< 5 Mosebok 12 >

1 Dette er de bud og de lover I skal akte på å leve efter i det land som Herren, dine fedres Gud, har gitt dig til eie, alle de dager I lever på jorden:
Awa ndi malangizo ndi malamulo amene muyenera kusamalitsanso kuti muwatsatire mʼdziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu wakupatsani kuti mutenge pa nthawi yonse imene muti mudzakhale mʼdzikomo.
2 I skal ødelegge alle de steder hvor hedningene som I skal drive bort, har dyrket sine guder, på de høie fjell og på haugene og under hvert grønt tre;
Muwonongeretu kwathunthu malo onse a pamwamba pa mapiri ataliatali ndi pa mapiri angʼonoangʼono ndi pansi pa mtengo uliwonse wotambalala pamene mitundu imene muyilande dzikolo ankapembedzerapo milungu yawo.
3 I skal rive ned deres altere og slå deres billedstøtter sønder, og deres Astarte-billeder skal I brenne op med ild, og de utskårne billeder av deres guder skal I hugge i stykker og utslette deres navn fra det sted hvor de stod.
Mugumule maguwa awo ansembe, ndi kuphwanya miyala yawo yachipembedzo ndipo mutenthe pa moto mafano awo a Asera: mugwetse mafano a milungu yawo ndi kufafaniza mayina awo mʼmalo amenewo.
4 I skal ikke gjøre som de når I dyrker Herren eders Gud,
Musapembedze Yehova Mulungu wanu monga mmene amachitira iwowa.
5 men til det sted Herren eders Gud utvelger av alle eders stammer for å la sitt navn bo der, dit skal I søke, og dit skal du komme.
Koma inu muzifunafuna kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe pakati pa mafuko anu kuti ayikeko dzina lake ndi kukhalako. Ku malo amenewa muyenera kupitako.
6 Og dit skal I føre eders brennoffer og eders slaktoffer og eders tiender og eders henders gaver og eders lovede offer og eders frivillige offer og det førstefødte av eders storfe og av eders småfe,
Kumeneko muzipititsako zopereka zanu ndi nsembe zanu zopsereza, ndi chakhumi chanu ndi mphatso zapadera zimene munalonjeza kupereka ndi zopereka zanu zaufulu ndi ana oyamba a ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu.
7 og der skal I ete for Herrens, eders Guds åsyn og glede eder med eders husfolk over alt det I har vunnet ved eders arbeid, alt det Herren din Gud har velsignet dig med.
Kumeneko, pamaso pa Yehova Mulungu wanu, inu ndi mabanja anu mudzadya ndi kusangalalako pa china chilichonse chimene mudzakhudza, chifukwa Yehova Mulungu wanu wakudalitsani.
8 I skal ikke gjøre således som vi gjør her idag, enhver det som tykkes ham å være rett;
Musadzachite monga tikuchitira lero lino, aliyense kumachita zimene akuona kuti ndi zoyenera,
9 for I er ennu ikke kommet inn til den hvile og den arv Herren din Gud gir dig.
pakuti simunafike ku malo opumulirako ndi ku cholowa chimene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
10 Men når I er gått over Jordan og bor i det land Herren eders Gud gir eder til arv, og han har gitt eder ro for alle eders fiender rundt om, så I bor trygt,
Koma mudzawoloka Yorodani ndi kukhazikika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, ndipo Iye adzakupatsani inu mpumulo ku adani anu okuzungulirani kuti mukhale motchinjirizidwa.
11 da skal det sted som Herren eders Gud utvelger for å la sitt navn bo der, være det eneste sted hvorhen I skal føre alt det jeg byder eder: eders brennoffere og eders slaktoffere, eders tiender og eders henders gaver og alle eders utvalgte offer som I lover Herren.
Tsono kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe kuti azikhalako muzikabweretsako chilichonse chimene ndikulamulirani inu: zopereka ndi nsembe zanu zopsereza, chakhumi chanu ndi mphatso zapadera, ndi chuma chanu chonse chosankhika chimene munalonjeza kwa Yehova.
