< Esaias 60 >
1 Stå op, bli lys! For ditt lys kommer, og Herrens herlighet går op over dig.
“Dzuka, wala, pakuti kuwala kwako kwafika, ndipo ulemerero wa Yehova wakuwalira.
2 Se, mørke dekker jorden, og mulm folkene, men over dig skal Herren opgå, og over dig skal hans herlighet åpenbare sig,
Taona, mdima waphimba dziko lapansi ndipo mdima wandiweyani wagwa pa anthu a mitundu ina, koma Yehova adzakuwalira iwe, ndipo ulemerero wake udzaoneka pa iwe.
3 og folkeslag skal søke til ditt lys, og konger til den glans som er gått op over dig.
Mitundu ya anthu idzatsata kuwunika kwako ndipo mafumu adzalondola kunyezimira kwa mʼbandakucha wako.
4 Løft dine øine og se dig omkring! De samler sig alle sammen, de kommer til dig; dine sønner skal komme fra det fjerne, og dine døtre skal bæres på armen.
“Tukula maso ako, yangʼanayangʼana ndipo ona zimene zikuchitika. Onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe; ana ako a amuna akubwera kuchokera kutali ndipo ana ako aakazi anyamulidwa mʼmanja.
5 Da skal du se det og stråle av glede, og ditt hjerte skal banke og utvide sig; for havets rikdom skal vende sig til dig, folkenes gods skal komme til dig.
Ukadzaona zimenezi udzasangalala kwambiri, mtima wako udzalumpha ndi kudzaza ndi chimwemwe; chuma chakunyanja chidzabwera kwa iwe chuma cha mitundu ya anthu chidzabwera kwa iwe.
6 Et mylder av kameler skal dekke dig, Midians og Efas kamelføll; alle sammen skal de komme fra Sjeba; gull og virak skal de føre til dig, og Herrens pris skal de forkynne.
Gulu la ngamira lidzaphimba dziko lako, ngamira zingʼonozingʼono zidzachokera ku Midiyani ndi ku Efai. Ndipo onse a ku Seba adzabwera atanyamula golide ndi lubani uku akutamanda Yehova.
7 Alle Kedars får skal samles til dig, Nebajots værer skal tjene dig; til mitt velbehag skal de ofres på mitt alter, og min herlighets hus vil jeg herliggjøre.
Ziweto zonse za ku Kedara adzazisonkhanitsa kwa inu, nkhosa zazimuna za ku Nabayoti zidzakutumikirani; zidzalandiridwa monga chopereka pa guwa langa la nsembe, ndipo ndidzakongoletsa Nyumba yanga.
8 Hvem er disse som kommer flyvende som skyer, som duer til sine dueslag?
“Kodi ndi zayani izo zikuwuluka ngati mitambo, ngati kapena nkhunda zobwerera ku zisa zawo?
9 For på mig skal øene vente, og fremst seiler Tarsis-skibene og fører dine barn hit fra det fjerne, deres sølv og gull kommer med dem - for Herrens, din Guds navns skyld, for Israels Helliges skyld, for han herliggjør dig.
Ndithu, izi ndi sitima za pa madzi zochokera ku mayiko akutali; patsogolo pali sitima zapamadzi za ku Tarisisi, zikubweretsa ana ako ochokera kutali, pamodzi ndi siliva wawo ndi golide wawo, kudzalemekeza Yehova Mulungu wako, Woyerayo wa Israeli, pakuti Iye wakuvekani inu ulemerero.
10 Og fremmede skal bygge dine murer, og deres konger skal tjene dig; i min harme har jeg slått dig, men i min nåde har jeg forbarmet mig over dig.
“Alendo adzamanganso malinga ako, ndipo mafumu awo adzakutumikira. Ngakhale ndinakukantha ndili wokwiya, koma tsopano ndidzakukomera mtima ndikukuchitira chifundo.
11 Og dine porter skal holdes åpne all tid, hverken dag eller natt skal de lukkes, så folkenes gods kan føres inn til dig, og deres konger føres med som fanger.
Zipata zako zidzakhala zotsekula nthawi zonse, sadzazitseka nthawi zonse, usana ndi usiku, kotero anthu adzabwera kwa iwe ndi chuma chawo, akuyenda pa mdipiti mafumu awo ali patsogolo.
