< Apostlenes-gjerninge 11 >
1 Apostlene og de brødre som var omkring i Judea, fikk da høre at også hedningene hadde tatt imot Guds ord.
Atumwi ndi abale a ku Yudeya konse anamva kuti anthu a mitundu ina analandiranso Mawu a Mulungu.
2 Da nu Peter kom op til Jerusalem, gikk de av omskjærelsen i rette med ham og sa:
Tsono Petro atafika ku Yerusalemu, abale amene anali a mdulidwe anamutsutsa iye,
3 Du gikk inn til uomskårne menn og åt med dem.
ndipo anati, “Iwe unalowa mʼnyumba ya anthu osachita mdulidwe ndi kudya nawo.”
4 Men Peter begynte da fra først av og la det ut i sammenheng og sa:
Koma Petro anayamba kuwafotokozera zonse mwatsatanetsatane momwe zinachitikira kuti,
5 Jeg var i byen Joppe og bad; da så jeg i en henrykkelse et syn: Det dalte ned noget, likesom en stor duk, som blev senket ned fra himmelen efter de fire hjørner, og det kom like bort til mig;
“Ine ndimapemphera mu mzinda wa Yopa ndipo ndili ngati wokomoka ndinaona masomphenya. Ndinaona chinthu chokhala ngati chinsalu chachikulu chikutsika kuchokera kumwamba chogwiridwa msonga zake zinayi, ndipo chinatsikira pa ine.
6 da jeg stirret på den og så nøie efter, blev jeg var jordens firføtte dyr og ville og krypende dyr og himmelens fugler.
Ine ndinayangʼana mʼkati mwake ndipo ndinaona nyama za miyendo inayi za mʼdziko lapansi, zirombo, zokwawa, ndi mbalame zamlengalenga.
7 Jeg hørte også en røst som sa til mig: Stå op, Peter! slakt og et!
Kenaka ine ndinamva mawu akuti, ‘Petro, Imirira. Ipha, nudye.’
8 Men jeg sa: Ingenlunde, Herre! aldri er noget vanhellig eller urent kommet i min munn.
“Ine ndinayankha kuti, ‘Ayi, Ambuye! Pakuti chinthu chodetsedwa ndi chonyansa sindinadyepo pakamwa pangapa.’
9 En røst fra himmelen svarte mig da annen gang: Det som Gud har renset, det må ikke du gjøre til urent.
“Mawu ochokera kumwamba ananenanso kachiwiri kuti, ‘Chimene Mulungu wachiyeretsa usanene kuti ndi chodetsedwa.’
10 Dette skjedde tre ganger; og det blev alt sammen dradd op igjen til himmelen.
Zimenezi zinachitika katatu ndipo kenaka zonse zinatengedwa kupita kumwamba.
11 Og se, i det samme stod tre menn utenfor huset der jeg var; de var utsendt til mig fra Cesarea,
“Nthawi yomweyo anthu atatu amene anatumidwa kuchokera ku Kaisareya anayima pa nyumba yomwe ndimakhalayo.
12 Og Ånden sa til mig at jeg skulde gå med dem uten å tvile; disse seks brødre drog også med mig; og vi kom inn i mannens hus.
Mzimu anandiwuza kuti ndisakayike, koma ndipite nawo. Abale asanu ndi mmodzi awa anapitanso nane ndipo tinalowa mʼnyumba ya munthuyo.
13 Og han fortalte oss hvorledes han hadde sett engelen som stod i hans hus og sa til ham: Send bud til Joppe og hent til dig Simon som kalles med tilnavn Peter!
Iye anatiwuza mmene anaonera mngelo atayimirira mʼnyumba mwake ndi kumuwuza kuti, ‘Tumiza anthu ku Yopa kuti akayitane Simoni wotchedwa Petro.
14 han skal tale ord til dig som du skal bli frelst ved, du og hele ditt hus.
Iye adzakuwuza uthenga umene udzapulumutsa iwe ndi a pa banja ako.’
15 Men da jeg begynte å tale, falt den Hellige Ånd på dem, likesom på oss i begynnelsen.
“Nditangoyamba kuyankhula, Mzimu Woyera anafika pa iwo monga momwe anafikira pa ife poyamba paja.
16 Da kom jeg Herrens ord i hu, at han sa: Johannes døpte med vann, men I skal døpes med den Hellige Ånd.
Kenaka ndinakumbukira zimene Ambuye ananena kuti, ‘Yohane anabatiza ndi madzi, koma inu mudzabatizidwa ndi Mzimu Woyera.’
