< Apostlenes-gjerninge 7 >

1 Ypperstepresten sa da: Er dette sant?
Kenaka mkulu wa ansembe anafunsa Stefano kuti, “Kodi zimene akukunenerazi ndi zoona?”
2 Han svarte: Brødre og fedre! Hør på mig: Herlighetens Gud åpenbarte sig for vår far Abraham mens han var i Mesopotamia, før han hadde bosatt sig i Karan,
Stefano anayankha kuti, “Abale ndi makolo, tamverani! Mulungu waulemerero anaoneka kwa kholo lathu Abrahamu pamene ankakhala ku Mesopotamiya, asanakakhale ku Harani.
3 og sa til ham: Dra ut fra ditt land og fra din slekt, og gå til det land som jeg vil vise dig!
Mulungu anati, ‘Tuluka mʼdziko lako, siya abale ako, ndipo pita ku dziko limene ndidzakusonyeza.’
4 Så drog han ut fra kaldeernes land og bosatte sig i Karan. Og derfra lot Gud ham efter farens død flytte til dette land som I nu bor i;
“Ndipo iye anatulukadi mʼdziko la Akaldeya ndi kukakhala ku Harani. Atamwalira abambo ake, Mulungu anamuchotsa kumeneko ndi kumubweretsa mʼdziko lino limene inu mukukhalamo tsopano.
5 men han gav ham ikke arvelodd der, enn ikke en fotsbredd; og han lovte å gi ham det til eie, og hans ætt efter ham, enda han ikke hadde barn.
Mulungu sanamupatse cholowa kuno, ngakhale kadera kakangʼono kadziko. Koma Mulungu anamulonjeza kuti adzapereka dziko lino kwa iye ndi kwa zidzukulu zake, ngakhale kuti pa nthawi imeneyi analibe mwana.
6 Og Gud talte således: Hans ætt skal bo i utlendighet i et fremmed land, og de skal holde den i trældom og mishandle den i fire hundre år;
Mulungu anayankhula motere kwa iye: ‘Zidzukulu zako zidzakhala alendo mʼdziko lachilendo, ndipo zidzakhala akapolo ndi kuzunzidwa zaka 400.’
7 og det folk som de skal træle under, vil jeg dømme, sa Gud, og derefter skal de dra ut derfra og tjene mig på dette sted.
Mulungu anati, ‘Ine ndidzalanga dziko limene zidzukulu zako zidzagwireko ukapolo, ndipo pambuyo pake akadzatuluka mʼdzikolo adzandipembedza Ine pamalo pano.’
8 Og han gav ham omskjærelsens pakt; og så fikk han sønnen Isak, og omskar ham på den åttende dag, og Isak fikk sønnen Jakob, og Jakob blev far til de tolv patriarker.
Kenaka Mulungu anachita pangano la mdulidwe ndi Abrahamu. Ndipo Abrahamu, anabereka Isake, namudula ali ndi masiku asanu ndi atatu. Ndipo Isake anabereka Yakobo, Yakobo anabereka makolo khumi ndi awiri aja.
9 Og patriarkene bar avind mot Josef og solgte ham til Egypten; og Gud var med ham
“Makolo athu anachita nsanje ndi Yosefe ndipo anamugulitsa kuti akakhale kapolo ku Igupto. Koma Mulungu anali naye
10 og fridde ham ut av alle hans trengsler, og gav ham nåde og visdom for Faraos, egypterkongens øine; og han satte ham til høvding over Egypten og hele sitt hus.
ndipo anamupulumutsa iye kumasautso ake onse. Mulungu anamupatsa Yosefe nzeru ndi chisomo pamaso pa Farao mfumu ya ku Igupto, kotero mfumuyo inamuyika iye kukhala nduna yayikulu ya dziko la Igupto ndiponso nyumba yake yonse yaufumu.
11 Så kom det hungersnød over hele Egyptens land og Kana'an, og stor trengsel, og våre fedre fant ikke føde.
“Kenaka munalowa njala mʼdziko la Kanaani, kotero kuti anthu anavutika kwambiri, ndipo makolo athu sanathe kupeza chakudya.
12 Men da Jakob fikk høre at det var korn i Egypten, sendte han våre fedre dit første gang;
Pamene Yakobo anamva kuti ku Igupto kunali tirigu, iye anatuma makolo athu ulendo woyamba.
13 og annen gang blev Josef gjenkjent av sine brødre, og Josefs byrd kom til Faraos kunnskap.
Pa ulendo wawo wachiwiri, Yosefe anadziwulula kwa abale akewo ndipo Farao anadziwa za banja la Yosefe.
