< 3 Johannes 1 >

1 Den eldste - til Gajus, den elskede, som jeg elsker i sannhet.
Ndine mkulu wampingo, kulembera: Gayo mnzanga wokondedwa, amene ndimamukonda mʼchoonadi.
2 Du elskede! jeg ønsker at du i alle deler må ha det godt og være ved god helse, likesom din sjel har det godt.
Wokondedwa, ndimakupempherera kuti zako zonse zikuyendere bwino, ndikuti ukhale bwino mʼthupi mwako, monga momwe ulili moyo wako wauzimu.
3 For jeg blev meget glad da det kom nogen brødre og vidnet om din sannhet, således som du vandrer i sannhet.
Ine ndinali ndi chimwemwe chachikulu pamene abale ena anafika nʼkundifotokozera za kukhulupirika kwako pa choonadi ndiponso mmene umayendera motsata choonadi.
4 Større glede har jeg ikke enn dette at jeg hører mine barn vandrer i sannheten.
Palibe chondikondweretsa kwambiri kuposa kumva kuti ana anga akukhala mʼchoonadi.
5 Du elskede! du gjør en trofast gjerning med det du gjør imot brødrene, enda de er fremmede,
Wokondedwa, ndiwe wokhulupirika pa zimene ukuchitira abale, ngakhale kuti iwowo ndi alendo.
6 og de har vidnet om din kjærlighet for menigheten. Du vil gjøre vel om du hjelper dem på vei, således som det sømmer sig for Gud;
Iwo anafotokozera mpingo za chikondi chako. Chonde uwathandize kupitiriza ulendo mʼnjira yokondweretsa Mulungu.
7 for det var for hans navns skyld de drog ut, og av hedningene tar de ikke imot noget.
Pakuti ananyamuka ulendo wawo chifukwa cha dzina la Ambuye, osalandira thandizo kwa osakhulupirira.
8 Vi er derfor skyldige å ta oss av slike, forat vi kan bli medarbeidere for sannheten.
Ife tiyenera kumathandiza anthu oterewa, kuti tigwirizane nawo pa ntchito ya choonadi.
9 Jeg har skrevet noget til menigheten; men Diotrefes, som gjerne vil være førstemann iblandt dem, tar ikke imot oss.
Ndinalembera mpingo, koma Diotrefe, amene amafuna kukhala wotsogolera, sanafune kutimvera.
10 Derfor vil jeg, når jeg kommer, minne om de gjerninger som han gjør, idet han baktaler oss med onde ord; og ikke tilfreds med dette tar han ikke selv imot brødrene, og dem som vil det, hindrer han og støter dem ut av menigheten.
Tsono ndikabwera ndidzakumbutsa zimene iye amachita. Iye amafalitsa nkhani zabodza zonena ife. Ndipo sakhutira ndi zimenezo, komanso iyeyo amakana kulandira abale. Komanso amaletsa amene akufuna kutero, ndipo amawachotsa mu mpingo.
11 Du elskede! ta ikke efter det onde, men det gode! Den som gjør det gode, er av Gud; den som gjør det onde, har ikke sett Gud.
Wokondedwa, usatsatire zinthu zoyipa koma zinthu zabwino. Aliyense amene amachita zinthu zabwino ndi wochokera kwa Mulungu. Aliyense amene amachita zoyipa sanamuonepo Mulungu.
12 Demetrius har godt lov av alle, og av sannheten selv; men også vi gir ham godt vidnesbyrd, og du vet at vårt vidnesbyrd er sant.
Aliyense akumuchitira umboni wabwino wa Demetriyo. Ngakhale choona chomwe chimamuchitira umboni, ndipo iweyo ukudziwa kuti umboni wathu ndi woona.
13 Jeg hadde meget å skrive til dig, men jeg vil ikke skrive til dig med blekk og penn;
Ndili ndi zambiri zoti ndikulembereni, koma sindikufuna kuzilemba mʼkalata.
14 men jeg håper snart å få se dig, og så skal vi tale muntlig sammen. Fred være med dig! Vennene hilser dig. Hils vennene ved navn!
Ndiyembekezera kufika kwanuko posachedwapa, ndipo tidzakambirana pamaso ndi pamaso. Mtendere ukhale nawe. Abwenzi anu kuno akupereka moni. Upereke moni kwa abwenzi onse mmodzimmodzi.

< 3 Johannes 1 >