12 Og I skal være glade for Herrens, eders Guds åsyn, I og eders sønner og eders døtre og eders tjenere og eders tjenestepiker og levitten som bor hos eder; for han har ingen del eller arv med eder.
Ndipo kumeneko inu mukasangalale pamaso pa Yehova Mulungu wanu pamodzi ndi ana anu aamuna ndi ana anu aakazi, antchito anu aamuna ndi adzakazi anu, ndi Alevi a mʼmidzi yanu, amene alibe gawo kapena cholowa chawochawo.
13 Vogt dig at du ikke ofrer dine brennoffer på noget sted som du selv utser dig!
Musamalitse kuti musakaphere nsembe zanu zopsereza paliponse pamene mungafune.
14 Men på det sted som Herren utvelger i en av dine stammer, der skal du ofre dine brennoffer, og der skal du gjøre alt det jeg byder dig.
Mukaphere pa malo okhawo amene Yehova adzawasankhe mwa limodzi la mafuko anu, ndipo kumeneko mukasunge chilichonse chimene ndikulamulireni.
15 Men ellers kan du efter ditt hjertes lyst slakte og ete kjøtt rundt om i alle dine byer, efter som Herren din Gud gir dig sin velsignelse; den urene så vel som den rene kan ete av det som om det var et rådyr eller en hjort.
Koma mukhoza kumapha ziweto zanu mʼmizinda iliyonse ndi kudya nyama yake mmene mungafunire, ngati kuti ndi agwape kapena mbawala, monga mwadalitso limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani. Woyeretsedwa ndi wosayeretsedwa akhoza kuyidya.
16 Men blodet må I ikke ete; I skal helle det ut på jorden likesom vann.
Koma musamadye magazi. Muziwathira pansi ngati madzi.
17 Hjemme i dine byer må du ikke ete tienden av ditt korn eller av din most eller av din olje, heller ikke det førstefødte av ditt storfe eller av ditt småfe, heller ikke noget av dine lovede offer eller dine frivillige offer eller din hånds gaver.
Musamadyere mʼmizinda yanu chakhumi cha tirigu wanu ndi vinyo watsopano ndi mafuta, kapena za ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu, kapena chilichonse chimene mwalonjeza kuchipereka, nsembe zanu zaufulu, kapena mphatso zapadera,
18 Men for Herrens, din Guds åsyn skal du ete det på det sted Herren din Gud utvelger, du og din sønn og din datter og din tjener og din tjenestepike og levitten som bor hos dig; og du skal glede dig for Herrens, din Guds åsyn over alt det du har vunnet ved ditt arbeid.
mʼmalo mwake, muzidya pamaso pa Yehova Mulungu wanu, kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhira inu, ana anu aamuna ndi aakazi, antchito anu aamuna ndi adzakazi anu, ndi Alevi ochokera mʼmizinda yanu, ndipo mudzasangalale pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa chilichonse chimene mudzachikhudza.
19 Vokt dig at du ikke glemmer levitten, så lenge du lever i ditt land!
Muonetsetse kuti musawataye Alevi pa masiku onse amene mukhale mʼdziko lanumo.
20 Når Herren din Gud utvider dine landemerker, således som han har tilsagt dig, og du sier: Jeg vilde gjerne ete kjøtt, fordi du har lyst til å ete kjøtt, da kan du ete kjøtt efter ditt hjertes lyst.
Yehova Mulungu wanu akadzakulitsa dziko lanu monga anakulonjezerani, ndipo mukapukwa nyama mumanena kuti, “Ndikufuna nyama,” pamenepo mudzadya mmene mungafunire.
21 Hvis du har lang vei til det sted Herren din Gud utvelger for å la sitt navn bo der, da kan du gjøre som jeg har befalt dig, og slakte av ditt storfe og av ditt småfe, som Herren har gitt dig, og du kan ete det hjemme i dine byer efter ditt hjertes lyst.
Ngati malo amene Yehova Mulungu wanu awasankha kuti ayike Dzina lake ali kutali kwambiri ndi inu, mukhoza kupha ziweto pakati pa ngʼombe ndi nkhosa zimene Yehova wakupatsani, monga ndinakulamulani, ndipo mʼmizinda yanuyanu mukhoza kuzidya mmene mungafunire.
