< Lukas 2 >
1 Og det skjedde i de dager at det utgikk et bud fra keiser Augustus at all verden skulde innskrives i manntall.
Mʼmasiku amenewo Kaisara Augusto anapereka lamulo kuti kalembera achitike mʼdziko lonse la Aroma.
2 Dette var den første innskrivning, i den tid Kvirinius var landshøvding i Syria.
(Uyu ndi kalembera woyamba amene anachitika pamene Kureniyo anali bwanamkubwa wa Siriya).
3 Og alle gikk for å la sig innskrive, hver til sin by.
Ndipo aliyense anapita ku mzinda wa kwawo kukalembetsa.
4 Men også Josef drog op fra Galilea, fra byen Nasaret, til Judea, til Davids stad, som heter Betlehem, fordi han var av Davids hus og ætt,
Choncho Yosefe anachoka ku Nazareti ku Galileya kupita ku Yudeya, ku Betelehemu ku mudzi wa Davide, chifukwa anali wa banja ndi fuko la Davide.
5 for å la sig innskrive sammen med Maria, sin trolovede, som var fruktsommelig.
Iye anapita kumeneko kukalembetsa pamodzi ndi Mariya, amene anapalana naye ubwenzi kuti akwatirane ndipo anali woyembekezera.
6 Men det skjedde mens de var der, da kom tiden da hun skulde føde.
Ali kumeneko, nthawi inakwana yakuti mwana abadwe,
7 Og hun fødte sin sønn, den førstefødte, og svøpte ham og la ham i en krybbe, fordi det ikke var rum for dem i herberget.
ndipo anabereka mwana wake woyamba, wamwamuna. Iye anamukulunga mʼnsalu ndi kumuyika modyera ngʼombe, chifukwa kunalibe malo mʼnyumba ya alendo.
8 Og det var nogen hyrder der på stedet, som var ute på marken og holdt nattevakt over sin hjord.
Ndipo kunali abusa amene amakhala ku dera lomwelo, kuyangʼanira ziweto zawo usiku.
9 Og se, en Herrens engel stod for dem, og Herrens herlighet lyste om dem, og de blev meget forferdet.
Mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iwo ndipo ulemerero wa Ambuye unawala mowazungulira. Iwo anachita mantha.
10 Og engelen sa til dem: Forferdes ikke! for se, jeg forkynner eder en stor glede, som skal vederfares alt folket!
Koma mngeloyo anawawuza kuti, “Musachite mantha. Ine ndakubweretserani Uthenga Wabwino wachimwemwe chachikulu umene udzakhala wa anthu onse.
11 Eder er idag en frelser født, som er Kristus, Herren, i Davids stad.
Lero mʼmudzi wa Davide wakubwadwirani Mpulumutsi; Iye ndi Khristu Ambuye.
12 Og dette skal I ha til tegn: I skal finne et barn svøpt, liggende i en krybbe.
Ichi chidzakhala chizindikiro kwa inu: mukapeza mwana wakhanda wokutidwa ndi nsalu atagona modyera ngʼombe.”
13 Og straks var det hos engelen en himmelsk hærskare, som lovet Gud og sa:
Mwadzidzidzi gulu lalikulu la angelo linaonekera pamodzi ndi mngeloyo, kuyamika Mulungu ndi kumati,
14 Ære være Gud i det høieste, og fred på jorden, i mennesker hans velbehag!
“Ulemerero kwa Mulungu mmwambamwamba, ndi mtendere kwa anthu pa dziko lapansi amene Iye akondwera nawo.”
15 Og det skjedde da englene var faret fra dem op til himmelen, da sa hyrdene til hverandre: La oss nu gå like til Betlehem og se dette som har hendt, og som Herren har kunngjort oss!
Angelowo atabwerera kumwamba, abusawo anati kwa wina ndi mnzake, “Tiyeni ku Betelehemu tikaone zinthu zomwe zachitika, zimene Ambuye atiwuza ife.”
16 Og de skyndte sig og kom og fant både Maria og Josef, og barnet som lå i krybben;
Ndipo iwo anafulumira nyamuka nakapeza Mariya ndi Yosefe ndi mwana wakhanda, amene anagona modyera ngʼombe.
17 og da de hadde sett det, fortalte de dem det ord som var sagt dem om dette barn.
Pamene anamuona Iye, iwo anafotokoza zomwe anawuzidwa za mwanayo,
18 Og alle som hørte det, undret sig over det som blev dem sagt av hyrdene;
ndipo onse amene anamva zimene abusawa ananena anadabwa.
