< 2 Samuel 20 >
1 Nu traff det sig så at det på det sted var en illesinnet mann som hette Seba, sønn av Bikri, en benjaminitt. Han støtte i basunen og sa: Vi har ingen del i David og ingen lodd i Isais sønn; hver mann til sine telt, Israel!
Ndipo munthu wina wokonda kuyambitsa chisokonezo, dzina lake Seba, mwana wa Bikiri wa fuko la Benjamini, anali komweko. Iye analiza lipenga ndipo anafuwula kuti, “Ife tilibe chathu mu mfumu wa Davide, tilibe gawo mwa mwana wa Yese! Inu Aisraeli aliyense apite ku nyumba kwake!”
2 Da forlot hver mann av Israel David og fulgte Seba, Bikris sønn, men Judas menn hang ved sin konge og fulgte ham fra Jordan like til Jerusalem.
Kotero Aisraeli onse anamuthawa Davide ndipo anatsatira Seba mwana wa Bikiri. Koma anthu a ku Yuda anakhala ndi mfumu yawo njira yonse kuchokera ku Yorodani mpaka ku Yerusalemu.
3 Så kom David hjem til Jerusalem. Og kongen tok de ti medhustruer som han hadde latt bli tilbake for å ta vare på huset, og lot dem bo i et hus for sig selv under varetekt; han forsørget dem med det nødvendige, men gikk ikke inn til dem. Der satt de nu innestengt til sin dødsdag og levde hele resten av sitt liv som enker.
Davide atabwerera ku nyumba yake yaufumu ku Yerusalemu, iye anatenga azikazi khumi aja amene anawasiya kuti aziyangʼanira nyumba yaufumu, ndipo anawayika mʼnyumba imene anayikapo mlonda. Iye ankawadyetsa koma sanagone nawonso. Anasungidwa kwa okha mpaka tsiku la kufa kwawo ndipo anakhala ngati akazi amasiye.
4 Så sa kongen til Amasa: Kall Judas menn sammen for mig innen tre dager og møt så selv frem her!
Kenaka mfumu inati kwa Amasa, “Itanitsa ankhondo a Yuda kuti abwere kwa ine pasanathe masiku atatu, ndipo iwe udzakhale nawo.”
5 Amasa tok da avsted for å kalle Juda sammen; men han drygde lenger enn den tid som var fastsatt.
Motero Amasa anakayitana Ayuda, koma anachedwa, napitirira pa nthawi imene mfumu inamuyikira.
6 Da sa David til Abisai: Nu kommer Seba, Bikris sønn, til å gjøre oss mere ondt enn Absalom; ta du din herres menn og sett efter ham! Bare han ikke alt har funnet faste byer og har undsloppet oss!
Davide anati kwa Abisai, “Tsono Seba mwana wa Bikiri adzatipweteka kuposa momwe Abisalomu anatichitira. Tenga asilikali a mbuye wako ndipo umuthamangitse, mwina adzapeza mizinda yotetezedwa ndi kutithawa ife.”
7 Så drog da Joabs menn og livvakten og alle de djerveste stridsmenn ut efter ham; de drog ut fra Jerusalem for å sette efter Seba, Bikris sønn.
Kotero anthu a Yowabu, Akereti ndi Apeleti ndiponso asilikali onse amphamvu anapita motsogozedwa ndi Abisai. Iwo anayenda kuchokera ku Yerusalemu kuthamangitsa Seba mwana wa Bikiri.
8 De var nettop kommet til den store sten ved Gibeon, da kom Amasa imot dem. Joab hadde på sig kappen som var hans vanlige drakt, og utenpå den et belte med et sverd i skjeden, fastbundet over hans lender, og da han gikk frem, falt det ut.
Ali pa mwala waukulu wa ku Gibiyoni, Amasa anabwera kudzakumana nawo. Yowabu anali atavala chovala chausilikali ndipo pamwamba pa malayawo, mʼchiwuno mwake anavala lamba womangirirapo lupanga lili moyikamo mwakemo. Akuyenda linasololoka kuchoka moyikamo mwake.
9 Og Joab sa til Amasa: Går det dig vel, bror? og grep med sin høire hånd fatt i Amasas skjegg for å kysse ham.
Yowabu anati kwa Amasa, “Kodi uli bwanji mʼbale wanga?” Kenaka Yowabu anamugwira ndevu Amasa uja ndi dzanja lake lamanja ndi kupsompsona.
10 Men Amasa tok sig ikke i vare for sverdet som Joab hadde i hånden, og Joab stakk ham med det i underlivet, så hans innvoller rant ut på jorden. Han stakk ham ikke mere enn denne ene gang, så var han død. Derefter satte Joab og hans bror Abisai efter Seba, Bikris sønn.
Amasa sanayangʼanitsitse lupanga limene linali mʼdzanja la Yowabu, ndipo Yowabu anamubaya nalo mʼmimba ndipo matumbo ake anatuluka ndi kugwera pansi. Popanda kubayanso kachiwiri, Amasa anafa. Ndipo Yowabu ndi mʼbale wake Abisai anathamangitsa Seba mwana wa Bikiri.
11 Men en av Joabs unge menn blev stående hos Amasa og ropte: Hvem som holder med Joab, og som står på Davids side, følge Joab!
Mmodzi mwa ankhondo a Yowabu anakayimirira pafupi ndi mtembo wa Amasa ndipo anati, “Aliyense amene amakonda Yowabu ndi aliyense amene ali wa Davide, atsatire Yowabu!”
