< Daniel 12 >
1 På den tid skal Mikael stå frem, den store fyrste som verner om ditt folks barn, og det skal komme en trengselstid som det ikke har vært fra den dag noget folk blev til, og like til den tid. Men på den tid skal alle de av ditt folk bli frelst som finnes opskrevet i boken.
“Pa nthawi imeneyo Mikayeli, mngelo wamkulu amene amateteza anthu a mtundu wako, adzabwera. Imeneyi idzakhala nthawi ya mavuto aakulu omwe sanaonekepo kuyambira pachiyambi cha mitundu ya anthu mpaka nthawi ikudzayo. Komatu pa nthawiyi anthu a mtundu wako, aliyense amene dzina lake lidzapezeke lolembedwa mʼbuku adzapulumutsidwa.
2 Og de mange som sover i jordens muld, skal våkne op, somme til evig liv og somme til skam og evig avsky.
Ambiri mwa amene akugona mʼnthaka adzadzuka: ena adzapita ku moyo wosatha, ena ku malo amanyazi ndi chilango chosatha.
3 Men de forstandige skal skinne som himmelhvelvingen skinner, og de som har ført de mange til rettferdighet, skal skinne som stjernene, evindelig og alltid.
Amene ali anzeru mʼnjira ya chilungamo adzawala ngati kuwala kwa mlengalenga, ndipo amene alondolera ambiri ku njira yolungama, adzawala ngati nyenyezi ku nthawi zosatha.
4 Og du, Daniel, gjem disse ord og forsegl boken inntil endens tid! Mange skal granske den, og kunnskapen skal bli stor.
Koma iweyo, Danieli, sungitsa mawuwa, umate bukuli kufikira nthawi ya chimaliziro. Anthu ambiri adzapita uku ndi uko ndipo nzeru zidzanka zikukulirakulira.”
5 Så fikk jeg, Daniel, i mitt syn se to andre som stod der, en på den ene elvebredd og en på den andre elvebredd.
Kenaka ine Danieli poyangʼana ndinaona anthu ena awiri atayima, wina tsidya lino la mtsinje, wina tsidya linalo.
6 Og en av dem sa til den mann som var klædd i linklær, og som stod ovenover elvens vann: Hvor lenge vil det vare før disse underfulle ting er til ende?
Mmodzi mwa awiriwo anafunsa munthu wovala chovala chosalala amene anali mʼmbali mwa madzi a mu mtsinje uja kuti, “Kodi padzapita nthawi yayitali bwanji kuti zodabwitsazi zidzakwaniritsidwe?”
7 Og jeg hørte hvad den mann sa som var klædd i linklær, og som stod ovenover elvens vann; han løftet sin høire hånd og sin venstre hånd op mot himmelen og svor ved ham som lever evindelig: En tid og tider og en halv tid, og når det hellige folks makt er fullstendig knust, skal alle disse ting fullendes.
Munthu wovala chovala chosalala, amene anali mʼmbali mwa madzi a mu mtsinje uja, anakweza dzanja lake lamanja ndi lamanzere kumwamba, ndipo ndinamumva akulumbira mʼdzina la Wamoyo ku nthawi zonse uja kuti, “Zidzachitika patapita zaka zitatu ndi theka. Zinthu zonsezi zidzachitika akadzatha masautso amene agwera anthu olungama.”
8 Og jeg hørte det, men forstod det ikke, og jeg sa: Herre! Hvad er det siste av disse ting?
Ndinamva, koma sindinamvetsetse. Choncho ndinafunsa kuti, “Mbuye wanga, nanga matsiriziro a zonsezi adzakhala chiyani?”
9 Så sa han: Gå bort, Daniel! For disse ord skal være gjemt og forseglet inntil endens tid.
Ndipo anandiyankha kuti, “Pita iwe Danieli, pakuti mawuwa ndi osungidwa ndi omatidwa kufikira nthawi ya chimaliziro.
10 Mange skal bli renset og tvettet og prøvd; men de ugudelige skal bli ved å være ugudelige, og ingen ugudelig skal forstå det; men de forstandige skal forstå det.
Anthu ambiri adzayeretsedwa nakhala olungama wopanda chodetsa, koma oyipa adzakhala chiyipire. Palibe mmodzi wa anthu oyipa amene adzamvetsetsa koma okhawo amene ali anzeru adzamvetsetsa.
11 Og fra den tid det stadige offer blir avskaffet, og den ødeleggende vederstyggelighet blir stilt op, skal det gå tusen, to hundre og nitti dager.
“Kuyambira pamene nsembe ya tsiku ndi tsiku idzathetsedwa ndi kukhazikitsa kwa chonyansa chobweretsa chisokonezo chija, padzapita masiku 1,290.
12 Salig er den som bier og når frem til tusen, tre hundre og fem og tretti dager.
Wodala munthu amene adikirabe nadzafika pa mapeto a masiku 1,335.
13 Men gå du din ende i møte! Du skal hvile og stå op til din lodd ved dagenes ende.
“Koma iweyo Danieli, pitiriza ndipo ulimbikire mpaka matsiriziro. Kenaka udzamwalira. Koma mʼmasiku otsiriza udzauka kuti ulandire gawo lako.”