< Esekiel 18 >

1 Og Herrens ord kom til mig, og det lød så:
Yehova anandiyankhula nati:
2 Hvorledes kan I bruke dette ordsprog i Israels land: Fedrene eter sure druer, og barnas tenner blir såre?
“Kodi anthu inu mumatanthauza chiyani mukamabwerezabwereza kunena mwambi uwu wokhudza dziko la Israeli kuti: “‘Nkhuyu zodya akulu zimapota ndi ana omwe?’”
3 Så sant jeg lever, sier Herren, Israels Gud, I skal ikke mere bruke dette ordsprog i Israel.
“Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, simudzanenanso mwambi umenewu mu Israeli.
4 Se, alle sjeler hører mig til, både farens sjel og sønnens sjel; mig hører de til; den som synder, han skal dø.
Pakuti moyo uliwonse ndi wanga. Moyo wa abambo ndi wanga, wamwananso ndi wanga. Munthu wochimwa ndi amene adzafe.
5 Og når en mann er rettferdig og gjør rett og rettferdighet,
“Tiyerekeze kuti pali munthu wolungama amene amachita zolungama ndi zolondola.
6 ikke eter avgudsoffer på fjellene og ikke løfter sine øine til Israels folks motbydelige avguder og ikke krenker sin næstes hustru og ikke nærmer sig en kvinne når hun er uren,
Iye sadyera nawo pa mapiri a chipembedzo kapena kupembedza mafano a Aisraeli. Iye sayipitsa mkazi wa mnzake kapena kugonana ndi mkazi pamene akusamba.
7 og ikke undertrykker nogen, men lar skyldneren få sitt pant igjen, ikke raner og røver, men gir den hungrige sitt brød og dekker den nakne med klær,
Iye sapondereza munthu wina aliyense, koma amabwezera wangongole nʼchigwiriro chake. Iye salanda zinthu za osauka, koma amapereka chakudya kwa anthu anjala, ndipo amapereka zovala kwa anthu ausiwa.
8 ikke låner ut mot rente og ikke tar overmål, holder sin hånd tilbake fra urett, dømmer rett dom mann og mann imellem,
Iye sakongoletsa ndalama mwa katapira, kapena kulandira chiwongoladzanja chachikulu. Amadziletsa kuchita zoyipa ndipo sakondera poweruza milandu.
9 følger mine bud og holder mine lover, så han gjør det som rett og godt er - han er rettferdig, han skal visselig leve, sier Herren, Israels Gud.
Iye amatsatira malangizo anga, ndipo amasunga malamulo anga mokhulupirika. Munthu ameneyo ndi wolungama; iye adzakhala ndithu ndi moyo, akutero Ambuye Yehova.
10 Men får han en sønn som blir en voldsmann, som utøser blod og gjør noget som helst av dette,
“Tiyerekeze kuti munthu wolungama chotere wabala mwana chimbalangondo amene amakhalira kupha anthu ndi kuchita zinthu zina zotere.
11 som ikke i noget av dette bærer sig at som faren har gjort, men endog eter avgudsoffer på fjellene og krenker sin næstes hustru,
Iye nʼkumachita zinthu zimene ngakhale abambo ake sanachitepo. “Amadyera nawo ku mapiri achipembedzo. Amayipitsa mkazi wa mnzake.
12 undertrykker den elendige og fattige, raner og røver, ikke gir pantet tilbake, løfter sine øine til de motbydelige avguder, gjør det som vederstyggelig er,
Iye amapondereza munthu wosauka ndi wosowa. Amalanda zinthu za osauka. Sabweza chikole cha munthu wa ngongole. Iye amatembenukira ku mafano nachita zonyansa.
13 låner ut mot rente og tar overmål, skulde så han få leve? Nei, han skal ikke få leve! Alle disse vederstyggeligheter har han gjort; han skal visselig late livet, hans blod skal komme over ham.
Iye amakongoletsa mwa katapira ndipo amalandira chiwongoladzanja chachikulu. Kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu! Chifukwa wachita zinthu zonyansa zonsezi, adzaphedwa ndipo adzalandira chilango chomuyenera.
14 Men får så han igjen en sønn som ser alle de synder som hans far gjør - ser dem og ikke gjør efter dem,
“Tsono tiyerekeze kuti munthu woyipa uyu wabala mwana amene amaona machimo onse amene abambo ake ankachita. Ngakhale amaona koma osatsanzira ntchito zake zoyipazo.
15 som ikke eter avgudsoffer på fjellene og ikke løfter sine øine til Israels folks avguder, ikke krenker sin næstes hustru,
“Sadyera nawo pa mapiri achipembedzo. Sapembedza mafano a ku Israeli. Sayipitsa mkazi wa mnzake.
16 ikke undertrykker nogen, ikke tar pant, ikke raner og røver, men gir den hungrige sitt brød og dekker den nakne med klær,
Sapondereza munthu wina aliyense. Satenga chikole akabwereketsa chinthu. Salanda zinthu za osauka. Salanda zinthu za munthu. Amapereka chakudya kwa anthu anjala. Amapereka zovala kwa anthu aumphawi.
17 ikke forgriper sig på den elendige, ikke tar rente eller overmål, men gjør efter mine lover og følger mine bud, så skal han ikke dø for sin fars misgjernings skyld, han skal visselig få leve.
Amadziletsa kuchita zoyipa. Sakongoletsa kuti apezepo phindu. Salandira chiwongoladzanja. Amasunga malangizo anga ndi kumvera malamulo anga. Munthu wotereyo sadzafa chifukwa cha machimo a abambo ake. Adzakhala ndi moyo ndithu.
18 Men hans far, som har gjort voldsgjerninger, ranet og røvet fra sin bror og gjort det som ikke er godt, iblandt sitt folk, se, han skal dø for sin misgjernings skyld.
