< Esaias 39 >
1 På den tid sendte Merodak Baladan, Baladans sønn, kongen i Babel, brev og gaver til Esekias, da han hørte at han hadde vært syk og var blitt frisk igjen.
Nthawi imeneyo Merodaki-Baladani, mwana wa Baladani mfumu ya ku Babuloni anatumiza nthumwi kwa Hezekiya nawapatsira makalata ndi mphatso, pakuti anamva za kudwala kwake ndi kuti anachira.
2 Esekias gledet sig over dem og lot dem få se sitt skattkammer, sølvet og gullet og krydderiene og den kostbare olje og hele sitt våbenhus og alt det som fantes i hans skattkammere; det var ikke den ting Esekias ikke lot dem få se i sitt hus og i hele sitt rike.
Hezekiya anawalandira mwasangala ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo siliva, golide, zokometsera zakudya, mafuta abwino kwambiri, zida zonse zankhondo ndiponso zonse zimene zinkapezeka mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Panalibe kanthu kalikonse ka mʼnyumba yaufumu kapena mu ufumu wake onse kamene sanawaonetse.
3 Da kom profeten Esaias til kong Esekias og sa til ham: Hvad sa disse menn, og hvorfra kommer de til dig? Esekias svarte: De er kommet til mig fra et land langt borte, fra Babel.
Tsono mneneri Yesaya anapita kwa mfumu Hezekiya ndipo anamufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani chiyani, ndipo anachokera kuti?” Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”
4 Og han sa: Hvad fikk de se i ditt hus? Esekias svarte: Alt det som er i mitt hus, har de fått se; det var ikke den ting jeg ikke lot dem få se i mine skattkammer.
Mneneri anafunsanso kuti, “Kodi mʼnyumba yanu yaufumu anaonamo chiyani?” Hezekiya anati, “Anaona chilichonse cha mʼnyumba yanga yaufumu. Palibe ndi chimodzi chomwe za mʼnyumba yosungiramo chuma changa chimene sindinawaonetse.”
5 Da sa Esaias til Esekias: Hør Herrens, hærskarenes Guds ord:
Pamenepo Yesaya anati kwa Hezekiya, “Imvani mawu a Yehova Wamphamvuzonse:
6 Se, de dager kommer da alt det som er i ditt hus, og alle de skatter dine fedre har samlet like til denne dag, skal føres bort til Babel; det skal ikke bli nogen ting tilbake, sier Herren.
Yehova akuti, nthawi idzafika ndithu pamene zonse za mʼnyumba mwanu ndi zonse zimene makolo anu anazisonkhanitsa mpaka lero lino, zidzatengedwa kupita nazo ku Babuloni. Sipadzatsalapo ndi kanthu kamodzi komwe.
7 Og blandt dine sønner som skal utgå av dig, som du skal avle, skal det være nogen som blir tatt til hoffmenn i kongen av Babels palass.
Ndipo ena mwa ana anu, obala inu amene adzatengedwanso, ndipo adzawasandutsa adindo ofulidwa mʼnyumba ya mfumu ya ku Babuloni.”
8 Da sa Esekias til Esaias: Det Herrens ord som du har talt, er godt. Så sa han: Det skal jo være fred og trygghet i mine dager.
Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhula ndi abwino.” Ponena izi iye ankaganiza kuti, “Padzakhala mtendere ndi chitetezo masiku a moyo wanga onse.”