< 3 Mosebok 20 >

1 Og Herren talte til Moses og sa:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Du skal si til Israels barn: Om nogen av Israels barn eller av de fremmede som bor i Israel, gir noget av sine barn fra sig til Molok, skal han late livet; folket i landet skal stene ham.
“Uza Aisraeli kuti, ‘Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala mu Israeli wopereka mwana wake kwa Moleki ayenera kuphedwa. Anthu a mʼdera lakelo amuphe ndi miyala.
3 Jeg vil sette mitt åsyn mot den mann og utrydde ham av hans folk fordi han har gitt sitt barn fra sig til Molok og gjort min helligdom uren og vanhelliget mitt hellige navn.
Munthu ameneyo ndidzamufulatira ndi kumuchotsa pakati pa anzake.’ Popereka mwana wake kwa Moleki, wadetsa malo anga wopatulika ndi kuyipitsa dzina langa loyera.
4 Om folket i landet lukker øinene til og ikke straffer en sådan mann med døden når han gir sitt barn fra sig til Molok,
Ngati anthu a mʼderalo achita ngati sakumuona munthuyo pamene akupereka mwana wake kwa Moleki ndi kusamupha,
5 da vil jeg sette mitt åsyn mot denne mann og hans slekt, og ham og alle dem som følger ham i å drive avgudsdyrkelse med Molok, vil jeg utrydde av deres folk.
Ineyo ndidzamufulatira pamodzi ndi banja lake. Ndidzawachotsa pakati pa anthu anzawo onse amene anamutsatira, nadziyipitsa okha popembedza Moleki.”
6 Når nogen vender sig til dødningemanere og sannsigere og driver avgudsdyrkelse med dem, da vil jeg sette mitt åsyn mot den mann og utrydde ham av hans folk.
“‘Ngati munthu adzapita kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa kapena kwa owombeza, nadziyipitsa powatsatira iwowo, Ine ndidzamufulatira ndi kumuchotsa pakati pa anthu anzake.
7 I skal hellige eder og være hellige; for jeg er Herren eders Gud.
“‘Chifukwa chake dzipatuleni ndi kukhala woyera popeza Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
8 Og I skal ta vare på mine lover og holde dem; jeg er Herren, som helliger eder.
Ndipo sungani malangizo anga ndi kuwatsata. Ine ndine Yehova amene ndimakuyeretsani.
9 Hver den som banner sin far eller sin mor, skal late livet; sin far og sin mor har han bannet, hans blod være over ham!
“‘Munthu aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa. Magazi ake adzakhala pamutu pake chifukwa iye watemberera abambo kapena amayi ake.
10 Når en mann driver hor med en annen manns hustru - med sin næstes hustru, da skal de begge late livet, både mannen og kvinnen som har drevet hor.
“‘Ngati munthu wachita chigololo ndi mkazi wa mnzake, mwamunayo pamodzi ndi mkaziyo ayenera kuphedwa.
11 Når en mann ligger hos sin fars hustru, har han vanæret sin fars leie; de skal begge late livet, deres blod være over dem!
“‘Ngati munthu agonana ndi mkazi wa abambo ake, wachititsa manyazi abambo ake. Munthuyo pamodzi ndi mkaziyo ayenera kuphedwa. Magazi awo adzakhala pa mitu pake.
12 Når en mann ligger hos sin sønnekone, skal de begge late livet; de har gjort en vederstyggelig gjerning, deres blod være over dem!
“‘Ngati munthu agonana ndi mkazi wa mwana wake, awiriwo ayenera kuphedwa. Iwo achita chinthu chonyansa kwambiri. Magazi awo adzakhala pa mitu pawo.
13 Når en mann ligger hos en annen mann som en ligger hos en kvinne, da har de begge gjort en vederstyggelig gjerning; de skal late livet, deres blod være over dem!
“‘Ngati munthu agonana ndi mwamuna mnzake ngati akugonana ndi mkazi, ndiye kuti onsewo achita chinthu cha manyazi. Choncho aphedwe. Magazi awo adzakhala pa mitu pawo.
14 Når en mann tar både mor og datter til ekte, da er det skammelig ferd; både han og kvinnene skal brennes med ild; slik skam skal ikke finnes blandt eder.
“‘Ngati munthu akwatira mkazi, nakwatiranso amayi ake, chimenecho ndi chinthu choyipa kwambiri. Mwamunayo pamodzi ndi akaziwo ayenera kutenthedwa pa moto kuti chinthu choyipa chotere chisapezekenso pakati panu.
15 En mann som har omgang med et dyr, skal late livet, og dyret skal I drepe.
“‘Ngati mwamuna agonana ndi nyama, iye ayenera kuphedwa, ndipo muyeneranso kupha nyamayo.
16 Når en kvinne kommer nær noget dyr og har omgang med det, da skal du slå ihjel både kvinnen og dyret; de skal late livet, deres blod være over dem!
