< 2 Peters 2 >
1 Men det opstod også falske profeter blandt folket, likesom det og blandt eder skal komme falske lærere, som skal lure inn vrange lærdommer som leder til fortapelse, idet de endog nekter den Herre som kjøpte dem, og fører over sig selv en brå fortapelse.
Koma panalinso aneneri onama pakati pa Aisraeli, monga padzakhalanso aphunzitsi onyenga pakati panu. Iwo adzalowetsa mwamseri ziphunzitso zonama ndi zowononga, nadzakana Ambuye amene anawawombola, ndipo motero adzadziyitanira okha chiwonongeko mwadzidzidzi.
2 Og mange skal følge dem efter i deres skamløshet, og for deres skyld skal sannhetens vei bli spottet,
Ambiri adzatsata njira zawo zochititsa manyazi ndipo chifukwa cha iwowa, anthu adzanyoza njira ya choonadi.
3 og av havesyke skal de med opdiktede ord utnytte eder til sin vinning. Men dommen over dem er fra gammel tid ikke ørkesløs, og deres fortapelse sover ikke.
Pofuna kupeza chuma, aphunzitsiwa adzakudyerani chuma chanu pokuwuzani nkhani zopeka. Chiweruzo chawo chinakonzedwa kale, ndipo chikuwadikira.
4 For så sant Gud ikke sparte engler da de syndet, men styrtet dem ned i avgrunnen og overgav dem til mørkets huler i varetekt til dom, (Tartaroō )
Pakuti Mulungu sanalekerere angelo atachimwa paja, koma anawaponya mʼndende, nawayika mʼmaenje amdima, kuwasunga kuti adzaweruzidwe. (Tartaroō )
5 og ikke sparte den gamle verden, men opholdt rettferdighetens forkynner Noah selv åttende, dengang han førte vannflommen over en verden av ugudelige,
Iye sanalekerere dziko lapansi kalelo, koma anapulumutsa Nowa, mlaliki wa chilungamo, ndi anthu ena asanu ndi awiri atadzetsa chigumula pa dziko lapansi kwa anthu akhalidwe losapembedza Mulunguyo.
6 og la byene Sodoma og Gomorra i aske og fordømte dem til undergang, og dermed har satt dem til et forbillede på de ugudelige i fremtiden,
Mulungu anaweruza mizinda ya Sodomu ndi Gomora nayiwononga ndi moto, kuti ikhale chitsanzo cha zimene zidzachitikira anthu osapembedza Mulungu.
7 og fridde ut den rettferdige Lot, som plagedes ved de ugudeliges skamløse ferd
Koma Iye anapulumutsa Loti, munthu wolungama, amene ankavutika ndi khalidwe lonyansa la anthu oyipa.
8 - for den rettferdige som bodde blandt dem, led dag for dag pine i sin rettferdige sjel ved de lovløse gjerninger han så og hørte -
(Pakuti munthu wolungamayo, pokhala pakati pawo tsiku ndi tsiku ankavutika mu mtima ndi makhalidwe awo oyipa amene ankawaona ndi kuwamva).
9 så sant vet Herren å utfri de gudfryktige av fristelser, men å holde de urettferdige i varetekt med straff til dommens dag,
Tsono mutha kuona kuti Ambuye amadziwa kuwapulumutsa kwake pa mayesero anthu opembedza. Amadziwanso kusunga osalungama kuti alangidwe mpaka tsiku la chiweruzo.
10 aller mest dem som går efter kjød i uren lyst og forakter herredømme. De selvgode vågehalser! De skjelver ikke for å spotte de høie makter,
Makamaka amene amatsata zilakolako zonyansa zathupi nanyoza ulamuliro. Anthu amenewa ndi odzikuza, ndipo otsata chifuniro cha iwo eni, sasamala za munthu, saopa kuchitira chipongwe zolengedwa za mmwamba.
11 mens dog engler, som er større i styrke og makt, ikke fremfører for Herren nogen spottende dom imot dem;
Komatu ngakhale angelo, amene ali akulu ndi amphamvu kuwaposa, sayankhula za chipongwe pobweretsa chiweruzo pa iwo kuchokera kwa Ambuye.