19 men Maria gjemte alle disse ord og grundet på dem i sitt hjerte.
Koma Mariya anasunga zonsezi mu mtima mwake ndi kumazilingalira.
20 Og hyrdene vendte tilbake, og priste og lovet Gud for alt det de hadde hørt og sett, således som det var blitt sagt dem.
Abusa anabwerera, akulemekeza ndi kuyamika Mulungu chifukwa cha zonse anazimva ndi kuziona, zomwe zinali monga anawuzidwira ndi angelo aja.
21 Og da åtte dager var til ende, og han skulde omskjæres, blev han kalt Jesus, det navn som engelen hadde nevnt før han blev undfanget i mors liv.
Pa tsiku lachisanu ndi chitatu, tsiku loti amuchite mdulidwe anamutcha Yesu, dzina limene mngelo anamupatsa asanabadwe.
22 Og da deres renselses-dager efter Mose lov var til ende, førte de ham op til Jerusalem for å stille ham frem for Herren -
Nthawi yoyeretsedwa kwawo itatha, monga mwa lamulo la Mose, Yosefe ndi Mariya anapita naye ku Yerusalemu kukamupereka kwa Ambuye.
23 som det er skrevet i Herrens lov: Alt mannkjønn som åpner mors liv, skal kalles hellig for Herren -
(Monga mmene zinalembedwera mu lamulo la Ambuye kuti, “Muzikapereka kwa Ambuye mwana aliyense wamwamuna woyamba kubadwa”),
24 og for å gi offer, efter det som er sagt i Herrens lov, et par turtelduer eller to due-unger.
ndi kupereka nsembe posunga zimene zinanenedwa mulamulo la Ambuye: “Njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri.”
25 Og se, det var en mann i Jerusalem ved navn Simeon, og denne mann var rettferdig og gudfryktig og ventet på Israels trøst; og den Hellige Ånd var over ham,
Ndipo taonani, mu Yerusalemu munali munthu wotchedwa Simeoni, amene anali wolungama ndi wodzipereka. Iye ankadikira chitonthozo cha Israeli, ndipo Mzimu Woyera anali pa iye.
26 og det var åpenbaret ham av den Hellige Ånd at han ikke skulde se døden før han hadde sett Herrens salvede.
Mzimu Woyera anamuwululira kuti sadzafa asanaone Khristu wa Ambuye.
27 Han kom, drevet av Ånden, inn i templet, og da foreldrene førte barnet Jesus inn for å gjøre med ham som skikk var efter loven,
Motsogozedwa ndi Mzimu Woyera, iye anapita ku bwalo la Nyumba ya Mulungu. Makolo ake a Yesu atabwera naye kuti achite naye mwambo malingana ndi malamulo,
28 da tok han ham på sine armer og lovet Gud og sa:
Simeoni anamunyamula mʼmanja mwake nayamika Mulungu, nati:
29 Herre! nu lar du din tjener fare herfra i fred, efter ditt ord;
“Ambuye waulamuliro, monga munalonjeza, tsopano lolani kuti mtumiki wanu apite mu mtendere.
30 for mine øine har sett din frelse,
Pakuti maso anga aona chipulumutso chanu,
31 som du har beredt for alle folks åsyn,
chimene Inu munakonza pamaso pa anthu onse,
32 et lys til åpenbarelse for hedningene, og en herlighet for ditt folk Israel.
kuwala kowunikira anthu a mitundu ina ndi kwa ulemerero kwa anthu anu Aisraeli.”
33 Og hans far og hans mor undret sig over det som blev talt om ham.
Abambo ndi amayi a Mwanayo anadabwa chifukwa cha zimene zinanenedwa za Iye.
34 Og Simeon velsignet dem, og sa til hans mor Maria: Se, denne er satt til fall og opreisning for mange i Israel, og til et tegn som blir motsagt;
Kenaka Simeoni anawadalitsa ndipo anati kwa Mariya amayi ake: “Mwana uyu wakonzedwa kukhala kugwa ndi kudzuka kwa ambiri mu Israeli, ndi kukhala chizindikiro chimene adzayankhula motsutsana nacho,
35 men også din sjel skal et sverd gjennemstinge, forat mange hjerters tanker skal bli åpenbaret.
kotero kuti malingaliro a mitima ya ambiri adzawululidwa. Ndipo lupanga lidzabaya moyo wakonso.”
