< Esekiel 37 >

1 Herrens hånd kom over mig, og Herren førte mig i ånden ut og satte mig ned midt i dalen, og den var full av ben.
Dzanja la Yehova linali pa ine, ndipo Mzimu wa Yehova unandinyamula nʼkukandikhazika pakati pa chigwa. Chigwacho chinali chodzaza ndi mafupa.
2 Og han førte mig rundt omkring dem, og jeg så at de lå der i store mengder utover dalen, og de var aldeles tørre.
Yehova anandiyendetsa uku ndi uku pakati pa mafupawo. Mafupawo anali ochuluka kwambiri mʼchigwa monsemo ndipo anali owuma kwambiri.
3 Og han sa til mig: Menneskesønn! Skal disse ben bli levende? Jeg svarte: Herre, Israels Gud, du vet det!
Tsono Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi mafupa amenewa angakhalenso ndi moyo?” Ndinayankha kuti, “Inu Ambuye Yehova, Inuyo nokha ndiye mukudziwa.”
4 Da sa han til mig: Spå om disse ben og si til dem: I tørre ben, hør Herrens ord!
Pamenepo anandiwuza kuti, “Lengeza kwa mafupa amenewa ndi kuwawuza kuti amve mawu a Ine Yehova!
5 Så sier Herren, Israels Gud, til disse ben: Se, jeg lar det komme livsånde i eder, og I skal bli levende.
Uwawuze kuti zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena kwa mafupa ndi izi: Ndidzawuzira mpweya mwa inu, ndipo mudzakhalanso ndi moyo.
6 Jeg vil legge sener på eder og la det komme kjøtt på eder og dekke eder med hud og gi livsånde i eder, og I skal bli levende; og I skal kjenne at jeg er Herren.
Ndidzakupatsani mitsempha ndi mnofu. Ndiponso ndidzakukutani ndi khungu. Pambuyo pake ndidzawuzira mpweya mwa inu ndipo mudzakhalanso ndi moyo. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
7 Og jeg spådde således som det var befalt mig, og mens jeg spådde, hørtes det en sterk lyd; det blev et bulder, og benene nærmet sig til hverandre.
Ndipo ndinanenera monga anandilamulira. Ndipo pamene ndinkanenera, ndinamva gobedegobede, ndipo mafupa aja anayamba kulumikizana, fupa ku fupa linzake.
8 Og jeg så, og se, det kom sener og kjøtt på dem, og ovenpå det drog det sig hud over dem; men livsånde var det ikke i dem.
Ine ndinayangʼana, ndipo mitsempha ndi mnofu zinabwera pa mafupawo ndipo khungu linaphimba pamwamba pake, koma munalibe mpweya mwa iwo.
9 Da sa han til mig: Spå og tal til livsånden! Spå, menneskesønn, og si til livsånden: Så sier Herren, Israels Gud: Kom du livsånde fra de fire vinder og blås på disse drepte menn, så de kan bli levende!
Tsono Yehova anandiwuza kuti, “Nenera kwa mpweya, nenera iwe mwana wa munthu ndi kuwuza mpweya mawu a Ine Ambuye Yehova kuti, ‘Bwera kuno iwe mpweya. Bwera kuchokera ku mbali zonse zinayi ndi kudzawuzira anthu ophedwawa kuti akhalenso ndi moyo.’
10 Og jeg spådde således som han hadde befalt mig, og livsånden kom i dem, og de blev levende og stod op på sine føtter, en meget, meget stor hær.
Choncho ndinanenera monga anandilamulira ndipo mpweya unalowa mwa iwo; apo anthu akufawo anakhala ndi moyo, nayimirira ndipo linali gulu lalikulu lankhondo.”
11 Og han sa til mig: Menneskesønn! Disse ben er hele Israels hus. Se, de sier: Våre ben er fortørket, og vårt håp er gått til grunne; vi er fortapt.
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, mafupa awa ndi nyumba yonse ya Israeli. Iwo amanena kuti, ‘Mafupa athu awuma ndipo chiyembekezo chathu chatayika, ife tawonongeka!’
12 Spå derfor og si til dem: Så sier Herren, Israels Gud: Se, jeg åpner eders graver og lar eder, mitt folk, stige op av eders graver, og jeg fører eder til Israels land.
Nʼchifukwa chake nenera ndi kuwawuza kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Inu anthu anga, ndidzafukula manda anu, ndipo ndidzakutulutsanimo ndi kukubwezerani ku dziko la Israeli.
13 Og I skal kjenne at jeg er Herren, når jeg åpner eders graver og lar eder, mitt folk, stige op av eders graver.
Ndipo inu, anthu anga, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene ndidzafukula manda anu ndikukutulutsanimo.
14 Og jeg vil gi min Ånd i eder, og I skal bli levende, og jeg vil bosette eder i eders land, og I skal kjenne at jeg, Herren, har sagt det, og at jeg også vil gjøre det, sier Herren.
Ine ndidzayika Mzimu wanga mwa inu ndipo mudzakhalanso ndi moyo. Pambuyo pake ndidzakulowetsani mʼdziko lanulanu. Choncho mudzadziwa kuti Ambuye Yehova ndayankhula zimenezi, ndipo ndidzazichitadi. Ndikutero Ine Yehova!’”
