< Esaias 23 >

1 Utsagn om Tyrus. Jamre eder, I Tarsis-skib! For det er ødelagt, så der ikke mere er hus, og I ikke mere kan komme hjem; fra Kittims land blir det kunngjort for dem.
Uthenga wonena za Turo: Lirani mofuwula, inu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi: pakuti mzinda wa Turo wawonongedwa ndipo mulibe nyumba kapena dooko. Zimenezi anazimva pochokera ku Kitimu.
2 Bli stille, I som bor på kysten som Sidons sjøfarende kjøbmenn opfylte!
Khalani chete inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja, inu amalonda a ku Sidoni, iwe amene unalemera ndi anthu oyenda pa nyanja.
3 Av Sikors sæd, av Nilens høst, som blev ført frem over det store hav, gjorde det sig vinning, og det var et marked for folkene.
Pa nyanja zazikulu panabwera tirigu wa ku Sihori; zokolola za ku Nailo, ndipo munachita malonda ndi anthu a mitundu ina.
4 Skam dig, Sidon! - For havet, havets festning sier: Jeg har ikke hatt fødselsveer, heller ikke født, heller ikke opfødd unge menn eller fostret jomfruer.
Chita manyazi, iwe Sidimu pakuti nyanja yayankhula, linga la ku nyanja (Turo) layankhula kuti, “Sindinamvepo zowawa za kubereka kapena kuberekapo mwana; sindinalerepo ana aamuna kapena kulera ana aakazi.”
5 Når de får høre om dette i Egypten, skal de skjelve ved ryktet om Tyrus.
Mawuwa akadzamveka ku Igupto, iwo adzachita mantha akadzamva kuti Turo wawonongeka.
6 Far over til Tarsis, jamre eder, I som bor på kysten!
Wolokerani ku Tarisisi, lirani mofuwula, inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja.
7 Er dette eders jublende by, som blev til i fordums dager, hvis føtter bærer den bort til å bo som fremmed i det fjerne?
Kodi uwu si mzinda wachisangalalo uja, mzinda wakalekale, umene anthu ake ankapita kukakhala ku mayiko akutali?
8 Hvem har besluttet dette mot Tyrus, mot henne som delte ut kroner, hun hvis kjøbmenn var fyrster, hvis kremmere var stormenn på jorden?
Kodi ndani anakonza zimenezi kuti zigwere Turo, mzinda umene unakhazikitsa mizinda ina, mzinda umene amalonda ake ndi akalonga ndi otchuka pa dziko lapansi?
9 Herren, hærskarenes Gud, har besluttet det for å vanhellige all stolt prakt, for å vanære alle jordens store.
Yehova Wamphamvuzonse anakonza zimenezi kuti athetse kunyada kwawo ndi kutsitsa anthu otchuka a pa dziko lapansi.
10 Bred dig ut over ditt land som strømmen, du Tarsis' datter! Det er intet bånd mere.
Mubalalike mʼdziko mwanu ngati mtsinje wa Nailo inu anthu a ku Tarisisi, pakuti mulibenso chokutetezani.
11 Han har rakt ut sin hånd over havet, han har fått kongeriker til å skjelve; Herren har befalt å ødelegge Kana'ans faste borger.
Yehova watambasula dzanja lake kuloza ku nyanja ndipo wagwedeza maufumu ake. Iye walamula kuti Kanaani agwetse malinga ake.
12 Han sa: Du skal ikke mere bli ved å juble, du voldtatte jomfru, Sidons datter! Bryt op, dra over til Kittim! Heller ikke der skal du finne ro.
Iye anati, “Simudzakondwanso konse, inu anthu opanikizidwa a ku Sidoni, tsopano wamphwanyidwa! “Ngakhale muwolokere ku Kitimu, kumeneko simukapezako mpumulo.”
13 Se, kaldeernes land, dette folk som fordum ikke var til, de hvis land Assur har gjort til bolig for ørkenens dyr, de reiser sine beleiringstårn, omstyrter dets palasser og gjør det til en grushaug.
Onani dziko la Ababuloni, anthu amenewa tsopano atheratu! Asiriya asandutsa Turo kukhala malo a zirombo za ku chipululu; anamanga nsanja zawo za nkhondo, anagumula malinga ake ndipo anawasandutsa bwinja.
14 Jamre eder, I Tarsis-skib! For ødelagt er eders faste borg.
Lirani mofuwula, inu anthu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi; chifukwa malinga ako agwetsedwa!
15 På den tid skal Tyrus bli glemt i sytti år, så lenge som en konges dager; når sytti år er til ende, skal det gå Tyrus som det heter i visen om skjøgen:
Pa nthawi imeneyo Turo adzayiwalika pa zaka 70, amene ndi masiku a moyo wa mfumu. Koma potsiriza pa zaka 70 zimenezi, Turo adzakhala ngati mkazi wachiwerewere woyimbidwa mu nyimbo:
16 Ta din citar, gå omkring i byen, du glemte skjøge! Spill det beste du kan, syng vise på vise, så folk kan komme dig i hu!
“Tenga zeze wako uzungulire mzinda, iwe mkazi wachiwerewere woyiwalika; imba zeze mokometsera, imba nyimbo zambiri, kuti anthu akukumbukire.”
17 Når de sytti år er til ende, da skal Herren ta sig av Tyrus, og det skal atter få ta imot horelønn, og det skal drive utukt med alle verdens riker over den vide jord.
Pakutha pa zaka 70, Yehova adzachitapo kanthu pa Turo. Iye adzabwerera ku ntchito yake yakale monga mkazi wachiwerewere ndipo adzachita zachiwerewere ndi maufumu onse a dziko lapansi.
18 Men dets vinning og dets horelønn skal være helliget til Herren, den skal ikke legges op og ikke gjemmes; for de som bor for Herrens åsyn, skal få dets vinning og bruke den til å ete sig mette og klæ sig i prektige klær for.
Koma phindu lake ndi malipiro ake adzazipereka kwa Yehova; sadzazikundika kapena kuzisunga. Phindu lake lidzapita kwa mtumiki wa Yehova kuti agule zakudya zambiri ndi zovala zokongola.

< Esaias 23 >