14 Da sendte Josef bud og kalte til sig sin far Jakob og hele sin slekt, fem og sytti sjeler.
Izi zinachitika, Yosefe anayitanitsa abambo ake Yakobo ndi banja lonse, onse pamodzi analipo 75.
15 Så drog Jakob ned til Egypten, og han døde, han og våre fedre,
Motero Yakobo anapita ku Igupto, kumene iye ndiponso makolo athu anamwalira.
16 og de blev ført til Sikem og lagt i den grav som Abraham kjøpte for en kjøpesum i sølv av Hemors barn i Sikem.
Mitembo yawo anayinyamula ndi kupita nayo ku Sekemu kumene inayikidwa mʼmanda amene Abrahamu anagula kochokera kwa ana a Hamori ku Sekemuko.
17 Efter som nu tiden nærmet sig da det løfte skulde opfylles som Gud hadde gitt Abraham, tok folket til og blev mannsterkt i Egypten,
“Nthawi itayandikira yakuti Mulungu achite zimene analonjeza kwa Abrahamu, mtundu wathu unakula ndi kuchuluka kwambiri mu Igupto.
18 inntil det fremstod en annen konge over Egypten, som ikke kjente Josef;
Pambuyo pake mfumu yatsopano imene sinkamudziwa Yosefe, inayamba kulamulira dziko la Igupto.
19 han fór med svik mot vårt folk, og ved mishandling tvang han våre fedre til å sette sine nyfødte barn ut, så de ikke skulde holdes i live.
Mfumuyo inachita mwachinyengo ndi mtundu wathu ndi kuwazunza kuti ataye ana awo akhanda kuti afe.
20 På den tid blev Moses født, og han var fager for Gud; han blev i tre måneder fostret i sin fars hus,
“Pa nthawi imeneyo Mose anabadwa, ndipo anali wokongola kwambiri. Iye analeredwa mʼnyumba ya abambo ake kwa miyezi itatu.
21 og da han var blitt utsatt, tok Faraos datter ham op, og fostret ham og tok ham i sønns sted.
Atakamutaya, mwana wamkazi wa Farao anamutola nakamulera ngati mwana wake.
22 Og Moses blev oplært i all egypternes visdom, og han var mektig i ord og gjerninger.
Mose anaphunzira nzeru zonse za Aigupto, ndipo anali wamphamvu mʼmawu ndi ntchito zake.
23 Men da han var blitt firti år gammel, fikk han i sinne å se til sine brødre, Israels barn,
“Mose ali ndi zaka makumi anayi, anaganizira zokayendera abale ake Aisraeli.
24 og da han så en lide urett, kom han ham til hjelp og hevnet den som blev mishandlet, og slo egypteren ihjel.
Iye ataona mmodzi wa iwo akuzunzidwa ndi Mwigupto, anatchinjiriza Mwisraeliyo, namupha Mwiguptoyo.
25 Han tenkte da at hans brødre skulde forstå at Gud gav dem frelse ved hans hånd; men de forstod det ikke.
Mose anaganiza kuti abale ake adzazindikira kuti Mulungu anamuyika kuti awapulumutse koma iwo sanazindikire.
26 Den næste dag kom han til dem mens de trettet, og han formante dem til å holde fred, han sa: I menn! I er brødre; hvorfor gjør I hverandre urett?
Mmawa mwake Mose anaona Aisraeli awiri akukangana. Iye anayesa kuwayanjanitsa ponena kuti, ‘Amuna inu, ndinu abale; chifukwa chiyani mukufuna kupwetekana?’
27 Men han som gjorde sin næste urett, støtte ham fra sig og sa: Hvem har satt dig til høvding og dommer over oss?
“Koma munthu amene amavutitsa mnzakeyo anakankha Mose ndipo anati, ‘Ndani anakuyika kuti ukhale wotilamulira ndi wotiweruza.
28 Vil du kanskje slå mig ihjel, som du igår slo ihjel egypteren?
Kodi ukufuna kundipha monga momwe unaphera Mwigupto uja dzulo?’
29 Men Moses flyktet for dette ords skyld, og blev en utlending i Midians land og fikk der to sønner.
Mose atamva mawu awa anathawira ku Midiyani, kumene anakhala mlendo ndipo anabereka ana amuna awiri.
30 Og da firti år var til ende, åpenbarte en engel sig for ham i berget Sinais ørken i en brennende tornebusk.
“Ndipo patapita zaka makumi anayi mngelo anaonekera kwa Mose mʼmalawi amoto pa chitsamba mʼchipululu pafupi ndi Phiri la Sinai.
