< Esekiel 5 >

1 Og du menneskesønn, ta dig et skarpt sverd! Bruk det som en rakekniv og la det gå over ditt hode og skjegg, og ta dig så en skålvekt og del både hår og skjegg.
Tsiku lina Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga lupanga lakuthwa ndipo uligwiritse ntchito ngati lumo lometera. Umete tsitsi ndi ndevu zako. Kenaka utenge sikelo ndipo ugawe tsitsilo patatu.
2 En tredjedel skal du brenne op midt i byen, når kringsetningsdagene er til ende, og en tredjedel skal du ta og hugge i med sverdet rundt omkring byen, og en tredjedel skal du sprede for vinden, og med draget sverd vil jeg forfølge dem.
Kuzinga mzinda kuja kukatha, chimodzi cha zigawo zitatu za tsitsilo uchitenthe pakati pa mzinda. Chigawo chachiwiri uchiduledule ndi lupanga, poyenda muzungulire mzinda wonsewo. Chigawo chachitatu uchimwazire ku mphepo, ndidzachitsata nditasolola lupanga.
3 Men nogen få hår skal du ta unda, og dem skal du knytte inn i dine kjortelfliker,
Koma utengeko tsitsi pangʼono, ulimange mu mpindiro wa mkanjo wako.
4 og av dem skal du igjen ta nogen og kaste dem midt i ilden og brenne dem op; derfra skal det gå ut ild til alt Israels hus.
Pa tsitsi limeneli utapepo lina, uliponye pa moto ndi kulitentha. Moto udzayambira pamenepo mpaka ku nyumba yonse ya Israeli.”
5 Så sier Herren, Israels Gud: Dette Jerusalem satte jeg midt iblandt hedningefolkene og la land rundt omkring det;
Ambuye Yehova akunena kuti, “Uyu ndi Yerusalemu amene ndamuyika pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mayiko onse amuzungulira.
6 men det var gjenstridig mot mine lover, så det var mere ugudelig enn hedningefolkene, og mot mine bud, så det var mere ugudelig enn landene rundt omkring det; for de forkastet mine lover og fulgte ikke mine bud.
Koma anthu a Yerusalemu aphwanya malamulo anga pochita zoyipa kuposa anthu a mitundu ina. Iwo anandipandukira kupambana anthu ena amene awazungulira. Iwo anakana malamulo anga ndipo sanasunge malangizo anga.
7 Derfor sier Herren, Israels Gud, så: Fordi I har rast verre enn folkene som bor rundt omkring eder, fordi I ikke har fulgt mine bud og ikke gjort efter mine lover og ikke engang gjort efter de folks lover som bor rundt omkring eder,
“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Popeza mwakhala osamvera kupambana anthu a mitundu ina amene akuzungulirani, popeza simunatsate malamulo anga kapena kusunga malangizo anga, mʼmalo mwake mwakhala mukutsata makhalidwe a anthu a mitundu ina amene akuzungulirani.
8 derfor sier Herren, Israels Gud, så: Se, jeg kommer over dig, jeg og, og jeg vil holde dom hos dig for folkenes øine,
“Tsono Ambuye Yehova akuti: Ine mwini ndikutsutsana nawe, Yerusalemu, choncho Ine ndidzakulangani. Ine ndidzakulangani anthu a mitundu ina akuona.
9 og jeg vil gjøre med dig hvad jeg ikke før har gjort og aldri mere vil gjøre maken til - for alle dine vederstyggeligheters skyld.
Chifukwa cha ntchito zanu zonyansa ndidzakulangani ndi chilango chimene sindinakulangeni nacho nʼkale lomwe ndipo sindidzakulangani ndi chofanana nacho mʼtsogolomo.
10 Derfor skal foreldre ete sine barn hos dig, og barn ete sine foreldre, og jeg vil holde dom hos dig og sprede alt som blir igjen av dig, for alle vinder.
Tsono pakati panu makolo adzadya ana awo, ndipo ana adzadya makolo awo. Ndidzakulanga ndipo otsala onse ndidzawabalalitsa ku mphepo zonse zinayi.
11 Derfor, så sant jeg lever, sier Herren, Israels Gud, sannelig, fordi du har gjort min helligdom uren med alle dine avskyeligheter og alle dine vederstyggeligheter, så vil også jeg vende mitt øie bort fra dig uten skånsel og ikke spare dig.
Ndithu, pali Ine, akutero Ambuye Yehova Wamoyo, pakuti mwayipitsa Nyumba yanga ndi mafano ano oyipa ndi miyambo yanu yonyansa, Inenso ndidzakulangani. Sindidzakulekererani kapena kukumverani chisoni.
12 Tredjedelen av dig skal dø av pest og fortæres av hunger midt i dig, og tredjedelen skal falle for sverd rundt omkring dig, og tredjedelen vil jeg sprede for alle vinder og forfølge med draget sverd.
Chimodzi mwa zigawo zitatu za anthu ako chidzafa ndi mliri, kapena chidzawonongeka ndi njala; chigawo china chidzaphedwa ndi lupanga kunja kwa mzinda, ndipo chigawo china ndidzachibalalitsira ku mphepo zonse zinayi pochita kuchithamangitsa.
13 Og min vrede skal uttømmes, og jeg vil stille min harme på dem og ta hevn, og de skal kjenne at jeg, Herren, har talt i min nidkjærhet, når jeg uttømmer min harme på dem.
“Ndi mmene udzachitire mkwiyo wanga. Ndikadzatsiriza kuwalanga, pamenepo mtima wanga udzakhala pansi. Adzadziwa kuti Ine Yehova ndinawayankhula mwa nsanje ndikadzawalanga.
14 Og jeg vil gjøre dig til en ørken og til en spott blandt folkene som bor rundt omkring dig, for øinene på hver den som går forbi.
“Ndidzakusandutsa iwe bwinja ndi chinthu chonyozeka pakati pa anthu a mitundu ina amene akuzungulira, ndi kwa onse odutsapo
15 Du skal bli til spott og hån, til en advarsel og en forferdelse for folkene som bor rundt omkring dig, når jeg holder dom over dig med vrede og harme og med harmfulle tuktelser - jeg, Herren, har talt -
Udzakhala chinthu chonyozeka ndi chonyogodoledwa. Udzakhala chenjezo ndi chinthu choopsa kwa anthu a mitundu ina amene akuzungulira ndikadzakulanga mokwiya ndi mwaukali ndi kugamula mlandu wako mokwiya. Ine Yehova ndayankhula.
16 når jeg sender inn blandt dem hungerens onde piler, som er til ødeleggelse, dem som jeg sender for å ødelegge eder, når jeg hoper op hunger over eder og sønderbryter brødets stav for eder.
Pamene ndidzakulasa ndi njala yolasa ngati mivi yoopsa ndi yosakaza ndidzatero nʼcholinga choti ndikuwonongeni. Ndidzagwetsa njalayo pa iwe mowirikiza pochepetsa chakudya chako cha tsiku ndi tsiku.
17 Jeg vil sende hunger over eder og ville dyr, og de skal gjøre dig barnløs, og pest og blod skal gå over dig, og sverd vil jeg la komme over dig; jeg, Herren, har talt.
Ndidzatumiza njala ndi zirombo za kuthengo, ndipo zidzakulanda ana ako. Mliri ndi kuphana zidzakhala pakati pako, ndipo ndidzakubweretsera nkhondo. Ine Yehova ndayankhula.”

< Esekiel 5 >