mønstret av Simeons stamme, var ni og femti tusen og tre hundre.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.
24 Efterkommerne av Gads sønner, opskrevet efter sine ætter og familier, med sine navn, fra tyveårsalderen og opover, alle som kunde dra ut i krig,
Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
25 så mange som blev mønstret av Gads stamme, var fem og firti tusen, seks hundre og femti.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.
26 Efterkommerne av Judas sønner, opskrevet efter sine ætter og familier, med sine navn, fra tyveårsalderen og opover, alle som kunde dra ut i krig,
Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
27 så mange som blev mønstret av Juda stamme, var fire og sytti tusen og seks hundre.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.
28 Efterkommerne av Issakars sønner, opskrevet efter sine ætter og familier, med sine navn, fra tyveårsalderen og opover, alle som kunde dra ut i krig,
Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
29 så mange som blev mønstret av Issakars stamme, var fire og femti tusen og fire hundre.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.
30 Efterkommerne av Sebulons sønner, opskrevet efter sine ætter og familier, med sine navn, fra tyveårsalderen og opover, alle som kunde dra ut i krig,
Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
31 så mange som blev mønstret av Sebulons stamme, var syv og femti tusen og fire hundre.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.
32 Josefs barn: Efterkommerne av Efra'ims sønner, opskrevet efter sine ætter og familier, med sine navn, fra tyveårsalderen og opover, alle som kunde dra ut i krig,
Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe: Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
33 så mange som blev mønstret av Efra'ims stamme, var firti tusen og fem hundre;
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.
34 efterkommerne av Manasses sønner, opskrevet efter sine ætter og familier, med sine navn, fra tyveårsalderen og opover, alle som kunde dra ut i krig,
Kuchokera mwa zidzukulu za Manase: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
35 så mange som blev mønstret av Manasse stamme, var to og tretti tusen og to hundre.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.
36 Efterkommerne av Benjamins sønner, opskrevet efter sine ætter og familier, med sine navn, fra tyveårsalderen og opover, alle som kunde dra ut i krig,
Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
37 så mange som blev mønstret av Benjamins stamme, var fem og tretti tusen og fire hundre.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.
38 Efterkommerne av Dans sønner, opskrevet efter sine ætter og familier, med sine navn, fra tyveårsalderen og opover, alle som kunde dra ut i krig,
Kuchokera mwa zidzukulu za Dani: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
39 så mange som blev mønstret av Dans stamme, var to og seksti tusen og syv hundre.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.
40 Efterkommerne av Asers sønner, opskrevet efter sine ætter og familier, med sine navn, fra tyveårsalderen og opover, alle som kunde dra ut i krig,
Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
41 så mange som blev mønstret av Asers stamme, var en og firti tusen og fem hundre.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.
42 Efterkommerne av Naftalis sønner, opskrevet efter sine ætter og familier, med sine navn, fra tyveårsalderen og opover, alle som kunde dra ut i krig,
Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali: Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
43 så mange som blev mønstret av Naftali stamme, var tre og femti tusen og fire hundre.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.
44 Dette var de som blev mønstret, de som Moses og Aron og Israels høvdinger mønstret, og høvdingene var tolv i tallet, en for hver stamme.
Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake.
45 Og alle de av Israels barn som blev mønstret efter sine familier, fra tyveårsalderen og opover, alle i Israel som kunde dra ut i krig,
Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo.
46 så mange som blev mønstret, var seks hundre og tre tusen, fem hundre og femti;
Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.
47 Men levittene efter sin fedrenestamme blev ikke mønstret sammen med dem.
Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena.
48 For Herren talte til Moses og sa:
Pakuti Yehova anawuza Mose kuti,
49 Bare Levi stamme skal du ikke mønstre, og over dem skal du ikke opta manntall sammen med de andre Israels barn.
“Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli.
50 Men du skal sette levittene over vidnesbyrdets tabernakel og over alle dets redskaper og over alt som hører til; de skal bære tabernaklet og alle dets redskaper, og de skal tjene ved tabernaklet og leire sig rundt omkring det.
Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo.
51 Når tabernaklet skal bryte op, skal levittene ta det ned, og når tabernaklet skal leire sig, skal levittene reise det op; kommer nogen fremmed;
Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa.
52 Israels barn skal leire sig, hver i sin leir og hver ved sitt banner, hær for hær.
Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake.
53 Men levittene skal leire sig rundt omkring vidnesbyrdets tabernakel, forat det ikke skal komme vrede over Israels barns menighet; og levittene skal ta vare på det som er å vareta ved vidnesbyrdets tabernakel.
Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”
54 Og Israels barn gjorde så; de gjorde i ett og alt således som Herren hadde befalt Moses.
Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.

< 4 Mosebok 1 >