< Nehemias 5 >
1 Men det reiste sig et stort skrik fra folket og deres hustruer mot deres jødiske brødre.
Tsono anthu ena ndi akazi awo anayamba kudandaula kwambiri chifukwa cha Ayuda anzawo.
2 Nogen sa: Vi med våre sønner og døtre er mange; la oss få korn, så vi kan ete og berge livet!
Ena ankanena kuti, “Ife ndi ana athu aamuna ndi aakazi, tilipo ochuluka kwambiri. Choncho tikufuna tirigu kuti tidye ndi kukhala ndi moyo.”
3 Andre sa: Våre marker og vingårder og hus må vi sette i pant; la oss få korn til å stille vår hunger!
Panali ena amene ankanena kuti, “Ife tikuchita kupereka minda yathu, mitengo yathu ya mphesa ndi nyumba zathu ngati chikole kuti tipeze tirigu chifukwa njala yakula.”
4 Atter andre sa: Vi har lånt penger på våre marker og vingårder for å betale skatten til kongen;
Panalinso ena amene ankanena kuti, “ife tinachita kukongola ndalama zoti tipereke msonkho wa minda ndi mitengo yathu ya mphesa kwa mfumu.
5 og dog er vi av samme kjød og blod som våre brødre, og våre barn som deres barn; men vi må la våre sønner og døtre bli træler, ja, nogen av våre døtre er alt blitt trælkvinner, og det står ikke i vår makt å hindre det; for våre marker og vingårder hører andre til.
Ngakhale kuti ndife amodzi ndi abale athuwa, ndipo ngakhalenso ana athu ndi ofanana ndi ana awo, ife tikukakamiza ana athu kuti akhale akapolo. Ena mwa ana athu aakazi atengedwa kale ukapolo. Ife tilibe mphamvu yochitapo kanthu popeza anthu ena anatenga kale minda yathu ndi mitengo yathu ya mphesa.”
6 Da jeg hørte deres klagerop og disse deres ord, blev jeg meget vred.
Nditamva madandawulo awo ndi zimene amanenazi ndinapsa mtima kwambiri.
7 Jeg overveide saken med mig selv, og så irettesatte jeg de fornemme og forstanderne og sa til dem: I krever rente av eders brødre! Så sammenkalte jeg et stort folkemøte mot dem.
Nditalingalira bwino ndinatsimikiza zoti ndichitepo kanthu ndipo kenaka ndinawadzudzula anthu olemekezeka ndi akuluakuluwo. Ndinawawuza kuti, “Zoona ndithu inu nʼkumalipiritsana chiwongoladzanja chachikulu anthu apachibale nokhanokha!” Choncho ndinayitanitsa msonkhano waukulu kuti ndiwazenge mlandu
8 Og jeg sa til dem: Vi har, så vidt vi kunde, løskjøpt våre jødiske brødre som var solgt til hedningene, og så vil I selge eders brødre, og de må selge sig til oss! Da tidde de og fant ikke et ord til svar.
ndipo ndinati, “Monga zakhaliramu ife tikutha kuwombola abale anthu amene anagulitsidwa ukapolo kwa anthu ena. Kodi tsopano inu mukugulitsanso abale anu kwa anzawo kuti ife tiwumirizidwe kuwawombola?” Iwo anakhala chete, chifukwa sanapeze mawu oti anene.
9 Så sa jeg: Det er ikke rett det I gjør; burde I ikke vandre i frykt for vår Gud, så ikke hedningene, våre fiender, skal få grunn til å håne oss?
Kotero ndinapitiriza kunena kuti, “Zimene mukuchitazi si zabwino. Kodi inu simungakhale ndi moyo woopa Mulungu wathu kuti tipewe kunyoza kwa adani athu, anthu a mitunda inayi?
10 Også jeg og mine brødre og mine folk har lånt dem penger og korn; la oss eftergi denne gjeld!
Ine ndi abale anga ndiponso antchito anga tikuwakongozanso anthuwa ndalama ndi tirigu. Ndipo tiyeni tilekeretu zolandira chiwongoladzanja!
11 Gi nu I dem på denne dag deres marker, vingårder, oljehaver og hus tilbake og eftergi dem rentene av pengene og kornet og mosten og oljen som I har lånt dem!
Abwezereni lero lomwe minda yawo, mitengo ya mphesa, mitengo ya olivi ndiponso nyumba zawo. Muwabwezerenso chiwongoladzanja cha ndalama, tirigu, vinyo ndi mafuta zimene munatenga.”