17 Gav nu altså Gud dem den samme gave som han gav oss, da de var kommet til troen på den Herre Jesus Kristus, hvem var da vel jeg, at jeg skulde være i stand til å hindre Gud?
Tsono ngati Mulungu anawapatsa iwo mphatso yomweyo imene anatipatsa ife, amene tinakhulupirira Ambuye Yesu Khristu, ndine yani kuti nditsutsane ndi Mulungu?”
18 Da de hørte dette, slo de sig til ro, og de priste Gud og sa: Så har da Gud også gitt hedningene omvendelsen til livet.
Iwo atamva zimenezi analibenso chonena ndipo anayamika Mulungu nati, “Potero Mulungu wapatsa anthu a mitundu ina mwayi wotembenuka mtima ndi kulandira moyo.”
19 De som nu var adspredt på grunn av den trengsel som opstod for Stefanus' skyld, drog omkring like til Fønikia og Kypern og Antiokia, men talte ikke ordet til andre enn jøder.
Tsopano amene anabalalika chifukwa cha mazunzo amene anayamba ataphedwa Stefano, anapita mpaka ku Foinike, ku Kupro ndi ku Antiokeya, ndipo ankalalikira kwa Ayuda okha.
20 Men iblandt dem var det nogen menn fra Kypern og Kyrene, som kom til Antiokia, og der talte de også til grekerne og forkynte dem evangeliet om den Herre Jesus.
Komabe, ena pakati pawo ochokera ku Kupro ndi ku Kurene anapita ku Antiokeya ndipo iwo anayamba kuyankhulanso kwa Agriki, nawawuza za Uthenga Wabwino wa Ambuye Yesu.
21 Og Herrens hånd var med dem, og et stort tall kom til troen og omvendte sig til Herren.
Mphamvu ya Ambuye inali nawo ndipo anthu ambiri anakhulupirira natembenukira kwa Ambuye.
22 Denne tidende kom da menigheten i Jerusalem for øre, og de sendte Barnabas ut for å dra til Antiokia;
Mbiri imeneyi inamveka ku mpingo wa ku Yerusalemu ndipo iwo anatumiza Barnaba ku Antiokeya.
23 da han kom dit og så Guds nåde, gledet han sig, og han formante alle til at de med hjertets forsett skulde holde fast ved Herren;
Atafika ndi kuona chisomo cha Mulungu pa iwo, anakondwa ndi kuwalimbikitsa anthu onsewo kuti apitirire kukhala woona mu mtima mwa Ambuye.
24 for han var en god mann og full av den Hellige Ånd og tro. Og en stor skare blev vunnet for Herren.
Barnabayo anali munthu wabwino, wodzazidwa ndi Mzimu Woyera ndi chikhulupiriro ndipo gulu lalikulu la anthu linabwera kwa Ambuye.
25 Han drog da ut til Tarsus for å opsøke Saulus, og da han hadde funnet ham, førte han ham til Antiokia.
Kenaka Barnaba anapita ku Tarisisi kukafuna Saulo,
26 Og et helt år var de sammen der i menigheten og lærte en stor skare, og i Antiokia fikk disiplene først navnet kristne.
ndipo pamene anamupeza anabwera naye ku Antiokeya. Barnaba ndi Saulo anasonkhana ndi mpingo kwa chaka chimodzi naphunzitsa anthu ambirimbiri. Okhulupirirawo anayamba kutchedwa Akhristu ku Antiokeya.
27 I disse dager kom det nogen profeter ned fra Jerusalem til Antiokia,
Masiku amenewo ku Antiokeya kunafika aneneri ena ochokera ku Yerusalemu.
28 og en av dem, ved navn Agabus, stod op og varslet ved Ånden at det skulde komme en stor hungersnød over hele jorderike; den kom også under Klaudius.
Mmodzi wa iwo dzina lake Agabu, anayimirira ndipo Mzimu anamutsogolera kunenera zamʼtsogolo kuti padzakhala njala yayikulu pa dziko lonse lapansi. (Izi zinachitikadi nthawi ya ulamuliro wa Klaudiyo).
29 Disiplene vedtok da, alt efter som enhver av dem hadde råd til, å sende noget til hjelp for de brødre som bodde i Judea.
Ophunzirawo, aliyense monga mwakupata kwake, anatsimikiza kuthandiza abale okhala ku Yudeya.
30 Dette gjorde de også, og de sendte det med Barnabas og Saulus til de eldste.
Izi anazichitadi ndipo anatuma Barnaba ndi Saulo kukapereka mphatsozo kwa akulu a mpingo.