15 Og Herrens ord kom til mig, og det lød så:
Yehova anandiyankhula kuti:
16 Og du menneskesønn! Ta dig en stav og skriv på den: For Juda og for Israels barn, hans medbrødre! Og ta dig en annen stav og skriv på den: For Josef - en stav for Efra'im og hele Israels hus, hans medbrødre!
“Iwe mwana wa munthu, tenga ndodo ndipo ulembepo kuti, ‘Ndodo ya Yuda ndi Aisraeli oyanjana nawo.’ Utengenso ndodo ina ndipo ulembepo kuti, ‘Ndodo ya Efereimu, ndiye kuti fuko la Yosefe ndi Aisraeli onse oyanjana nawo.’
17 Og sett dem sammen, den ene til den andre, til én stav, så de blir til ett i din hånd!
Ulumikize ndodo ziwirizi kuti zikhale ndodo imodzi mʼdzanja lako.
18 Og når ditt folks barn sier til dig: Vil du ikke la oss få vite hvad du mener med dette? -
“Anthu a mtundu wako akadzakufunsa tanthauzo la zimenezi
19 da skal du si til dem: Så sier Herren, Israels Gud: Se, jeg tar Josefs stav, som er i Efra'ims hånd, og Israels stammer, hans medbrødre, og jeg legger dem til Judas stav og gjør dem til én stav, så de blir til ett i min hånd.
iwe udzawawuze mawu awa a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndidzatenga ndodo ya Yosefe imene ili mʼdzanja la Efereimu, ndi ya mafuko a Aisraeli oyanjana naye, ndi kuyilumikiza ku ndodo ya Yuda, kuti zikhale ndodo imodzi, ndipo zidzakhaladi ndodo imodzi mʼdzanja langa!’
20 Og de staver som du skriver på, skal du holde i din hånd for deres øine.
Ndodo ziwiri zimene udzalembepozo zikadzakhala mʼmanja mwako pamaso pa anthu onse,
21 Si så til dem: Så sier Herren, Israels Gud: Se, jeg henter Israels barn fra de folk som de drog bort til, og jeg vil samle dem fra alle kanter og føre dem til deres eget land.
udzawawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzawachotsa Aisraeli pakati pa anthu a mitundu ina kumene anapita ku ukapolo. Ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mbali zonse ndi kubwera nawo ku dziko lawolawo.
22 Og jeg vil gjøre dem til ett folk i landet, på Israels fjell, og én konge skal være konge for dem alle, og de skal ikke mere være to folk og ikke mere dele sig i to riker.
Ndidzawasandutsa mtundu umodzi mʼdzikomo, pa mapiri a Israeli. Padzakhala mfumu imodzi yowalamulira, ndipo sadzakhalanso mitundu iwiri kapena kugawikana maufumu awiri.
23 Og de skal ikke mere gjøre sig urene med sine motbydelige avguder og med sine vederstyggeligheter eller med nogen av sine misgjerninger, og jeg vil utfri dem fra alle deres bosteder, hvor de har syndet, og rense dem, og de skal være mitt folk, og jeg vil være deres Gud.
Sadzadziyipitsanso ndi mafano awo, kapena ndi zinthu zawo zonyansa, kapenanso ndi ntchito zawo zoyipa zilizonse. Ndidzawapulumutsa ku machimo awo onse ndi kuwayeretsa. Choncho adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo.
24 Og min tjener David skal være konge over dem, og én hyrde skal det være for dem alle, og mine lover skal de følge, og mine bud skal de holde og gjøre efter dem.
“‘Mtumiki wanga Davide adzakhala mfumu yawo, motero onsewa adzakhala ndi mʼbusa mmodzi. Iwo adzatsatira malamulo anga ndipo adzasamalira kusunga malangizo anga.
25 Og de skal bo i det land jeg gav min tjener Jakob, det som eders fedre bodde i; de skal bo i det, de og deres barn og deres barnebarn, til evig tid, og David, min tjener, skal være deres fyrste evindelig.
Iwo adzakhala mʼdziko limene ndinalipereka kwa mtumiki wanga Yakobo, dziko limene makolo anu ankakhalamo. Iwo ndi ana awo pamodzi ndi zidzukulu zawo adzakhala kumeneko ndipo Davide adzakhala mfumu yawo kwa muyaya.
26 Og jeg vil gjøre en fredspakt med dem - en evig pakt med dem skal det være; og jeg vil bosette dem i mitt land og la dem bli tallrike, og jeg vil sette min helligdom midt iblandt dem for evig tid.
Ndidzachita nawo pangano lamtendere; lidzakhala pangano lamuyaya. Ndidzawakhazikitsa ndi kuwachulukitsa, ndipo ndidzayika malo anga opatulika pakati pawo kwamuyaya.
27 Og min bolig skal være over dem, og jeg vil være deres Gud, og de skal være mitt folk.
Nyumba yanga yokhalamo idzakhala pakati pawo; Ine ndidzakhala Mulungu wawo, ndipo iwo adzakhala anthu anga.
28 Og folkene skal kjenne at jeg er Herren, som helliger Israel, når min helligdom blir midt iblandt dem til evig tid.
Pamenepo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti Ine Yehova ndiye amene ndimasandutsa Israeli kukhala woyera, pamene malo anga opatulika adzakhala pakati pawo kwamuyaya!’”

< Esekiel 37 >