< Dommernes 13 >

1 Men Israels barn gjorde atter det som var ondt i Herrens øine; og Herren gav dem i filistrenes hånd i firti år.
Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova, kotero Yehova anawapereka mʼmanja mwa Afilisti kwa zaka makumi anayi.
2 Der var en mann fra Sora av danittenes ætt, han hette Manoah; hans hustru var ufruktbar og hadde aldri hatt barn.
Ku Zora kunali munthu wina dzina lake Manowa, wochokera ku fuko la Dani. Mkazi wake analibe ana popeza anali wosabereka.
3 Og Herrens engel åpenbarte sig for kvinnen og sa til henne: Se, du er ufruktbar og har aldri hatt barn; men du skal bli fruktsommelig og føde en sønn.
Mngelo wa Yehova anaonekera mkaziyo ndipo anati, “Ndinu wosabereka ndipo mulibedi mwana, komabe mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna.
4 Så ta dig nu i vare og drikk ikke vin eller sterk drikk og et ikke noget urent!
Tsono mudzisamale bwino, osamwa vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa ndiponso musamadye chakudya chilichonse chodetsedwa,
5 For nu skal du bli fruktsommelig og føde en sønn, og det skal ikke komme rakekniv på hans hode, for barnet skal være en Guds nasireer fra mors liv; og han skal begynne å frelse Israel fra filistrenes hånd.
chifukwa mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna. Mwanayo akadzabadwa lumo lisadzapite pa mutu chifukwa mnyamatayo adzakhala Mnaziri, ndiye kuti wopatulika kwa Mulungu kuyambira pa nthawi imene adzakhale ali mʼchiberekero. Ndipo adzayamba ntchito yopulumutsa Israeli mʼmanja mwa Afilisti.”
6 Og kvinnen kom og sa til sin mann: En Guds mann kom til mig; han var å se til som Guds engel, såre forferdelig; men jeg spurte ham ikke hvorfra han var, og han sa mig ikke sitt navn.
Kenaka mayiyo anapita kukawuza mwamuna wake kuti, “Munthu wa Mulungu anabwera kwa ine, ndipo maonekedwe ake anali ngati mngelo wa Mulungu, maonekedwe woopsa kwambiri. Ine sindinamufunse kumene amachokera, ndipo iyeyo sanandiwuzenso dzina lake.
7 Men han sa til mig: Nu skal du bli fruktsommelig og føde en sønn; drikk nu ikke vin eller sterk drikk og et ikke noget urent! For barnet skal være en Guds nasireer fra mors liv og til sin dødsdag.
Koma anandiwuza kuti, ‘Mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna. Choncho musamamwe vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa, musamadye chakudya chilichonse choyipitsidwa chifukwa mwanayo adzakhala Mnaziri, wopatulika kwa Mulungu kuyambira pa nthawi imene adzakhale ali mʼchiberekero mpaka tsiku la kufa kwake.’”
8 Da bad Manoah til Herren og sa: Hør mig, Herre! La den Guds mann som du sendte, komme til oss igjen og lære oss hvad vi skal gjøre med det barn som skal fødes!
Kenaka Manowa anapemphera kwa Yehova kuti, “Chonde Ambuye, lolani munthu wa Mulungu amene munamutuma abwerenso kwa ife kuti adzatiphunzitse zochita ndi mwanayo akadzabadwa.”
9 Og Gud hørte Manoahs bønn; og Guds engel kom atter til kvinnen, mens hun satt ute på marken, og Manoah, hennes mann, ikke var med henne.
Mulungu anamva pemphero la Manowa, ndipo mngelo wa Mulungu anabweranso kwa mkaziyo nthawi imene anali ku munda, koma Manowa mwamuna wake sanali naye.
10 Da skyndte kvinnen sig og løp hjem og fortalte det til sin mann og sa: Nu har han vist sig for mig igjen den mann som kom til mig her om dagen.
Tsono mkaziyo anathamanga kukawuza mwamuna wake kuti, “Wandionekeranso munthu uja amene anabwera kwa ine tsiku lija.”
11 Manoah stod op og fulgte efter sin hustru, og da han kom til mannen, sa han til ham: Er du den mann som talte til min kone? Han svarte: Ja.
Choncho Manowa ananyamuka namutsatira mkazi wake. Atafika kwa munthuyo anamufunsa kuti, “Kodi ndinu munayankhula ndi mkazi wanga?” Iye anayankha kuti, “Ndine.”
12 Og Manoah sa: Når nu dine ord går i opfyllelse, hvorledes skal vi da bære oss at med barnet, og hvad skal vi gjøre med ham?
Kenaka Manowa anafunsa kuti, “Tiyerekeze kuti mawu anuwa akwaniritsidwadi, ndiye mwanayu azidzakhala bwanji ndipo azidzachita chiyani?”