12 men disse, likesom ufornuftige dyr, av naturen født til å fanges og forgå - de skal, fordi de spotter det de ikke kjenner, også forgå i sin vanart
Koma anthu awa amachita chipongwe zinthu zimene sakuzidziwa. Ali ngati zirombo zopanda nzeru. Zirombo zolengedwa kuti zigwidwe ndi kuwonongedwa, ndipo ngati zirombozo adzawonongedwa.
13 og få urettferdighets lønn. De setter sin lyst i å bruke dagen til vellevnet; disse styggelser og skamflekker, de fråtser i sin svik når de holder gilde med eder;
Iwo adzalangidwa chifukwa cha zoyipa zimene anachita. Koma chimene chimawakomera ndi kumangochita zokondweretsa thupi masanasana. Iwo ali ngati mawanga ndi zilema. Podya nanu pamodzi amakondwera kuchita za chinyengo.
14 de har øine som er fulle av skjøgen og umettelige i synd; de forlokker ubefestede sjeler; de har et hjerte som er opøvd i havesyke, de forbannelsens barn!
Ndi maso awo odzaza ndi chigololo, salekeza kuchimwa. Amanyengerera anthu osakhazikika. Iwo ndi akatswiri pa dyera ndi chuma, ndipo ndi ana otembereredwa!
15 De har forlatt den bene vei og faret vill, idet de har fulgt Bileams, Beors sønns vei, han som elsket urettferdighets lønn
Iwo anasiya njira yolungama ndipo anapatuka kutsata njira ya Baalamu mwana wa Beori, amene anakonda malipiro a chosalungama.
16 og blev refset for sin egen brøde: et umælende trældyr talte med et menneskes mæle og hindret profetens dårskap.
Koma anadzudzulidwa chifukwa cha kulakwa kwakeko. Bulu, nyama imene siyankhula, inayankhula ngati munthu kuletsa misala ya mneneriyo.
17 Disse er vannløse brønner, skodde som drives av stormvind; mørkets natt er rede for dem.
Anthu amenewa ali ngati akasupe wopanda madzi, ndiponso ngati nkhungu yowuluzidwa ndi mphepo yamkuntho. Mulungu wawasungira mdima wandiweyani.
18 For idet de taler skrytende, tomme ord, forlokker de i kjødslyster ved usedelighet dem som just har flyktet bort fra dem som ferdes i forvillelse,
Pakuti anayankhula mawu opanda pake ndi onyada, ndipo ndi zilakolako zoyipa za thupi amanyenga anthu amene angopulumuka kumene pakati pa anzawo oyipa.
19 idet de lover dem frihet, de som selv er vanartens træler; for det som en ligger under for, det er han og blitt træl av.
Amawalonjeza ufulu, pomwe iwo eni ndi akapolo a zizolowezi zowononga. Pajatu munthu amakhala kapolo wa chilichonse chimene chikumulamulira.
20 For om de har flyktet bort fra verdens urenhet ved å ha lært vår Herre og frelser Jesus Kristus å kjenne, og så atter lar sig fange av den og ligger under for den, da er det siste blitt verre med dem enn det første.
Ngati anapulumuka ku zodetsa za dziko lapansi podziwa Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu, pambuyo pake nagwidwanso ndi kugonjetsedwa ndi zomwezo, potsiriza adzakhala oyipa kuposa mmene analili poyamba.
21 For det var bedre for dem at de ikke hadde kjent rettferdighetens vei, enn at de kjente den og så vendte sig bort fra det hellige bud som var overgitt dem.
Kukanakhala bwino akanapanda kudziwa njira ya chilungamo, koposa ndi kuyileka atadziwa lamulo loyera limene Mulungu anawapatsa.
22 Det er gått dem som det sanne ordsprog sier: Hunden vender sig om til sitt eget spy, og den vaskede so velter sig i søle.
Kwa iwo miyambi iyi ndi yoona, “Galu wabwerera ku masanzi ake,” ndipo, “Nkhumba imene inasamba, yakunkhunizikanso mʼmatope.”