36 Og der var en profetinne, Anna, Fanuels datter, av Asers stamme; hun var kommet langt ut i årene, hadde levd med sin mann i syv år efter sin jomfrustand,
Panalinso mneneri wamkazi, dzina lake Ana, mwana wa Fanuelo, wa fuko la Aseri. Anali wokalamba kwambiri; anakhala ndi mwamuna wake zaka zisanu ndi ziwiri atakwatiwa,
37 og nu for sig selv som enke inntil en alder av fire og åtti år; hun vek aldri fra templet, men tjente Gud med faste og bønn natt og dag.
ndipo kenaka anakhala wamasiye mpaka pamene anali ndi zaka 84. Iye sanachoke mʼNyumba ya Mulungu koma ankapembedza usiku ndi usana, kusala kudya ndi kupemphera.
38 Og hun trådte til i samme stund og priste Gud, og hun talte om ham til alle dem som ventet på forløsning for Jerusalem.
Pa nthawiyo pamene ankapita kwa iwo, iye anayamika Mulungu ndi kuyankhula za Mwanayo kwa onse amene ankayembekezera chipulumutso cha Yerusalemu.
39 Og da de hadde fullført alt efter Herrens lov, vendte de tilbake til Galilea, til sin by Nasaret.
Yosefe ndi Mariya atachita zonse zimene zinkafunikira ndi lamulo la Ambuye, anabwerera ku Galileya ku mudzi wa Nazareti.
40 Men barnet vokste og blev sterkt og fullt av visdom, og Guds velbehag var over ham.
Ndipo Mwanayo anakula nakhala wamphamvu; Iye anadzazidwa ndi nzeru, ndipo chisomo cha Mulungu chinali pa Iye.
41 Og hans foreldre drog hvert år til Jerusalem til påskefesten.
Chaka chilichonse makolo ake ankapita ku Yerusalemu ku phwando la Paska.
42 Og da han var tolv år gammel, drog de der op, som det var skikk på høitiden;
Iye ali ndi zaka khumi ndi ziwiri, anapita ku phwando, monga mwa mwambo.
43 og da de hadde vært der de dager til ende, og de vendte hjem igjen, blev barnet Jesus tilbake i Jerusalem, og hans foreldre visste ikke om det.
Phwando litatha, pamene makolo ake ankabwerera kwawo, mnyamata Yesu anatsalira ku Yerusalemu, koma iwo sanadziwe zimenezi.
44 Men da de trodde at han var i reisefølget, kom de en dags reise frem, og lette efter ham blandt slektninger og kjenninger;
Poganiza kuti anali nawo mʼgulu lawo, anayenda tsiku limodzi. Kenaka anayamba kumufunafuna pakati pa abale awo ndi anzawo.
45 og da de ikke fant ham, vendte de tilbake til Jerusalem og lette efter ham.
Atalephera kumupeza, anabwerera ku Yerusalemu kukamufuna.
46 Og det skjedde tre dager derefter, da fant de ham i templet; der satt han midt iblandt lærerne og hørte på dem og spurte dem,
Patatha masiku atatu anamupeza ali mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu, atakhala pakati pa aphunzitsi, akumvetsera ndi kuwafunsa mafunso.
47 og alle som hørte ham, var ute av sig selv av forundring over hans forstand og svar.
Aliyense amene anamumva Iye anadabwa ndi chidziwitso chake ndi mayankho ake.
48 Og da de så ham, blev de forferdet, og hans mor sa til ham: Barn! hvorfor gjorde du oss dette? Se, din far og jeg har lett efter dig med smerte.
Makolo ake atamuona, anadabwa. Amayi ake anati kwa Iye, “Mwanawe, watichitira zimenezi chifukwa chiyani? Abambo ako ndi ine takhala tili ndi nkhawa kukufunafuna Iwe.”
49 Og han sa til dem: Hvorfor lette I efter mig? Visste I ikke at jeg må være i min Faders hus?
Iye anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mumandifunafuna? Kodi simukudziwa kuti ndikuyenera kukhala mʼnyumba ya Atate anga?”
50 Men de forstod ikke det ord han talte til dem.
Koma iwo sanazindikire chomwe Iye amatanthauza.
51 Og han gikk ned med dem og kom til Nasaret og var dem lydig. Og hans mor gjemte alle disse ord i sitt hjerte.
Kenaka anapita nawo ku Nazareti ndipo anawamvera iwo. Koma amayi ake anasunga zinthu zonsezi mu mtima mwawo.
52 Og Jesus gikk frem i visdom og alder og yndest hos Gud og mennesker.
Ndipo Yesu anakula mu nzeru, msinkhu ndi chisomo cha Mulungu ndi anthu.