< Esekiel 7 >
1 Og Herrens ord kom til mig, og det lød så:
Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti,
2 Og du menneskesønn! Så sier Herren, Israels Gud, til Israels land: Ende! - Enden kommer over landets fire hjørner.
“Iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuwuza dziko la Israeli kuti: “Chimaliziro! Chimaliziro chafika ku ngodya zinayi za dziko.
3 Nu kommer enden over dig, og jeg vil sende min vrede mot dig og dømme dig efter din ferd, og jeg vil la dig bøte for alle dine vederstyggeligheter.
Chimaliziro chili pa iwe tsopano. Mkwiyo wanga ndidzawuthira pa iwe. Ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako ndi kukulanga chifukwa cha zonyansa zako.
4 Jeg vil ikke vise skånsel mot dig og ikke spare dig; men jeg vil la dig bøte for din ferd, og dine vederstyggeligheter skal komme over dig selv, og I skal kjenne at jeg er Herren.
Ine sindidzakumvera chisoni kapena kukuleka. Ndidzakulanga ndithu chifukwa cha ntchito zako zoyipa komanso chifukwa cha miyambo yako yonyansa imene ili pakati pako. Pamenepo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
5 Så sier Herren, Israels Gud: Ulykke, en ulykke uten like, se, den kommer.
“Zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: “Chiwonongeko! Chiwonongeko chimene sichinamvekepo! Taona chikubwera!
6 Det kommer en ende, enden kommer, den våkner op og kommer til dig; se, det kommer.
Chimaliziro chafika! Chimaliziro chafika! Chiwonongeko chakugwera. Taona chafika!
7 Nu kommer turen til dig, du som bor i landet! Tiden kommer, dagen er nær, krigslarm er der og ikke fryderop på fjellene.
Inu anthu okhala mʼdziko, chiwonongeko chakugwerani. Nthawi yafika, tsiku layandikira; tsiku la chisokonezo osati la chimwemwe pa mapiri.
8 Nu, om en liten stund, vil jeg utøse min harme over dig og uttømme min vrede på dig og dømme dig efter din ferd, og jeg vil la dig bøte for alle dine vederstyggeligheter.
Ine ndili pafupi kukukwiyirani, ndipo ukali wanga udzathera pa iwe; Ine ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako ndiponso ndidzakulanga chifukwa cha miyambo yako yonyansa.
9 Jeg vil ikke vise skånsel og ikke spare dig; efter din ferd vil jeg gjengjelde dig, og dine vederstyggeligheter skal komme over dig selv, og I skal kjenne at jeg, Herren, slår.
Ine sindidzakumvera chisoni kapena kukuleka. Ndidzakulanga malingana ndi ntchito zako ndiponso chifukwa cha miyambo yako yonyansa pakati pako.
10 Se, dagen er der! Se, det kommer! Nu begynner det, riset blomstrer, overmotet grønnes;
“Taona, tsikulo! Taona, lafika! Chiwonongeko chako chabwera. Ndodo yaphuka mphundu za maluwa. Kudzitama kwaphuka.
11 voldsomheten reiser sig til et ris over ugudeligheten. Intet av dem, intet av deres larmende hop, intet av deres buldrende mengde, intet herlig blir tilbake iblandt dem.
Chiwawa chasanduka ndodo yowakwapulira chifukwa cha kuyipa kwawo. Palibe mwa anthu amenewo amene adzatsale. Palibe ndi mmodzi yemwe mwa unyinji wawo. Palibiretu ndipo sipadzapezeka munthu wowalira maliro.
12 Tiden kommer, dagen er nær. Kjøperen glede sig ikke, og selgeren gremme sig ikke! For det kommer brennende vrede over hele deres hop.
Nthawi yafika! Tsiku layandikira! Munthu wogula asakondwere ndipo wogulitsa asamve chisoni, popeza ukali wanga uli pa gulu lonse.
13 Selgeren skal ikke få igjen det han har solgt, om han enn er i live; for spådommen mot hele deres hop skal ikke tas tilbake, og for sin misgjernings skyld skal ingen kunne trygge sig i sitt liv.
Wogulitsa sadzazipezanso zinthu zimene anagulitsa kwa wina chinkana onse awiri akanali ndi moyo, pakuti chilango chidzagwera onsewo ndipo sichingasinthike. Chifukwa cha machimo awo, palibe aliyense amene adzapulumutsa moyo wake.
14 De støter i basun og gjør alt ferdig, men ingen drar ut til strid; for min harme er vendt mot hele deres hop.
“Lipenga lalira, ndipo zonse zakonzeka. Koma palibe ndi mmodzi yemwe amene akupita ku nkhondo, pakuti mkwiyo wanga uli pa gulu lonse.
15 Sverdet utenfor og pesten og hungeren innenfor; den som er ute på marken, skal dø ved sverdet, og den som er inne i byen, ham skal hunger og pest fortære.
