< Esaias 20 >

1 I det år da Tartan kom til Asdod, da assyrerkongen Sargon sendte ham dit, og han stred imot Asdod og inntok byen -
Mʼchaka chimene mkulu wankhondo wotumidwa ndi mfumu ya ku Asiriya, anabwera ku Asidodi ndi kuwuthira nkhondo ndi kuwulanda,
2 på den tid talte Herren ved Esaias, Amos' sønn, og sa: Du skal løse hårkjortelen av dine lender og dra skoen av din fot! Og han gjorde så og gikk naken og barfotet.
nthawi imeneyo Yehova anawuza Yesaya mwana wa Amozi kuti, “Pita kavule chiguduli ndi nsapato zako.” Ndipo iye anaterodi, ankangoyenda wamaliseche ndiponso wopanda nsapato.
3 Da sa Herren: Likesom min tjener Esaias har gått naken og barfotet og nu i tre år har vært et tegn og varsel om Egypten og Etiopia,
Kenaka Yehova anati, “Monga momwe mtumiki wanga Yesaya wakhala akuyendera wamaliseche ndiponso wopanda nsapato kwa zaka zitatu ngati chizindikiro ndi chenjezo kwa dziko la Igupto ndi Kusi,
4 således skal kongen i Assyria føre bort fangene fra Egypten og de landflyktige fra Etiopia, de unge og de gamle, nakne og barfotede og med bar bak, til vanære for Egypten.
momwemonso mfumu ya ku Asiriya idzatenga ukapolo anthu a ku Igupto ndi a ku Kusi, anyamata ndi okalamba. Iwo adzakhala amaliseche ndi opanda nsapato, matako ali pa mtunda. Zimenezi zidzachititsa manyazi Igupto.
5 Da skal de forferdes og ha skam av Etiopia, som de satte sitt håp til, og av Egypten, som de var stolte av.
Amene ankadalira Kusi, ndiponso amene ankadzitukumula chifukwa cha Igupto adzakhumudwa ndi kuchita manyazi.
6 På den tid skal de som bor her i kystlandet, si: Se, således er det gått dem vi satte vårt håp til, dem som vi tydde til efter hjelp, for å fries fra kongen i Assyria. Hvorledes skal da vi komme unda?
Tsiku limenelo anthu amene amakhala mʼmbali mwa nyanja adzati, ‘Taonani zomwe zawachitikira amene ife tinkawadalira, amene ife tinkathawirako kuti atithandize ndi kutipulumutsa kwa mfumu ya ku Asiriya! Nanga ife tidzapulumuka bwanji?’”

< Esaias 20 >