“‘Ngati mkazi agonana ndi nyama, aphedwe pamodzi ndi nyamayo. Mkaziyo ndi nyamayo ayenera kuphedwa, ndipo magazi awo adzakhala pa mitu pawo.
17 Når en mann tar sin søster, sin fars eller sin mors datter, til ekte og har omgang med henne, og hun med ham, da er det skammelig ferd, og de skal utryddes for sitt folks øine; han har hatt omgang med sin søster, han skal lide for sin misgjerning.
“‘Ngati munthu akakwatira mlongo wake, mwana wamkazi wa abambo ake, kapena mwana wamkazi wa amayi ake, ndipo iwo nʼkugonana, ndiye kuti achita chinthu chochititsa manyazi. Onse awiri ayenera kuchotsedwa pa gulu la abale awo. Tsono popeza munthuyo wachititsa manyazi mlongo wake, adzayenera kulandira chilango.
18 Når en mann ligger hos en kvinne som har sin månedlige urenhet, og har omgang med henne, da har han avdekket hennes kilde, og hun har avdekket sitt blods kilde; de skal begge utryddes av sitt folk.
“‘Ngati munthu agonana ndi mkazi pa nthawi yake yosamba, ndiye kuti wavula msambo wake, ndipo mkaziyo wadzivulanso. Onse awiri achotsedwe pakati pa anthu anzawo.
19 Din mors eller din fars søster skal du ikke ha omgang med, for den som gjør dette, vanærer sin nærmeste slekt; de skal lide for sin misgjerning.
“‘Musagonane ndi mchemwali wa amayi anu kapena abambo anu, pakuti kutero ndi kuchititsa manyazi mʼbale wanu. Nonse mudzalipira mlandu wanu.
20 Når en mann ligger hos sin farbrors hustru, har han vanæret sin farbror; de skal lide for sin synd, de skal dø barnløse.
“‘Ngati munthu agonana ndi azakhali ake, munthuyo wachititsa manyazi a malume ake. Onse adzalipira mlandu wawo. Onsewo adzafa wopanda mwana.
21 Når en mann tar sin brors hustru, da er det skamløs ferd; han har vanæret sin bror, de skal være barnløse.
“‘Munthu akakwatira mkazi wa mchimwene wake ndiye kuti wachita chinthu chonyansa. Wachititsa manyazi mʼbale wakeyo. Onse awiriwo adzakhala wopanda mwana.
22 I skal ta vare på alle mine lover og alle mine bud og holde dem, forat ikke landet skal utspy eder, det land som jeg fører eder til og vil la eder bo i,
“‘Nʼchifukwa chake muzisunga malangizo anga onse ndi malamulo anga ndipo muwatsatire kuti ku dziko limene Ine ndikupita nanu kuti mukakhalemo lisakakusanzeni.
23 og I skal ikke følge det folks skikker som jeg driver ut for eder; for alt dette har de gjort, og jeg vemmedes ved dem,
Musatsanzire miyambo ya mitundu ya anthu imene ndi kuyipirikitsa inu mukufika. Chifukwa iwo anachita zinthu zonsezi, ndipo Ine ndinanyansidwa nawo.
24 og jeg sa til eder: I skal ta deres land i eie, og jeg vil gi eder det til eiendom, et land som flyter med melk og honning; jeg er Herren eders Gud, som har skilt eder ut fra folkene.
Koma Ine ndinakuwuzani kuti, ‘Mudzatenga dziko lawo. Ine ndidzakupatsani dzikolo kuti likhale cholowa chanu, dziko loyenda mkaka ndi uchi.’ Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndakupatulani pakati pa mitundu yonse ya anthu.
25 Derfor skal I skille mellem rene dyr og urene og mellem urene fugler og rene og ikke gjøre eder selv vederstyggelige ved å ete de firføtte dyr eller de fugler eller det kryp på jorden som jeg har skilt ut for eder, forat I skal holde dem for urene.
“‘Chifukwa chake muzisiyanitsa pakati pa nyama zoyeretsedwa ndi nyama zodetsedwa ndiponso pakati pa mbalame zoyeretsedwa ndi mbalame zodetsedwa. Musadzidetse pakudya nyama iliyonse kapena mbalame, kapena chilichonse chimene chimakwawa pansi, chimene Ine ndachipatula kuti chikhale chodetsedwa kwa inu.
26 I skal være hellige for mig; for jeg, Herren, er hellig, og jeg har skilt eder ut fra folkene, forat I skal høre mig til.
Muzikhala woyera pamaso panga chifukwa Ine Yehova, ndine woyera ndipo ndakupatulani pakati pa anthu a mitundu yonse kuti mukhale anthu anga.
27 Når det i en mann eller kvinne er en dødningemaner-ånd eller en sannsiger-ånd, da skal de late livet; de skal stenes, deres blod være over dem!
“‘Mwamuna kapena mkazi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa kapena wanyanga pakati panu ayenera kuphedwa. Muwagende ndi miyala, ndipo magazi awo adzakhala pa mitu pawo.’”

< 3 Mosebok 20 >