< Esaias 35 >
1 Ørkenen og det tørre land skal glede sig, og den øde mark skal juble og blomstre som en lilje.
Chipululu ndi dziko lopanda madzi zidzasangalala; dziko lowuma lidzakondwa ndi kuchita maluwa.
2 Den skal blomstre og juble, ja juble og synge med fryd; Libanons herlighet er gitt den, Karmels og Sarons prakt; de skal se Herrens herlighet, vår Guds prakt.
Dzikolo lidzakhala ndi maluwa ochuluka lidzasangalala kwambiri ndi kufuwula mwachimwemwe. Lidzakhala ndi ulemerero monga wa ku mapiri a ku Lebanoni, maonekedwe ake wokongola adzakhala ngati a ku Karimeli ndi a ku Saroni. Aliyense adzaona ulemerero wa Yehova, ukulu wa Mulungu wathu.
3 Styrk de slappe hender og gjør de vaklende knær sterke!
Limbitsani manja ofowoka, limbitsani mawondo agwedegwede;
4 Si til de urolige hjerter: Vær frimodige, frykt ikke! Se, der er eders Gud! Hevnen kommer, Guds gjengjeldelse, han kommer selv og frelser eder.
nenani kwa a mitima yamantha kuti; “Limbani mtima, musachite mantha; Mulungu wanu akubwera, akubwera kudzalipsira; ndi kudzabwezera chilango adani anu; akubwera kudzakupulumutsani.”
5 Da skal de blindes øine åpnes, og de døves ører oplates;
Pamenepo maso a anthu osaona adzapenyanso ndipo makutu a anthu osamva adzatsekuka.
6 da skal den lamme springe som en hjort, og den stummes tunge juble. For kilder bryter frem i ørkenen, og bekker i ødemarken,
Anthu olumala adzalumpha ngati mbawala, ndipo osayankhula adzayimba mokondwera. Akasupe adzatumphuka mʼchipululu ndipo mitsinje idzayenda mʼdziko lowuma,
7 og det glødende sandhav skal bli til en sjø, og det tørste land til vannrike kilder; på det sted hvor sjakalene hvilte, vokser siv og rør.
mchenga wotentha udzasanduka dziwe, nthaka yowuma idzasanduka ya akasupe. Pamene panali mbuto ya ankhandwe padzamera udzu ndi bango.
8 Og der skal være en ryddet vei, og den skal kalles den hellige vei, ingen uren skal gå på den, men den hører hans folk til; ingen veifarende, ikke engang dårer, skal fare vill.
Ndipo kumeneko kudzakhala msewu waukulu; ndipo udzatchedwa Msewu Wopatulika. Anthu odetsedwa sadzayendamo mʼmenemo; zitsiru sizidzasochera mʼmenemo.
9 Der skal det ingen løve være, og intet rovdyr skal komme op på den, de skal ikke finnes der; men de gjenløste skal ferdes der.
Kumeneko sikudzakhala mkango, ngakhale nyama yolusa sidzafikako; sidzapezeka konse kumeneko. Koma okhawo amene Yehova anawapulumutsa adzayenda mu msewu umenewu.
10 Og Herrens forløste skal vende tilbake og komme til Sion med frydesang, og evig glede er det over deres hode; fryd og glede skal de nå, og sorg og sukk skal fly.
Iwo amene Yehova anawawombola adzabwerera. Adzalowa mu mzinda wa Ziyoni akuyimba; kumeneko adzakondwa mpaka muyaya. Adzakutidwa ndi chisangalalo ndi chimwemwe, ndipo chisoni ndi kudandaula zidzatheratu.