< Predikerens 9 >
1 For alt dette har jeg tatt mig til hjerte, og jeg har søkt å utgrunde alt dette: at de rettferdige og de vise og deres gjerninger er i Guds hånd; om det er kjærlighet eller hat, vet intet menneske; de kan vente sig alt.
Ndinalingalira zonse ndanenazi ndipo ndinapeza kuti anthu olungama ndi anthu anzeru ali mʼmanja mwa Mulungu pamodzi ndi zimene amachita, koma palibe amene amadziwa zimene zikumudikira mʼtsogolo mwake, kaya chikondi kapena chidani.
2 Det går dem i alt likesom alle andre; det samme hender den rettferdige og den ugudelige, den gode og rene og den urene, den som ofrer og den som ikke ofrer; den gode går det som synderen, den som sverger, går det som den som er redd for å sverge.
Onsewa mathero awo ndi amodzi, anthu olungama ndi anthu oyipa, abwino ndi oyipa, oyera ndi odetsedwa, amene amapereka nsembe ndi amene sapereka nsembe. Zomwe zimachitikira munthu wabwino, zimachitikiranso munthu wochimwa, zomwe zimachitikira amene amalumbira, zimachitikiranso amene amaopa kulumbira.
3 Det er en ond ting ved alt det som hender under solen, at det går alle likedan, og så er også menneskenes hjerte fullt av det som ondt er, og det er uforstand i deres hjerte, så lenge de lever, og siden går det avsted til de døde;
Choyipa chimene chili mʼzonse zochitika pansi ndi ichi: Mathero a zonse ndi amodzi. Ndithu, mitima ya anthu ndi yodzaza ndi zoyipa, ndipo mʼmitima mwawo muli zamisala pamene ali ndi moyo, potsiriza pake iwo amakakhala pamodzi ndi anthu akufa.
4 for hvem er det vel som slipper? For alle dem som lever, er det håp; for en levende hund er bedre enn en død løve;
Aliyense amene ali ndi moyo amakhala ndi chiyembekezo, pajatu galu wamoyo aposa mkango wakufa!
5 for de levende vet at de skal dø, men de døde vet ikke nogen ting, og de får ikke lenger nogen lønn, for minnet om dem er glemt.
Pakuti amoyo amadziwa kuti adzafa, koma akufa sadziwa kanthu; alibe mphotho ina yowonjezera, ndipo palibe amene amawakumbukira.
6 Både deres kjærlighet og deres hat og deres ærgjerrighet er det for lenge siden forbi med, og de har i all evighet ingen del mere i alt det som hender under solen.
Chikondi chawo, chidani chawo ndiponso nsanje yawo, zonse zinatha kalekale; sadzakhalanso ndi gawo pa zonse zochitika pansi pano.
7 Så et da ditt brød med glede og drikk vel til mote din vin! For Gud har for lenge siden godkjent det du gjør.
Pita, kadye chakudya chako mokondwera ndi kumwa vinyo wako ndi mtima wosangalala, pakuti tsopano Mulungu akukondwera ndi zochita zako.
8 La dine klær alltid være hvite, og la ikke olje fattes på ditt hode!
Uzivala zovala zoyera nthawi zonse, uzidzola mafuta mʼmutu mwako nthawi zonse.
9 Nyt livet med en hustru som du elsker, alle dager i ditt tomme liv, som Herren har gitt dig under solen, alle dine tomme dager! For det er din del i livet og i ditt strev som du møier dig med under solen.
Uzikondwerera moyo pamodzi ndi mkazi wako amene umamukonda, masiku onse a moyo uno wopanda phindu, amene Mulungu wakupatsa pansi pano. Pakuti mkaziyo ndiye gawo la moyo wako pa ntchito yako yolemetsa pansi pano.
10 Alt det din hånd er i stand til å gjøre med din kraft, det skal du gjøre! For det finnes hverken gjerning eller klokskap eller kunnskap eller visdom i dødsriket, dit du går. (Sheol )
Ntchito iliyonse imene ukuyigwira, uyigwire ndi mphamvu zako zonse, pakuti ku manda kumene ukupita kulibe kugwira ntchito, kulibe malingaliro, chidziwitso ndiponso nzeru. (Sheol )
11 Fremdeles så jeg under solen at det ikke er visst at de som er lette på foten, vinner i løpet, eller at heltene seirer i krigen, eller at de vise kan få sig brød, eller at de forstandige kan vinne rikdom eller de kloke finne yndest; for tid og hendelse møter dem alle.
Ine ndinaonanso chinthu china pansi pano: opambana pa kuthamanga si aliwiro, kapena opambana pa nkhondo si amphamvu, ndiponso okhala ndi chakudya si anzeru, kapena okhala ndi chuma si odziwa zambiri, kapena okomeredwa mtima si ophunzira; koma mwayi umangowagwera onsewa pa nthawi yake.
12 For mennesket kjenner like så lite sin tid som fiskene som fanges i det onde garn, eller fuglene som blir fanget i snaren; likesom de fanges også menneskenes barn i en ond tid, når den med ett kommer over dem.
Kungoti palibe munthu amene amadziwa kuti nthawi yake idzafika liti: monga momwe nsomba zimagwidwira mu ukonde, kapena mmene mbalame zimakodwera mu msampha, chimodzimodzinso anthu amakodwa mu msampha pa nthawi yoyipa, pamene tsoka limawagwera mosayembekezera.
13 Også i dette så jeg visdom under solen, og stor syntes den mig:
Ine ndinaonanso pansi pano chitsanzo ichi cha nzeru chimene chinandikhudza kwambiri:
14 Det var en liten by med få folk i; til den kom det en stor konge og kringsatte den og bygget store voller mot den;
Panali mzinda waungʼono umene unali ndi anthu owerengeka. Ndipo mfumu yamphamvu inabwera kudzawuthira nkhondo, inawuzungulira ndi kumanga mitumbira yankhondo.
15 men det fantes i byen en fattig, vis mann, og han berget den ved sin visdom, og ikke et menneske var kommet denne fattige mann i hu.
Tsono mu mzindamo munali munthu wosauka koma wanzeru, ndipo anapulumutsa mzindawo ndi nzeru zakezo. Koma palibe amene anakumbukira munthu wosaukayo.
16 Da sa jeg: Visdom er bedre enn styrke; men den fattiges visdom er foraktet, og folk hører ikke på det han sier.
Choncho ine ndinati, “Nzeru ndi yopambana mphamvu.” Koma nzeru ya munthu wosauka imanyozedwa, ndipo palibe amene amalabadirako za mawu ake.
17 De vises ord som høres i ro, er bedre enn rop fra en hersker blandt dårene.
Mawu oyankhula mofatsa a munthu wanzeru, anthu amawasamalira kwambiri kupambana kufuwula kwa mfumu ya zitsiru.
18 Visdom er bedre enn krigsvåben, men en synder kan ødelegge meget godt.
Nzeru ndi yabwino kupambana zida zankhondo, koma wochimwa mmodzi amawononga zinthu zambiri zabwino.