12 Da sa de: Vi vil gi det tilbake og ikke kreve noget av dem; vi vil gjøre som du sier. Og efterat jeg hadde tilkalt prestene, lot jeg dem sverge på at de vilde gjøre som de hadde sagt.
Iwo anayankha kuti, “Ife tidzawabwezera zimenezi popanda kupemphapo kanthu kalikonse kwa iwo. Tidzachita monga mwanena.” Pambuyo pake ndinayitanitsa ansembe ndipo pamaso pawo ndinawalumbiritsa atsogoleriwo ndi akuluakuluwo kuti adzachitadi zomwe analonjezazo.
13 Jeg rystet også ut brystfolden på min kjortel og sa: Således skal Gud ryste hver mann som ikke holder dette sitt ord, ut av hans hus og gods - så utrystet og tom skal han bli! Og hele forsamlingen sa: Amen! Og de priste Herren, og folket gjorde efter det som var sagt.
Ndipo inenso ndinakutumula chovala changa ndi kuti, “Chimodzimodzinso Mulungu akutumule munthu wosasunga malonjezano ake. Amulande nyumba yake ndi katundu wake ndi kumusandutsa mʼmphawi!” Apo msonkhano wonse unati, “Ameni” natamanda Yehova. Ndipo anthu aja anachita monga analonjezera.
14 Fra den dag jeg blev utnevnt til stattholder i Juda land, fra kong Artaxerxes' tyvende år til hans to og trettiende år, i hele tolv år, har hverken jeg eller mine brødre nytt noget av den kost som stattholderen kunde kreve.
Ndiponso kuyambira nthawi imene anandisankha kuti ndikhale bwanamkubwa wa dziko la Yuda, kuchokera chaka cha makumi awiri mpaka chaka cha 32 muulamuliro wa ufumu wa Aritasasita, ndiye kuti kwa zaka zokwana 12, ine ngakhale abale anga sitinalandire chakudya choyenerera bwanamkubwa.
15 De forrige stattholdere, de som var før mig, falt folket til byrde og tok brød og vin av dem foruten firti sekel sølv, og endog deres tjenere trykket folket; men jeg gjorde ikke så, for jeg fryktet Gud.
Koma abwanamkubwa akale ankasautsa anthu. Iwo ankalanda anthu chakudya ndi vinyo ndi kuwalipiritsanso masekeli asiliva makumi anayi. Ngakhalenso antchito awo amavutitsa anthu kwambiri. Koma ine sindinachite zimenezo chifukwa ndimaopa Mulungu.
16 Jeg var også selv med i arbeidet på denne mur, og noget jordstykke har vi ikke kjøpt; og alle mine folk har vært samlet til arbeidet der.
Ndiponso ndinadzipereka kugwira ntchito yomanga khoma la mzinda wa Yerusalemu popanda ngakhale kugulapo munda. Antchito anganso anasonkhana komweko kuti agwire ntchito ndipo sitinafunenso malo ena.
17 Og jødene og forstanderne, hundre og femti mann, åt ved mitt bord, foruten dem som kom til oss fra hedningefolkene rundt omkring.
Kuwonjezera apa, ndinkadyetsa Ayuda, akuluakulu kuphatikizanso anthu amene ankabwera kwa ife kuchokera kwa mitundu ya anthu otizungulira okwanira 150.
18 Og det som blev tillaget for hver dag, var en okse og seks utvalgte stykker småfe foruten fugler, og alt dette kostet jeg selv; og en gang hver tiende dag var det overflod av all slags vin; og allikevel krevde jeg ikke den kost som stattholderen hadde rett til; for arbeidet lå tungt på dette folk.
Tsiku lililonse pamaphikidwa ngʼombe imodzi, nkhosa zabwino zisanu ndi imodzi pamodzi ndi nkhuku. Ndipo pakutha pa masiku khumi aliwonse pankakhala matumba achikopa ochuluka a vinyo wa mitundu yonse. Ngakhale zinali choncho, Ine sindinatenge chakudya choperekedwa kwa bwanamkubwa, chifukwa izi zinali zosautsa anthu.
19 Kom mig i hu, min Gud, og regn mig til gode alt det jeg har gjort for dette folk!
Kuti zinthu zindiyendere bwino, kumbukirani Yehova Mulungu wanga pa zonse zimene ndachitira anthu awa.