< Esaias 44 >
1 Men hør nu, Jakob, min tjener, og Israel, som jeg har utvalgt!
Yehova akuti, “Mvera tsopano, iwe Yakobo, mtumiki wanga, Israeli, amene ndinakusankha.
2 Så sier Herren, som skapte dig og dannet dig fra mors liv, som hjelper dig: Frykt ikke, min tjener Jakob, Jesurun som jeg har utvalgt!
Yehova amene anakupanga iwe, anakuwumba iwe mʼmimba ya amayi ako, ndi amene adzakuthandiza iwe. Iye akuti, Usachite mantha, iwe Yakobo, mtumiki wanga, Yesuruni, amene ndinakusankha.
3 For jeg vil øse vann over det tørste og strømmer over det tørre; jeg vil utgyde min Ånd over din sæd og min velsignelse over dine spirer,
Pakuti ndidzathira madzi pa nthaka yowuma, ndi kuyendetsa mitsinje mʼdziko lowuma; ndidzatumiza Mzimu wanga pa ana anu, ndi kutsitsa madalitso anga pa zidzukulu zanu.
4 så de vokser op som iblandt gress, som piletrær ved bekkene.
Iwo adzakula ngati udzu wothirira bwino ndi ngati bango lomera mʼmbali mwa mitsinje ya madzi oyenda.
5 En skal si: Jeg hører Herren til, en annen skal kalle sig med Jakobs navn, en tredje skal skrive med sin hånd: Jeg hører Herren til, og Israel skal han bruke som hedersnavn.
Wina adzanena kuti, ‘Ine ndine wa Yehova;’ wina adzadzitcha yekha wa banja la Yakobo; winanso adzalemba pa dzanja lake, ‘Wa Yehova’ ndipo adzadzitcha wa banja la Israeli.
6 Så sier Herren, Israels konge og gjenløser, Herren, hærskarenes Gud: Jeg er den første, og jeg er den siste, og foruten mig er det ingen Gud.
“Yehova Mfumu ndi Mpulumutsi wa Israeli, Yehova Wamphamvuzonse akuti: Ine ndine woyamba ndi wotsiriza; palibenso Mulungu wina koma Ine ndekha.
7 Hvem forkynner som jeg det som skal skje? La ham kunngjøre og legge frem for mig det han har forkynt, like siden jeg skapte oldtidens ætt! Og det som i fremtiden skal komme - la dem kunngjøre det!
Ndani nanga angafanane ndi Ine? Muloleni kuti ayankhule. Muloleni andifotokozere ndi kundiyalira bwino lomwe zimene zinachitika kuyambira pamene ndinkakhazikitsa anthu anga akalekale, ndi ziti zimene zidzachitike; inde, muloleni alosere zimene zikubwera.
8 Frykt ikke og forferdes ikke! Har jeg ikke for lenge siden latt dig høre det og forkynt dig det? I er mine vidner. Er det nogen Gud foruten mig? Det er ingen klippe, jeg kjenner ingen.
Musanjenjemere, musachite mantha. Kodi sindinakuwuzeni zimenezi ndi kuzilosera kalekale lomwe? Inu ndinu mboni zanga. Kodi aliponso Mulungu wina kupatula Ine? Ayi, palibe Thanthwe linanso limene sindikulidziwa.”
9 De som lager utskårne billeder, er alle sammen intet, og deres kjære guder er til ingen nytte, og de som gir dem vidnesbyrd, ser ikke og skjønner ikke, så de skal bli til skamme.
Onse amene amapanga mafano ngachabe, ndipo milungu imene amayilemekeza ndi yopanda phindu. Iwo amene amapembedza mafano ndi wosaona; ndipo sazindikira kanthu. Choncho adzawachititsa manyazi.
10 Hvem har dannet en gud og støpt et billede - til ingen nytte?
Ndani amasema mulungu ndi kuwumba fano, limene silingamupindulire?
11 Se, alle de som holder sig til det, skal bli til skamme, og mestrene selv er jo mennesker; la dem samle sig alle sammen, la dem trede frem! De skal reddes, de skal bli til skamme alle sammen.