13 Da sa Herrens engel til Manoah: Alt det jeg har nevnt for kvinnen, skal hun ta sig i vare for.
Ndipo mngelo wa Yehova uja anamuyankha kuti, “Zonse zimene ndinawawuza akazi anuwa asamale ndipo adzazichitedi.
14 Hun skal ikke ete noget av det som kommer av vintreet, og ikke drikke vin eller sterk drikk og ikke ete noget urent; alt det jeg har pålagt henne, skal hun holde sig efter.
Asadzadye chilichonse chochokera ku mphesa. Asadzamwe vinyo kapena choledzeretsa chilichonse, ngakhale kudya chakudya chilichonse chodetsedwa. Zonse zimene ndinawalamula azisunge bwino.”
15 Da sa Manoah til Herrens engel: Kan vi ikke få dig til å bli en stund her, sa vi kan lage til et kje for dig!
Manowa anamuwuza mngelo wa Yehova uja kuti, “Chonde dikirani pangʼono, timati tikukonzereni mwana wambuzi.”
16 Men Herrens engel sa til Manoah: Om du får mig til å bli, så eter jeg allikevel ikke av din mat; men vil du stelle til et brennoffer, så skal du ofre det til Herren. For Manoah visste ikke at det var Herrens engel.
Mngelo wa Yehova anayankha kuti, “Ngakhale mukundidikiritsa, ine sindidya chakudya chanu. Koma ngati mukonze nsembe yopsereza iperekeni kwa Yehova.” (Manowa nʼkuti asakudziwa kuti munthuyo anali mngelo wa Mulungu).
17 Da sa Manoah til Herrens engel: Hvad er ditt navn? - så vi kan ære dig når dine ord går i opfyllelse.
Tsono Manowa anapempha mngelo wa Yehova kuti, “Chonde tidziwitseni dzina lanu kuti zikadzachitika zimene mwanenazi ife tidzakulemekezeni?”
18 Men Herrens engel sa til ham: Hvorfor spør du om mitt navn? - Det er et underlig navn!
Iye anayankha kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukufunsa dzina langa? Dzina laketu ndi lodabwitsa.”
19 Så tok Manoah kjeet og matofferet og ofret det på berget til Herren. Da lot han et under skje mens Manoah og hans hustru så på det:
Ndipo Manowa anatenga mwana wambuzi pamodzi ndi chopereka cha chakudya nakapereka nsembe pa thanthwe kwa Yehova ndipo Yehova anachita zodabwitsa kwa Manowa ndi mkazi wake akuona.
20 Da luen steg op fra alteret mot himmelen, fór Herrens engel op i alterets lue mens Manoah og hans hustru så på det, og de falt på sitt ansikt til jorden.
Pamene malawi a moto amakwera kumwamba kuchoka pa guwa, mngelo wa Yehova uja anakwera kumwamba mʼmalawi a motowo Manowa ndi mkazi wake akuona. Tsono anadzigwetsa pansi naweramitsa mitu yawo pansi.
21 Siden viste Herrens engel sig ikke mere for Manoah og hans hustru; da forstod Manoah at det var Herrens engel.
Mngelo wa Yehova uja sanaonekerenso kwa Manowa ndi mkazi wake. Choncho Manowa anazindikira kuti anali mngelo wa Yehova.
22 Og Manoah sa til sin hustru: Vi må visselig dø; vi har sett Gud.
Iye anawuza mkazi wake kuti, “Ife tifa basi pakuti taona Mulungu!”
23 Men hans hustru sa til ham: Dersom Herren hadde lyst til å drepe oss, så hadde han ikke tatt imot brennoffer og matoffer av vår hånd og ikke latt oss se alt dette og ikke nu latt oss høre sådant.
Koma mkazi wake anamuyankha kuti, “Yehova akanafuna kutipha sakanayilandira nsembe yathu yopsereza ndi chopereka chathu chachakudya chija, ndipo sakanationetsanso zinthu zonsezi kapena kutiwuza zinthu ngati zimenezi nthawi ino.”
24 Og kvinnen fødte en sønn og gav ham navnet Samson; og gutten vokste op, og Herren velsignet ham.
Motero mkaziyo anabereka mwana wa mwamuna, namutcha dzina lake Samsoni. Iye anakula ndipo Yehova anamudalitsa.
25 Og Herrens Ånd begynte å drive ham, mens han var i Dans leir mellem Sora og Estaol.
Mzimu wa Yehova unayamba kumulimbikitsa pamene ankakhala ku misasa ya anthu a fuko la Dani, malo amene anali pakati pa Zora ndi Esitaoli.

< Dommernes 13 >