22 Men du skal ete det som en eter et rådyr eller en hjort; både den urene og den rene kan ete det.
Muzidye ngati mukudya gwape kapena mbawala. Onse oyeretsedwa monga mwa mwambo ndi osayeretsedwa omwe akhoza kudya.
23 Hold bare fast ved at du ikke eter blodet! For blodet er sjelen, og du skal ikke ete sjelen sammen med kjøttet.
Koma muonetsetse kuti musadye magazi, chifukwa magazi ndi moyo, ndipo musamadye moyo pamodzi ndi nyama.
24 Du skal ikke ete det; du skal helle det ut på jorden likesom vann.
Inu musamadye magazi, muziwathira pansi ngati madzi.
25 Et det ikke, så skal det gå dig vel og dine barn efter dig, når du gjør det som er rett i Herrens øine.
Musamadye magazi kuti zikuyendereni bwino inu pamodzi ndi ana anu a pambuyo panu, popeza mudzakhala mukuchita zoyenera pamaso pa Mulungu.
26 Men de hellige gaver som du vil gi, og dine lovede offer skal du ta og føre med dig til det sted som Herren utvelger.
Koma mutenge zinthu zanu zoyeretsedwa ndi china chilichonse chimene munalumbira kupereka, ndi kupita kumalo kumene Yehova adzasankhe.
27 Og du skal ofre dine brennoffer, både kjøttet og blodet, på Herrens, din Guds alter; og av dine slaktoffer skal blodet helles ut på Herrens, din Guds alter, men kjøttet kan du ete.
Mupereke nsembe zanu zopsereza pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu, nyama pamodzi ndi magazi omwe. Magazi a nsembe zanu athiridwe pambali pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu, koma nyamayo mukhoza kudya.
28 Akt vel på å lyde alle disse bud som jeg gir dig, forat det må gå dig vel og dine barn efter dig til evig tid, når du gjør det som godt og rett er i Herrens, din Guds øine.
Onetsetsani kuti muzimvera mawu onsewa amene ndikukupatsani kuti zinthu zizikuyenderani bwino nthawi zonse inu ndi ana anu chifukwa mudzakhala mukuchita zabwino ndi zoyenera pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
29 Når Herren din Gud har utryddet folkene for dig der hvor du nu kommer for å drive dem bort, og du har drevet dem bort og bor i deres land,
Yehova Mulungu wanu adzachotsa pamaso panu mitundu ya anthu amene mukufuna kuwathira nkhondo ndi kuwalanda dzikolo. Koma mukawapirikitsa ndi kukhazikika mʼdziko lawo,
30 da vokt dig at du ikke lar dig dåre og følger i deres spor, efterat de er utryddet for dig, og at du ikke spør efter deres guder og sier: Hvorledes tjente disse folk sine guder? Således vil også jeg gjøre.
ndipo pamene iwo awonongeka pamaso panu, samalirani kuti musakodwe mu msampha pa kufufuza za milungu yawo, nʼkumati, “Kodi anthu a mitunduwa amatumikira bwanji milungu yawo? Ifenso tichita momwemo.”
31 Du skal ikke gjøre som de når du dyrker Herren din Gud; for alt det som er en vederstyggelighet for Herren, og som han hater, det gjør de for sine guder; endog sine sønner og sine døtre brenner de i ilden til ære for sine guder.
Musapembedze Yehova Mulungu wanu momwe amachitira iwowo, chifukwa popembedza milungu yawoyo amachita zonyansa zamitundumitundu zimene Yehova amadana nazo. Amatentha ngakhale ana awo aamuna ndi aakazi pa moto ngati nsembe za kwa milungu yawo.
32 Alt det jeg byder eder, skal I akte vel på å gjøre; du skal ikke legge noget til og ikke ta noget fra.
Onetsetsani kuti mukuchita zimene ndikukulamulirani. Musawonjezerepo kapena kuchotserapo.

< 5 Mosebok 12 >