< Esaias 27 >
1 På den tid skal Herren med sitt sverd, det hårde og store og sterke, hjemsøke Leviatan, den lettfarende drage, og Leviatan, den buktede drage, og han skal drepe uhyret som er i havet.
Tsiku limenelo, Yehova ndi lupanga lake lakuthwa, lalikulu ndi lamphamvu, adzalanga Leviyatani chinjoka chothawa chija, Leviyatani chinjoka chodzikulunga; adzapha chirombo choopsa cha mʼnyanja.
2 På den tid skal de synge: Der er en edel vingård; syng om den!
Tsiku limenelo Yehova adzati, “Tidzayimba nyimbo ya munda wamphesa wobereka bwino:
3 Jeg, Herren, er dens vokter, hvert øieblikk vanner jeg den; forat ikke nogen skal hjemsøke den, vokter jeg den dag og natt.
Ine, Yehova, ndimawuyangʼanira; ndimawuthirira nthawi zonse. Ndimawulondera usana ndi usiku kuti wina angawononge.
4 Vrede har jeg ikke mot den. Hadde jeg torner og tistler mot mig i krig, da vilde jeg gå løs på dem og brenne dem op alle sammen,
Ine sindinakwiye. Ngati mkandankhuku ndi minga zikanaoneka ndikanalimbana nazo! Ndikachita nazo nkhondo; ndikanazitentha zonse ndi moto.
5 dersom de da ikke skulde søke vern hos mig, gjøre fred med mig, ja, gjøre fred med mig.
Koma ngati apo ayi, abweretu kwa Ine adani angawo kuti ndidzawateteze; apangane nane za mtendere, ndithu, apangane nane za mtendere.”
6 I de kommende dager skal Jakob skyte røtter, Israel blomstre og få skudd, og de skal fylle jorderike med frukt.
Masiku akubwerawo Yakobo adzazika mizu, Israeli adzaphukira ndi kuchita maluwa, ndipo adzadzaza dziko lonse lapansi ndi zipatso.
7 Har vel Herren slått Israel så hårdt som han slo den som slo ham? Eller blev han drept således som hans fiender blev drept?
Kodi Yehova anakantha Israeli ngati momwe anakanthira anthu amene anazunza Israeli? Kapena kodi Yehova anapha Israeli ngati mmene anthu ena anaphera Israeli?
8 Med måte gikk du i rette med folket da du jaget det fra dig. Herren drev det bort med sitt hårde vær på østenvindens dag.
Yehova mwawalanga powapirikitsa ndi kuwatumiza ku ukapolo, mwawachotsa ndi mpweya wanu woopsa, monga zimachitikira pa tsiku la mkuntho wochokera kummawa.
9 Derfor blir Jakobs misgjerning utsonet, og det at hans synd blir tatt bort, gir full frukt, når alle alterstener blir knust som kalkstener, og Astarte-billeder og solstøtter ikke reiser sig mere.
Yehova adzakhululuka kulakwa kwa Yakobo. Iwo adzaonetsa kuti alapadi pamene adzaphwanya miyala yonse ya guwa lachikunja, ngati mmene anthu amaphwanyira miyala yanjereza mpaka kukhala ngati fumbi lokhalokha. Sipadzapezekanso mafano a Asera kapena maguwa ofukiza lubani.
10 For den faste by ligger forlatt, en folketom bolig, øde som ørkenen. Kalver beiter der; der hviler de og fortærer dens kvister;
Mzinda wamalinga uja wasanduka bwinja, wasanduka malo osiyidwa, ndi kutayidwa ngati chipululu; kumeneko amadyetselako ana angʼombe kumeneko zimapumulako ziweto ndi kumwetula nthambi za mitengo kotheratu.
11 når dens grener blir tørre, brytes de av, kvinner kommer og gjør op ild med dem. For dette er ikke noget forstandig folk; derfor forbarmer dets skaper sig ikke over det, og han som dannet det, er ikke nådig mot det.
Pamene nthambi za mitengoyo zauma, zimathyoka ndipo amayi amabwera nazitola ndi kuzisandutsa nkhuni. Pakuti awa ndi anthu opanda nzeru; kotero Mulungu amene anawapanga sadzachitira chisoni, ndipo Mlengi wawo sawakomera mtima.
12 Og det skal skje på den tid at Herren skal slå ned frukter like fra Storelven til Egyptens bekk, og I, Israels barn, I skal sankes op en for en.
Tsiku limenelo Yehova adzasonkhanitsa pamodzi anthu ake mmodzimmodzi kumalo opunthira tirigu, kuchokera ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku mtsinje wa ku Igupto.
13 Og det skal skje på den tid at de skal støte i en stor basun, og da skal de komme de fortapte i Assurs land og de fordrevne i Egyptens land, og de skal tilbede Herren på det hellige berg i Jerusalem.
Ndipo tsiku limenelo lipenga lalikulu lidzalira. Amene akuzunzika ku Asiriya iwo amene ali ku ukapolo ku Igupto adzabwera ndi kudzalambira Yehova pa phiri lopatulika mu Yerusalemu.