< Esaias 16 >
1 Send landsherren de lam han skal ha, fra Sela gjennem ørkenen til Sions datters berg!
Anthu a ku Mowabu atumiza mphatso za ana ankhosa onenepa, kuchokera ku Sela kudutsa chipululu mpaka kukafika ku phiri la Ziyoni.
2 Som flagrende fugler, lik unger som er jaget bort fra redet, skal Moabs døtre være ved Arnons ferjesteder.
Monga momwe mbalame zimawulukira uku ndi uku akazimwaza mʼchisa, momwemonso akazi a ku Mowabu akuyendayenda ku madooko a Arinoni.
3 Gi råd, finn utvei for oss! La din skygge midt på dagen være som natten! Skjul de fordrevne, forråd ikke dem som flykter!
Amowabu aja anawuza a ku Yuda kuti, “Tiwuzeni chochita, gamulani zoti tichite. Inu mutiteteze kwa adani anthu. Mukhale ngati mthunzi wathu dzuwa lili pa liwombo. Mutibise, musatipereke ife othawa nkhondo kwa adani athu.
4 La mine fordrevne barn få herberge hos dig! Vær et skjul for Moab mot ødeleggeren! For det er forbi med voldsmannen, ødeleggelsen får ende, undertrykkerne blir borte av landet.
Lolani kuti anthu othawa nkhondo a ku Mowabu azikhala pakati panu; mukhale populumukira pawo kwa wowonongayo.” Nthawi idzafika ndipo wozunzayo sadzakhalaponso, kuwononga kudzaleka; waukaliyo adzachoka mʼdzikomo.
5 Så skal tronen bli grunnfestet ved miskunnhet, og en konge skal sitte trygt på den i Davids telt, en fyrste som søker rett og fremmer rettferdighet.
Mpando waufumu udzakhazikitsidwa mwachikondi; mmodzi mwa zidzukulu za Davide adzakhalapo mokhulupirika. Iyeyo poweruza adzatsata chilungamo ndipo adzalimbikitsa kuchita zachilungamo.
6 Vi har hørt om Moabs veldige overmot, om dets stolthet, dets overmot og dets storaktighet, dets tomme skryt.
Tinamva kuti Mowabu anadzikuza kwambiri. Kunyada kwawo ndi kunyogodola kwawo ndi kudzitama kwawo, zonse ndi zopanda phindu.
7 Derfor skal Moab klage over Moab, alle skal klage; over Kir-Haresets druekaker skal I sukke i dyp sorg.
Nʼchifukwa chake Amowabu akulira kwambiri; iwo akulirira dziko lawo. Akubuma momvetsa chisoni chifukwa cha makeke a mphesa a ku Kiri Hareseti.
8 For Hesbons marker er visnet, og Sibmas vintre, hvis edle ranker slo folkenes herskere til jorden; de nådde like til Jaser og forvillet sig ut i ørkenen; dets kvister bredte sig ut og gikk over havet.
Minda ya ku Hesiboni yauma, minda ya mpesa ya ku Sibina yaguga. Atsogoleri a mitundu ina anapondaponda minda ya mpesa wabwino, imene nthambi zake zinakafika ku Yazeri, mpaka kutambalalira ku chipululu. Mizu yake inakafika mpaka ku tsidya la nyanja.
9 Derfor gråter jeg med Jaser over Sibmas vintre; jeg vanner dig med mine tårer, Hesbon, og dig El'ale! For over din frukthøst og over din kornhøst faller frydeskrik.
Kotero Ine ndikulira, monga mmene akulirira anthu a ku Yazeri, chifukwa cha minda ya mpesa ya ku Sibima. Inu anthu a ku Hesiboni, inu anthu a ku Eleali, ndikukunyowetsani ndi misozi! Mwalephera kupeza zokolola, chifukwa cha nkhondo imene inawononga zokolola zonse.
10 Og glede og fryd tas bort fra frukthavene, og i vingårdene lyder ingen frydesang, intet jubelrop; ingen treder vin i persekarene; frydeskriket gjør jeg ende på.
Chimwemwe ndi chisangalalo zalekeka ku minda yanu ya zipatso; palibe amene akuyimba kapena kufuwula mʼminda ya mpesa; palibe amene akupsinya vinyo ku malo opsinyira mphesa, pakuti ndathetsa kufuwula.
11 Derfor bruser mitt indre for Moab som en citar, og mitt hjerte for Kir-Heres.
Chifukwa chake moyo wanga ukulira ngati pangwe kulirira Mowabu, mtima wanga ukubuwula chifukwa cha Kiri Hareseti.
12 Og når Moab har møtt frem på offerhaugen og trettet sig ut der, og det går til sin helligdom for å bede, da utretter det intet.
Ngakhale anthu a ku Mowabu apite ku malo awo achipembedzo koma amangodzitopetsa ndi kutaya nthawi chabe chifukwa sizidzatheka.
13 Dette er det ord som Herren fordum talte mot Moab.
Awa ndi mawu amene Yehova wayankhula kale zokhudza Mowabu.
14 Men nu taler Herren og sier: Innen tre år, således som en dagarbeider regner årene, skal Moabs herlighet være aktet ringe tross hele dets store folkemengde, og det som blir levnet, skal være lite og ringe og ikke meget verdt.
Koma tsopano Yehova akuti, “Zisanathe zaka zitatu, potsata mʼmene munthu waganyu amawerengera, ulemerero wa Mowabu udzakhala utatheratu ndipo anthu ake ambiri adzakhala atawonongeka, ndipo opulumuka ake adzakhala ochepa ndi ofowoka.”