Ku bwalo kuli kumenyana ndipo mʼkati muli mliri ndi njala. Anthu okhala ku midzi adzafa ndi nkhondo. Iwo okhala ku mizinda adzafa ndi mliri ndi njala.
16 Og om nogen av dem undkommer, skal de alle være på fjellene som kurrende duer i dalene, hver for sin misgjernings skyld.
Onse amene adzapulumuka ndi kumakakhala ku mapiri, azidzalira ngati nkhunda za ku zigwa. Aliyense azidzabuwula chifukwa cha machimo ake.
17 Alle hender skal synke, og alle knær skal bli som vann.
Dzanja lililonse lidzalefuka, ndipo bondo lililonse lidzalobodoka ngati madzi.
18 Og de skal binde sekk om sig, og redsel skal legge sig over dem, og alle ansikter skal dekkes av skam, og alle deres hoder skal være skallet.
Iwo adzavala ziguduli ndipo adzagwidwa ndi mantha. Adzakhala ndi nkhope zamanyazi ndipo mitu yawo adzameta mpala.
19 Sitt sølv skal de kaste på gatene, og sitt gull skal de akte for urent; deres sølv og deres gull skal ikke kunne berge dem på Herrens vredes dag; de skal ikke kunne mette sig eller fylle sin buk med det. For det har vært et anstøt til misgjerning for dem,
“Iwo adzataya siliva wawo mʼmisewu ndipo golide wawo adzakhala chinthu chonyansa. Siliva ndi golide wawo sizidzatha kuwapulumutsa pa tsiku la ukali wa Yehova. Chuma chawochi sichidzawathandiza kuthetsa njala, kapena kukhala okhuta, pakuti ndicho chinawagwetsa mʼmachimo.
20 og sine prektige smykker som er laget av det, har de brukt til storaktighet, og sine vederstyggelige billeder, sine avskyelige avguder har de gjort av det; derfor gjør jeg det til urenhet for dem.
Iwo ankanyadira zodzikongoletsera zawo zamakaka ndipo ankazigwiritsa ntchito kupanga mafano awo onyansa ndi zonyansa zawo zina. Nʼchifukwa chake Ine ndidzazisandutsa kukhala zowanyansa.
21 Og jeg vil gi det i de fremmedes hånd som rov og til jordens ugudelige som hærfang, og de skal vanhellige det;
Ndidzazipereka kwa alendo kuti azifunkhe. Anthu oyipa a dziko lapansi adzazilanda ndi kudziyipitsa.
22 Og jeg vil vende mitt åsyn bort fra dem, og de skal vanhellige min skatt; røvere skal komme inn over den og vanhellige den.
Ine ndidzawalekerera anthuwo ndipo adzayipitsa malo anga apamtima. Adzalowamo ngati mbala ndi kuyipitsamo.
23 Gjør lenken ferdig! For landet er fullt av bloddommer, og byen er full av vold.
“Konzani maunyolo, chifukwa dziko ladzaza ndi anthu opha anzawo ndipo mzinda wadzaza ndi chiwawa.
24 Og jeg vil la de verste av hedningene komme, og de skal ta deres hus i eie, og jeg vil gjøre ende på de frekkes stolthet, og deres helligdommer skal vanhelliges.
Ndidzabweretsa mitundu ya anthu oyipitsitsa kuti idzalande nyumba zawo. Ndidzathetsa kunyada kwa anthu amphamvu pamene anthu akunja adzalowa mʼmalo awo achipembedzo ndi kuyipitsamo.
25 Det skal komme redsel, og de skal søke frelse, men der er ingen.
Nkhawa ikadzawafikira adzafunafuna mtendere koma osawupeza.
26 Ulykke på ulykke skal komme, og rykte på rykte skal opstå, og de skal søke efter syn hos profeten, og lov skal ikke være å finne hos presten eller råd hos de gamle;
Tsoka lidzatsatana ndi tsoka linzake, ndipo mphekesera idzatsatana ndi mphekesera inzake. Iwo adzayesa kufuna masomphenya kuchokera kwa mneneri. Adzasowa ansembe owaphunzitsa malamulo, ndipo anthu akuluakulu sadzakhalanso ndi uphungu.
27 kongen skal sørge, og høvdingen skal klæ sig i forferdelse, og hendene på landets folk skal skjelve. Efter deres ferd vil jeg gjøre med dem, og med deres dommer vil jeg dømme dem, og de skal kjenne at jeg er Herren.
Mfumu idzalira, kalonga adzagwidwa ndi mantha. Manja a anthu a mʼdzikomo azidzangonjenjemera ndi mantha. Ine ndidzawalanga molingana ndi machitidwe awo, ndipo ndidzawaweruza molingana ndi momwe anaweruzira anzawo.