12 Men Amasa lå veltet i sitt blod midt på landeveien, og da mannen så at alt folket blev stående. flyttet han Amasa fra landeveien bort på marken og kastet et klæde over ham, fordi han så at enhver som kom bort til ham, blev stående.
Amasa anagona pakati pa msewu atasamba magazi ake, ndipo munthuyo anaona kuti asilikali onse amayima pamenepo. Atazindikira kuti aliyense amene ankafika pamene panali Amasa amayima, iye anamuchotsa mu msewu ndi kumukokera mʼmunda ndipo anamuphimba ndi nsalu.
13 Da han var ført bort fra landeveien, gikk hver mann forbi og fulgte Joab for å sette efter Seba, Bikris sønn.
Amasa atachotsedwa pa msewu anthu onse anapita ndi Yowabu kuthamangitsa Seba mwana wa Bikiri.
14 Han drog frem gjennem alle Israels stammer til Abel og Bet-Ma'aka og hele Berim; og de samlet sig og fulgte også efter ham.
Seba anadutsa mafuko onse a Israeli mpaka ku Abeli ndi Beti-Maaka ndiponso chigawo chonse cha Abeli, amene anasonkhana pamodzi ndi kumutsata iye.
15 Og de kom og kringsatte ham i Abel-Bet-Ma'aka og opkastet en voll mot byen; den støtte op mot yttermuren; og alt folket som var med Joab, var i ferd med å ødelegge muren for å få den til å falle.
Ankhondo onse pamodzi ndi Yowabu anafika ndi kumuzungulira Seba mu Abeli-Beti-Maaka. Iwo anapanga mzere wa nkhondo mpaka ku mzinda, ndipo unayangʼanana ndi malo otetezera a kunja. Pamene amalimbana ndi khoma kuti aligwetse,
16 Da ropte en klok kvinne fra byen: Hør, hør! Si til Joab: Kom nærmere, så jeg kan få tale med dig!
mayi wina wanzeru anafuwula kuchokera mu mzindawo, “Tamverani! Tamverani! Muwuzeni Yowabu abwere pano kuti ndiyankhule naye.”
17 Da gikk han bort til henne, og kvinnen spurte: Er du Joab? Han svarte: Ja. Hun sa til ham: Hør din tjenerinnes ord! Han svarte: Jeg hører.
Yowabu anayandikira kumene kunali mayiyo, ndipo iye anafunsa kuti, “Kodi ndinu Yowabu?” Iye anayankha kuti, “Ndine.” Mayiyo anati, “Tamverani zimene mtumiki wanu akuti anene.” Yowabu anayankha kuti, “Ndikumvetsera.”
18 Da sa hun: Før pleide folk å si så: En skal spørre sig for i Abel, og så utførte de det.
Iye anapitiriza kunena kuti, “Kalekale ankanena kuti, ‘Kapeze yankho lako ku Abeli,’ ndipo nkhani imathera pamenepo.
19 Jeg er en av de fredsommelige og trofaste i Israel; du søker å ødelegge en by, en mor i Israel, hvorfor vil du tilintetgjøre Herrens arv?
Ife ndife anthu a mtendere ndi okhulupirika mu Israeli. Inu mukufuna kuwononga mzinda umene ndi mayi mu Israeli. Nʼchifukwa chiyani mukufuna kufafaniza cholowa cha Yehova?”
20 Da svarte Joab og sa: Langt, langt være det fra mig at jeg skulde tilintetgjøre eller ødelegge.
Yowabu anayankha kuti, “Ayi ndisatero. Ine sindikufuna kuwufafaniza kapena kuwuwononga.
21 Det har sig ikke så. Men en mann fra Efra'im-fjellet som heter Seba, sønn av Bikri, har løftet sin hånd mot kongen, mot David; la mig bare få ham, så skal jeg dra bort fra byen. Da sa kvinnen til Joab: Hans hode skal bli kastet ut til dig over muren.
Nkhani simeneyo ayi. Koma munthu wina wa ku dziko lamapiri la Efereimu, dzina lake Seba mwana wa Bikiri, wawukira mfumu Davide. Muperekeni munthuyo ndipo ine ndidzachoka pa mzinda uno.” Mayiyo anati kwa Yowabu, “Mutu wake tikuponyerani pa khoma pano.”
22 Så gikk kvinnen med sitt kloke råd til alt folket, og de hugg hodet av Seba, Bikris sønn, og kastet det ut til Joab. Da støtte han i basunen, og de drog bort fra byen og spredte sig hver mann til sitt hjem; og Joab vendte tilbake til Jerusalem, til kongen.
Ndipo mayiyo anapita kwa anthu onse ndi malangizo ake anzeru, ndipo anadula mutu wa Seba mwana wa Bikiri ndipo anawuponya kwa Yowabu. Kotero iye analiza lipenga ndipo anthu ake anachoka pa mzindawo, aliyense nʼkubwerera kwawo. Ndipo Yowabu anabwerera kwa mfumu ku Yerusalemu.
23 Joab var høvding over hele Israels hær, og Benaja, sønn av Jojada, var høvding over livvakten;
Yowabu ndiye amalamulira gulu lonse la ankhondo. Benaya mwana wa Yehoyada amalamulira Akereti ndi Apeleti.
24 Adoram hadde opsyn med dem som gjorde pliktarbeid, og Josafat, sønn av Akilud, var historieskriver;
Adoramu amayangʼanira anthu ogwira ntchito ya thangata, Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika,
25 Seja var statsskriver, og Sadok og Abjatar var prester.
Seva anali mlembi wa mfumu. Zadoki ndi Abiatara anali ansembe
26 Ja'iritten Ira var også prest hos David.
ndipo Ira wa ku Yairi anali wansembe wa Davide.