12 For det folk og det rike som ikke vil tjene dig, skal gå til grunne, og hedningene skal bli aldeles ødelagt.
Pakuti mtundu wa anthu ndi mafumu amene sakutumikira iwe; adzawonongeka kotheratu.
13 Libanons herlighet skal komme til dig, både cypress og lønn og buksbom, for å pryde det sted der min helligdom er, og det sted hvor mine føtter står, vil jeg herliggjøre.
“Adzabwera nayo kwa iwe mitengo ya payini, mkuyu ndi naphini imene ili mʼnkhalango ya Lebanoni kuti adzakongoletsere malo a nyumba yanga yopatulika; ndipo ndidzalemekeza malo amene Ine ndimapondapo.
14 Og barna til dem som har plaget dig, skal komme bøiede til dig, og alle de som har foraktet dig, skal kaste sig ned for dine føtter, og de skal kalle dig Herrens stad, Israels Helliges Sion.
Ana aja amene anakuzunzani adzabwera ndipo adzakugwadirani; onse amene anakunyozani adzagwada pansi pa mapazi anu. Ndipo adzakutchani kuti Mzinda wa Yehova; Ziyoni mzinda wa Woyerayo wa Israeli.
15 I stedet for at du var forlatt og hatet, så det ikke var nogen som drog igjennem dig, vil jeg gjøre dig til en evig herlighet, en fryd for slekt efter slekt.
“Ngakhale anthu anakusiya nadana nawe, koma Ine ndidzakukuza mpaka muyaya, ndipo udzakhala malo a chimwemwe cha anthu amibado yonse.
16 Og du skal die hedningefolks melk, ja, kongers bryst skal du die, og du skal kjenne at jeg, Herren, er din frelser, og Jakobs Veldige din gjenløser.
Udzamwa mkaka wa mitundu ya anthu ndi kuleredwa pa maere aufumu, motero udzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wako, Momboli wako ndiye Wamphamvu wa Yakobo.
17 I stedet for kobber vil jeg gi gull, i stedet for jern vil jeg gi sølv, i stedet for tre kobber og i stedet for sten jern, og jeg vil gjøre fred til din øvrighet og rettferdighet til din styrer.
Ndidzakupatsa golide mʼmalo mwa mkuwa, ndi siliva mʼmalo mwa chitsulo. Ndidzakupatsa mkuwa mʼmalo mwa thabwa ndi chitsulo mʼmalo mwa miyala. Olamulira ako adzakhala a mtendere. Ndidzasandutsa okulamulira kuti akhale achilungamo.
18 Det skal ikke mere høres om vold i ditt land, ikke om hærfang og ødeleggelse innen dine landemerker, og du skal kalle frelsen dine murer og lovsangen dine porter.
Ziwawa sizidzamvekanso mʼdziko lako, bwinja kapena chiwonongeko sizidzapezeka mʼdziko lako, ndidzakhala malinga ako okuteteza ndipo udzanditamanda.
19 Solen skal ikke mere være ditt lys om dagen, og månen skal ikke skinne og lyse for dig; men Herren skal være et evig lys for dig, og din Gud skal være din herlighet.
Sipadzakhala dzuwa kuti likuwunikire, kapena mwezi kuti uwunikire usiku, pakuti Yehova ndiye adzakhale kuwunika kwako kwa muyaya, ndipo Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.
20 Din sol skal ikke mere gå ned, og din måne ikke miste sitt skinn; for Herren skal være et evig lys for dig, og din sorgs dager skal være til ende.
Dzuwa lako silidzalowanso, ndipo mwezi wako sudzazimiriranso; Yehova adzakhala kuwunika kwako kwamuyaya, ndipo masiku a mavuto ako adzatha.
21 Og ditt folk - de er alle sammen rettferdige; til evig tid skal de eie landet; de er jo en kvist som jeg har plantet, et verk av mine hender til min ære.
Ndipo anthu ako onse adzakhala olungama ndipo dzikolo lidzakhala lawo mpaka muyaya. Iwo ndi mphukira imene Ine ndayidzala, ntchito ya manja anga, kuti aonetse ulemerero wanga.
22 Den minste skal bli til tusen, og den ringeste til et veldig folk; jeg, Herren, jeg vil la det skje hastig, i sin tid.
Kabanja kakangʼono kadzasanduka fuko, kafuko kakangʼono kudzasanduka mtundu wamphamvu. Ine ndine Yehova, nthawi yake ikafika ndidzazichita zimenezi mofulumira.”