Iye pamodzi ndi anzake onse adzawachititsa manyazi; amisiri a mafano ndi anthu chabe. Aloleni onse asonkhane ndi kuyima pabwalo la milandu; onse adzaopsedwa ndipo adzachita manyazi.
12 Smeden bruker sin meisel og arbeider ved kullild; han former billedet med hamrer, han arbeider på det med sin kraftige arm; han blir sulten under arbeidet og kraftløs, han drikker ikke vann og blir slapp.
Mmisiri wa zitsulo amatenga chitsulo ndipo amachiyika pa makala amoto; ndi dzanja lake lamphamvu amachisula pochimenya ndi nyundo. Pambuyo pake mʼmisiri uja amamva njala natha mphamvu; iye samwa madzi, ndipo amalefuka.
13 Treskjæreren spenner ut en målesnor, risser av med en stift, arbeider treet med en kniv og risser av med passer, og han lager det til som billedet av en mann, som en prektig menneskeskikkelse, til å bo i et hus.
Mmisiri wa matabwa nayenso amayeza mtengo ndi chingwe ndipo amajambula chithunzi ndi cholembera; amasema bwinobwino ndi chipangizo chake ndipo amachiwongola bwino ndi chida chake. Amachipanga ngati munthu, munthu wake wokongola kuti aliyike mʼnyumba yake yachipembedzo.
14 En gir sig til å felle sedrer, og han tar stenek og ek og velger sig ut et blandt skogens trær; han planter en furu, og regnet får den til å vokse.
Amagwetsa mitengo ya mkungudza, mwinanso amatenga mtengo wa payini kapena wa thundu nʼkudzisankhira mtengo wabwino pakati pa mitengo ya mʼnkhalango, ndipo amadzala mtengo wa payini ndi kuwuleka kuti ukule ndi mvula.
15 Og så tjener treet mennesket til brenne; han tar av det og varmer sig med det; han fyrer også og baker brød med det; han gjør også en gud av det, som han tilbeder, han gjør et utskåret billede av det, som han faller ned for.
Mitengoyo munthu amachitako nkhuni; nthambi zina amasonkhera moto wowotha, amakolezera moto wophikira buledi ndi mbali ina ya mtengowo amapangira mulungu ndipo amapembedza; iye amapanga fano ndi kumaligwadira.
16 Halvdelen av det brenner han op med ild; med halvdelen av det tillager han det kjøtt han skal ete, han steker en stek og metter sig; han varmer sig også og sier: Å! Jeg er blitt varm, jeg kjenner ilden.
Chigawo china cha mtengowo amasonkhera moto wowotcherapo nyama imene amadya, nakhuta. Iye amawotha motowo ndipo amanena kuti, “Aa! Ndikumva kutentha; pano pali moto.”
17 Resten av det gjør han til en gud, til sitt utskårne billede; han faller ned for det og tilbeder det; han ber til det og sier: Frels mig, for du er min gud!
Chigawo chotsala amapanga kamulungu, fano lake limenelo; amaligwadira ndi kulipembedza. Amapemphera kwa fanolo ndipo amanena kuti, “Iwe ndiwe mulungu wanga, ndipulumutse.”
18 De skjønner intet og forstår intet; for han har klint deres øine til, så de ikke ser, forherdet deres hjerter, så de ikke forstår.
Anthu otere sadziwa kanthu, samvetsa kanthu kalikonse; maso awo ndi omatirira ndipo sangathe kuona, ndipo mitu yawo ndi yogontha kotero sangathe kumvetsa.
19 Han tar sig det ikke til hjerte, og han har ikke klokskap og forstand nok til å si: Halvdelen av det har jeg brent op med ild, jeg har også bakt brød over glørne av det, jeg steker kjøtt og eter, og resten av det skulde jeg gjøre til en vederstyggelighet, for en treklubbe skulde jeg falle ned!
Palibe amene amayima nʼkulingalira. Palibe wanzeru kapena womvetsa zinthu bwino woti nʼkunena kuti, chigawo china cha mtengowo ndinasonkhera moto; pa makala ake ndinaphikira buledi, ndinawotchapo nyama ndipo ndinadya. Chigawo chotsalachi ndipangire chinthu chonyansachi. Kodi ndidzagwadira mtengo?
