< Apostlenes-gjerninge 6 >
1 I disse dager da disiplenes tall øket, gav de gresktalende jøder sig til å knurre mot hebreerne over at deres enker blev satt til side ved den daglige utdeling.
Mʼmasiku amenewo pamene chiwerengero cha ophunzira chinkachuluka, Ayuda a Chihelene pakati pawo anadandaula chifukwa cha Ayuda a Chihebri chifukwa amasiye awo samawagawira chakudya cha tsiku ndi tsiku.
2 Da kalte de tolv hele disippelskaren sammen og sa: Det er ikke tilbørlig at vi forlater Guds ord og gjør tjeneste ved bordene;
Tsono Atumwi khumi ndi awiriwo anasonkhanitsa ophunzira onse pamodzi ndipo anati, “Nʼkosayenera kuti ife tisiye kulalikira Mawu a Mulungu ndi kuyangʼanira za chakudya.
3 utse derfor iblandt eder, brødre, syv menn som har godt vidnesbyrd, fulle av Ånd og visdom! dem vil vi innsette til å røkte dette hverv;
Choncho abale, sankhani pakati panu anthu asanu ndi awiri a mbiri yabwino, odzazidwa ndi Mzimu Woyera ndi anzeru. Ife tidzawapatsa udindo oyangʼanira.
4 vi derimot vil holde ved i bønnen og ordets tjeneste.
Koma ife tidzadzipereka kuti tizipemphera ndi kulalikira mawu.”
5 Dette ord syntes hele skaren godt om, og de valgte Stefanus, en mann full av tro og den Hellige Ånd, og Filip og Prokorus og Nikanor og Timon og Parmenas og Nikolaus, en tilhenger av jødenes tro, fra Antiokia;
Mawu amenewa anakondweretsa gulu lonse la anthu. Iwo anasankha, Stefano, munthu wodzazidwa ndi chikhulupiriro ndiponso Mzimu Woyera; anasankhanso Filipo, Prokoro, Nikanora, Timo, Parmena ndi Nikolao amene anatembenuka mtima ndi kulowa Chiyuda kuchokera kwa Antiokeya.
6 dem stilte de frem for apostlene, og disse bad og la sine hender på dem.
Iwo anapereka anthuwa kwa atumwi amene anawapempherera ndi kuwasanjika manja.
7 Og Guds ord hadde fremgang, og tallet på disiplene i Jerusalem øket sterkt, og en stor mengde av prestene blev lydige mot troen.
Ndipo Mawu a Mulungu anapitirira kufalikira. Chiwerengero cha ophunzira mu Yerusalemu chinakula mofulumira ndipo ansembe ochuluka anakhulupirira.
8 Men Stefanus var full av nåde og kraft, og gjorde undergjerninger og store tegn blandt folket.
Stefano, munthu wodzazidwa ndi chisomo cha Mulungu ndi mphamvu anachita zodabwitsa ndiponso zizindikiro zazikulu pakati pa anthu.
9 Da stod nogen frem av den synagoge som kalles de frigittes og kyreneernes og aleksandrinernes, og av dem fra Kilikia og Asia, og de innlot sig i ordskifte med Stefanus,
Panauka mtsutso kuchokera kwa anthu a ku Kurene ndi a ku Alekisandriya komanso a ku dera la Silisiya ndi Asiya, otchedwa a Sunagoge ya Mfulu. Anthu amenewa anayamba kutsutsana ndi Stefano.
10 og de var ikke i stand til å stå sig mot den visdom og den Ånd han talte av.
Koma iwo sanathe kumugonjetsa chifukwa iye ankayankhula ndi nzeru zimene Mzimu Woyera anamupatsa.
11 Da traff de lønnlig avtale med nogen menn som sa: Vi har hørt ham tale bespottelige ord mot Moses og Gud.
Iwo ananyengerera anthu ena mwamseri kuti anene kuti, “Ife tinamva Stefano akuchitira chipongwe Mose ndiponso Mulungu.”
12 Og de opegget folket og de eldste og de skriftlærde, og de falt over ham og drog ham avsted og førte ham for rådet,
Motero anawutsa mitima ya anthu, akulu ndi aphunzitsi amalamulo. Anamugwira Stefano ndi kumubweretsa ku Bwalo Lalikulu.
13 og stilte frem falske vidner som sa: Dette menneske holder ikke op med å tale mot det hellige sted og mot loven;
Iwo anabweretsa mboni zonama zimene zinati, “Munthu uyu akupitirirabe kuyankhula mawu onyoza malo oyera ndi malamulo.
14 for vi har hørt ham si at denne Jesus fra Nasaret skal bryte ned dette sted og forandre de skikker som Moses gav oss.
Pakuti tinamumva akunena kuti Yesu uja wa ku Nazareti adzawononga malo ano ndiponso kusintha miyambo imene Mose anatipatsa.”
15 Og da alle de som satt i rådet, stirret på ham, så de hans ansikt som en engels ansikt.
Onse amene anakhala pansi Mʼbwalo Lalikulu anamuyangʼanitsitsa Stefano, ndipo anaona kuti nkhope yake ikuwala ngati ya mngelo.