31 Da Moses så det, undret han sig over synet; men da han gikk bort for å se på det, kom en røst fra Herren:
Iye ataona zimenezi, anadabwa. Akupita kuti akaonetsetse pafupi, Mose anamva mawu a Ambuye:
32 Jeg er dine fedres Gud, Abrahams og Isaks og Jakobs Gud. Men Moses skalv av redsel, og vågde ikke å se på det.
‘Ine ndine Mulungu wa makolo ako, Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Yakobo.’ Mose ananjenjemera chifukwa cha mantha ndipo sanalimbe mtima kuyangʼananso.
33 Og Herren sa til ham: Løs skoene av dine føtter! for det sted du står på, er hellig jord.
“Ndipo Ambuye anati kwa Mose, ‘Vula nsapato zako, pakuti malo amene wayimapo ndi opatulika.
34 Jeg har grant sett hvor mitt folk blir mishandlet i Egypten, og deres sukk har jeg hørt, og jeg er steget ned for å utfri dem. Og nu, kom, la mig sende dig til Egypten!
Ine ndaona ndithu mazunzo a anthu anga amene ali ku Igupto. Ndamva kulira kwawo choncho ndabwera kuti ndiwapulumutse. Tsopano tiye ndikutume ku Igupto.’
35 Denne Moses som de fornektet, idet de sa: Hvem har satt dig til høvding og dommer? ham sendte Gud til å være både høvding og redningsmann ved den engels hånd som åpenbarte sig for ham i tornebusken.
“Uyu ndi Mose yemwe uja amene Aisraeli anamukana ndi kunena kuti, ‘Ndani anakuyika kuti ukhale wotilamulira ndi wotiweruza?’ Iyeyo anatumidwa ndi Mulungu mwini kuti akakhale wowalamulira ndiponso mpulumutsi, mothandizidwa ndi mngelo amene anamuonekera pa chitsamba.
36 Han var den som førte dem ut, idet han gjorde undergjerninger og tegn i Egyptens land og i det Røde Hav og i ørkenen i firti år.
Iye anawatulutsa mu Igupto ndipo anachita zodabwitsa ndi zizindikiro zozizwitsa mu Igupto, pa Nyanja Yofiira, ndiponso mʼchipululu kwa zaka makumi anayi.
37 Han er den Moses som sa til Israels barn: En profet, likesom mig, skal Gud opreise eder av eders brødre.
“Uyu ndi Mose uja amene anati kwa Aisraeli, ‘Mulungu adzawutsa pakati pa abale anu mneneri ngati ine.’
38 Han er den som i menigheten i ørkenen var med den engel som talte til ham på Sinai berg, og med våre fedre, han som mottok levende ord for å gi oss dem.
Iyeyu anali mʼgulu la Aisraeli mʼchipululu pamodzi ndi mngelo amene anamuyankhula pa phiri la Sinai ndiponso makolo athu; ndipo Mose analandira mawu amoyo kuti atipatse ife.
39 Ham vilde våre fedre ikke være lydige, de støtte ham fra sig, og vendte sig i sitt hjerte til Egypten, og de sa til Aron:
“Koma makolo athu anakana kumumvera iye. Iwo anamukana iye ndipo mʼmitima mwawo anatembenukira ku Igupto.
40 Gjør oss guder som kan dra foran oss! for denne Moses som førte oss ut av Egyptens land vi vet ikke hvad det er blitt av ham.
Iwo anati kwa Aaroni, ‘Bwera utipangire milungu imene idzititsogolera. Kunena za Mose amene anatitsogolera kutuluka mʼdziko la Igupto, sitikudziwa chimene chamuchitikira.
41 Og de gjorde en kalv i hine dager og bar frem offer til avgudsbilledet, og de gledet sig over sine henders verk.
Iyi ndi nthawi imene anapanga fano la mwana wangʼombe. Anapereka nsembe kwa fanoli nachita chikondwerero kulemekeza ntchito ya manja awo.
42 Men Gud vendte sig bort, og overgav dem til å dyrke himmelens hær, som skrevet er i profetenes bok: Israels hus! gav I mig vel slaktoffer og andre offer i firti år i ørkenen?
Koma Mulungu anawafulatira, nawapereka kuti apembedze zolengedwa zakumwamba. Zimenezi zikugwirizana ndi zimene zinalembedwa mʼbuku la aneneri kuti, “‘Kodi pa zaka makumi anayi zimene munakhala mʼchipululu muja munkandibweretsera nsembe ndi zopereka, inu nyumba ya Israeli?’
43 Nei, I bar med eder Moloks telt og guden Remfans stjerne, de billeder som I gjorde for å tilbede dem, og jeg vil flytte eder bort hinsides Babylon.
Ayi, inu mwanyamula tenti ya Moloki ndi nyenyezi ya mulungu wanu Refani, mafano amene munapanga kuti muziwapembedza. Chifukwa chake, Ine ndidzakutumizani kutali, kupitirira dziko la Babuloni.