20 Den som holder sig til det som bare er aske, ham har et dåret hjerte ført vill, og han redder ikke sin sjel og sier ikke: Er det ikke løgn det jeg har i min høire hånd?
Munthu wotere ali ngati wodya phulusa, maganizo ake opusa amusocheretsa; motero kuti sangathe kudzipulumutsa yekha kapena kudzifunsa kuti, “Kodi chinthu chili mʼmanja mwangachi si chabodza?”
21 Kom dette i hu, Jakob! Kom det i hu, Israel! For du er min tjener; jeg har dannet dig, du er min tjener; Israel, du skal ikke bli glemt av mig.
Yehova akuti, “Iwe Yakobo, kumbukira zinthu izi popeza kuti ndiwe mtumiki wanga, iwe Israeli. Ine ndinakupanga iwe, ndiwe mtumiki wanga; iwe Israeli, sindidzakuyiwala.
22 Jeg utsletter dine overtredelser som en tåke og dine synder som en sky; vend om til mig, for jeg gjenløser dig!
Ndachotsa zolakwa zako ngati mitambo, ndi machimo ako ngati nkhungu ya mmawa. Bwerera kwa Ine, popeza ndakupulumutsa.”
23 Juble, I himler! For Herren utfører sitt verk. Rop med fryd, I jordens dybder! Bryt ut i jubel, I fjell, du skog, hvert tre i dig! For Herren gjenløser Jakob, og på Israel vil han åpenbare sin herlighet.
Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga, pakuti Yehova wachita zimenezi; fuwula, iwe dziko lapansi. Imbani nyimbo, inu mapiri, inu nkhalango ndi mitengo yonse, chifukwa Yehova wawombola Yakobo, waonetsa ulemerero wake mwa Israeli.
24 Så sier Herren, din gjenløser, han som dannet dig fra mors liv: Jeg er Herren, som gjør alle ting, som utspente himmelen alene, som bredte ut jorden uten hjelp fra nogen,
Yehova Mpulumutsi wanu, amene anakuwumbani mʼmimba ya amayi anu akuti: “Ine ndine Yehova, amene anapanga zinthu zonse, ndinatambasula ndekha zinthu zakuthambo, ndinayala ndekha dziko lapansi.
25 som gjør snakkernes tegn til intet og spåmennene til dårer, som driver de vise tilbake og gjør deres visdom til dårskap,
Ndine amene ndinalepheretsa mipingo ya anthu onyenga, ndipo ndimapusitsa owombeza mawula. Ndimasokoneza anthu a nzeru, ndi kuonetsa kuti nzeru zawo nʼzopusa.
26 som stadfester sin tjeners ord og fullbyrder sine sendebuds råd, som sier om Jerusalem: Der skal bo folk, og om Judas byer: De skal bygges op igjen, deres ruiner vil jeg reise,
Ndine amene ndimatsimikiza mawu a atumiki ake ndi kukwaniritsa zimene analosera amithenga ake. “Ndine amene ndinanena za Yerusalemu kuti mudzakhalanso anthu. Ndinanenanso za mizinda ya Yuda kuti idzamangidwanso. Za mabwinja awo ndinanena kuti ndidzawawutsanso.
27 som sier til dypet: Bli tørt, dine strømmer vil jeg tørke ut,
Ndine amene ndinawuza nyanga yayikulu kuti, ‘Uma’ ndipo ndidzawumitsa mitsinje yako.
28 som sier om Kyros: Han er min hyrde; all min vilje skal han fullbyrde og si om Jerusalem: Det skal bygges op igjen, og templet skal bli grunnlagt.
Ndine amene ndinanena kwa Koresi kuti, ‘Iye ndiye mʼbusa wanga,’ ndipo adzachita zonse zimene ndikufuna; iye adzalamula kuti, ‘Yerusalemu amangidwenso’ ndi kuti, ‘Maziko a Nyumba ya Mulungu ayikidwenso.’”