Koma abambo ake, popeza kuti anazunza anthu ena ndi kubera mʼbale wawo ndiponso popeza kuti sanachitire zabwino anansi ake, adzafera machimo ake omwe.
19 Men I sier: Hvorfor skal ikke sønnen bære farens misgjerning? - Sønnen har jo gjort rett og rettferdighet, alle mine bud har han holdt og gjort efter dem; han skal visselig leve.
“Mwina inu mukhoza kufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mwana salangidwa chifukwa cha kulakwa kwa abambo ake? Ayi, mwanayo adzakhala ndi moyo chifukwa ankachita zolungama ndi zolondola ndipo ankasamala kumvera malamulo anga onse.
20 Den som synder, han skal dø; en sønn skal ikke bære sin fars misgjerning, og en far skal ikke bære sin sønns misgjerning; den rettferdiges rettferdighet skal hvile over ham, og den ugudeliges ugudelighet skal hvile over ham.
Munthu wochimwa ndiye amene adzafe. Mwana sadzapezeka wolakwa chifukwa cha abambo ake, kapena abambo kupezeka wolakwa chifukwa cha mwana wawo. Chilungamo cha munthu wolungama ndicho chidzamupulutse, ndipo kuyipa kwa munthu wochimwa ndiko kudzamuwonongetse.
21 Men når den ugudelige vender om fra alle de synder han har gjort, og holder alle mine bud og gjør rett og rettferdighet, da skal han visselig leve - han skal ikke dø.
“‘Munthu woyipa akatembenuka mtima ndi kusiya machimo amene ankachita ndi kuyamba kumvera malamulo anga ndi kumachita zolungama ndi zokhulupirika, ndiye kuti adzakhala ndi moyo. Sadzafa ayi.
22 Ingen av de overtredelser han har gjort, skal tilregnes ham; for den rettferdighets skyld som han har gjort, skal han leve.
Zoyipa zake zonse zidzakhululukidwa. Chifukwa cha zinthu zolungama zimene anazichita adzakhala ndi moyo.
23 Skulde jeg ha behag i den ugudeliges død? sier Herren, Israels Gud - mon ikke heller i at han vender om fra sin vei og lever?
Kodi Ine ndimakondwera ndi imfa ya munthu woyipa? Ayi, ndimakondwera pamene woyipa watembenuka mtima kuti akhale ndi moyo. Akutero Ambuye Yehova.
24 Men når en rettferdig vender om fra sin rettferdighet og gjør urett, gjør efter alle de vederstyggeligheter som den ugudelige gjør, skulde han da få leve? Ingen av de rettferdige gjerninger som han har gjort, skal tilregnes ham; for den troløshet han har vist, og for den synd han har gjort, skal han dø.
“‘Koma ngati munthu wolungama apatuka kusiya zachilungamo ndi kuyamba kuchita tchimo ndi zonyansa za mtundu uliwonse zimene amachita anthu oyipa, kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu, zolungama zake zonse sizidzakumbukiridwa. Iye adzayenera kufa chifukwa cha machimo amene anachita.
25 Og I sier: Herrens vei er ikke rett. Hør, du Israels hus! Er ikke min vei rett? Er det ikke eders veier som ikke er rette?
“Komabe inu mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Tamvani tsono inu Aisraeli: Kodi zochita zanga ndizo zosalungama? Kodi si zochita zanu zimene ndi zosalungama?
26 Når en rettferdig vender om fra sin rettferdighet og gjør urett, så skal han dø til straff for det; for den urett som han gjør, skal han dø.
Ngati munthu wolungama atembenuka kusiya chilungamo chake ndi kuchita tchimo, iye adzafa chifukwa cha tchimolo.
27 Og når en ugudelig vender om fra sin ugudelige ferd og gjør rett og rettferdighet, da skal han berge sitt liv.
Koma ngati munthu woyipa aleka zoyipa zake zimene anazichita ndi kuyamba kuchita zimene ndi zolungama ndi zolondola, iye adzapulumutsa moyo wake.
28 Han så og vendte om fra alle de overtredelser han hadde gjort; han skal visselig leve - han skal ikke dø.
Popeza waganizira za zolakwa zonse ankachita ndipo wazileka, iye adzakhala ndi moyo ndithu; sadzafa.
29 Men Israels hus sier: Herrens vei er ikke rett. Er ikke mine veier rette, Israels hus? Er det ikke eders veier som ikke er rette?
Komabe Aisraeli akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Kodi zochita zanga ndizo zopanda chilungamo, inu Aisraeli? Kodi si zochita zanu zimene ndi zopanda chilungamo?
30 Derfor vil jeg dømme eder, Israels hus, hver efter hans veier, sier Herren, Israels Gud. Vend om og vend eder bort fra alle eders overtredelser, forat ikke nogen misgjerning skal bli eder til fall!
“Chifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: inu Aisraeli, Ine ndidzakuweruzani aliyense wa inu molingana ndi ntchito zake. Lapani! Lekani zoyipa zanu kuti musawonongeke nazo.
31 Kast fra eder alle eders overtredelser, som I har forsyndet eder med, og få eder et nytt hjerte og en ny ånd! Hvorfor vil I dø, Israels hus?
Tayani zolakwa zanu zonse zimene munandichimwira nazo ndipo khalani ndi mtima watsopano ndi mzimu watsopano. Kodi muferanji inu Aisraeli?
32 For jeg har ikke behag i nogens død, sier Herren, Israels Gud; så omvend eder da, og I skal leve!
Ine sindikondwera ndi imfa ya munthu aliyense, akutero Ambuye Yehova. Chifukwa chake, lapani kuti mukhale ndi moyo.”

< Esekiel 18 >