44 Våre fedre hadde i ørkenen vidnesbyrdets telt, således som den som talte til Moses, bød ham å gjøre det efter det forbillede han hadde sett;
“Makolo athu anali ndi tenti ya msonkhano pakati pawo mʼchipululu. Anayipanga monga momwe Mulungu anawuzira Mose, molingana ndi chithunzi chimene Mose anachiona.
45 dette tok våre fedre i arv, og førte det med Josva inn i de hedningers eiendomsland som Gud drev bort for våre fedre, inntil Davids dager.
Makolo athu, atayilandira Tentiyo, anabwera nayo motsogozedwa ndi Yoswa pamene analanda dziko la mitundu imene Mulungu anayipirikitsa pamaso pawo. Tentiyo inakhala mʼdzikomo mpaka nthawi ya Davide,
46 Han fant nåde hos Gud, og bad om at han måtte finne et bosted for Jakobs Gud.
amene anapeza chisomo pamaso pa Mulungu ndipo anapempha kuti amʼmangire nyumba Mulungu wa Yakobo.
47 Men Salomo bygget ham et hus.
Koma anali Solomoni amene anamanga nyumbayo.
48 Men den Høieste bor ikke i hus som er gjort med hender, således som profeten sier:
“Komatu, Wammwambamwambayo sakhala mʼnyumba zomangidwa ndi anthu. Monga mneneri akunena kuti,
49 Himmelen er min trone, og jorden en skammel for mine føtter; hvad hus vil I bygge mig, sier Herren, eller hvor er det sted jeg skal hvile på?
“‘Kumwamba ndi mpando wanga waufumu, ndipo dziko lapansi ndi chopondapo mapazi anga. Kodi mudzandimangira nyumba yotani? Akutero Ambuye. Kapena malo opumuliramo Ine ali kuti?
50 Har ikke min hånd gjort alt dette?
Kodi si dzanja langa linapanga zonsezi?’
51 I hårde halser og uomskårne på hjerte og ører! I står alltid den Hellige Ånd imot, som eders fedre, således også I.
“Anthu wokanika inu, osachita mdulidwe wa mu mtima ndi a makutu ogontha! Inu ofanana ndi makolo anu. Nthawi zonse mumakana kumvera Mzimu Woyera:
52 Hvem av profetene forfulgte ikke eders fedre? De drepte dem som forut forkynte at den rettferdige skulde komme, han som I nu har forrådt og myrdet,
Kodi analipo mneneri amene makolo anu sanamuzunze? Iwo anapha ngakhale amene ananeneratu za kubwera kwa Wolungamayo. Ndipo tsopano inu munamupereka ndi kumupha Iye.
53 I som mottok loven gitt ved engler og ikke har holdt den!
Inu amene munalandira Malamulo amene anaperekedwa ndi angelo ndipo simunawamvere.”
54 Men da de hørte dette, stakk det dem i deres hjerter, og de skar tenner mot ham.
Atamva zimenezi, iwo anakwiya kwambiri ndipo anamukukutira mano.
55 Men han var full av den Hellige Ånd og skuet ufravendt op mot himmelen, og han så Guds herlighet, og Jesus stå ved Guds høire hånd,
Koma Stefano, wodzaza ndi Mzimu Woyera, anayangʼana kumwamba ndipo anaona ulemerero wa Mulungu ndiponso Yesu atayimirira ku dzanja lamanja la Mulungu.
56 og han sa: Nu ser jeg himlene åpne, og Menneskesønnen stå ved Guds høire hånd!
Stefano anati, “Taonani, ndikuona kumwamba kotsekuka ndiponso Mwana wa Munthu atayimirira ku dzanja la manja la Mulungu.”
57 Da skrek de med høi røst og holdt for sine ører, og stormet alle som en inn på ham
Koma iwo anatseka mʼmakutu mwawo, ndipo anafuwula kolimba, onse anathamangira kwa iye,
58 og drev ham ut av byen og stenet ham; og vidnene la sine klær av sig ved en ung manns føtter som hette Saulus.
anamukokera kunja kwa mzinda ndipo anayamba kumugenda miyala. Mboni zinasungitsa zovala zawo kwa mnyamata otchedwa Saulo.
59 Og de stenet Stefanus, mens han bad og sa: Herre Jesus, ta imot min ånd!
Akumugenda miyala, Stefano anapemphera kuti, “Ambuye Yesu, landirani mzimu wanga.”
60 Og han falt på kne og ropte med høi røst: Herre, tilregn dem ikke denne synd! Og som han hadde sagt dette, sov han inn.
Ndipo anagwada pansi nafuwula mwamphamvu kuti, “Ambuye musawawerengere tchimoli.” Atanena mawu amenewa anamwalira.

< Apostlenes-gjerninge 7 >