< 2 Kongebok 25 >
1 I hans niende regjeringsår, i den tiende måned, på den tiende dag i måneden, drog kongen i Babel Nebukadnesar med hele sin hær mot Jerusalem og leiret sig mot det, og de bygget skanser mot det rundt omkring.
Choncho mʼchaka chachisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku lakhumi la mwezi, Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anabwera ndi gulu lake lonse la ankhondo, nadzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu. Iye anamanga misasa kunja kwa mzindawo ndipo anamanga mitumbira ya nkhondo kuzungulira mzindawo.
2 Og de holdt byen kringsatt like til kong Sedekias' ellevte år.
Mzindawo anawuzinga mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha Mfumu Zedekiya.
3 På den niende dag i måneden var hungersnøden så stor i byen at landets folk ikke hadde noget å ete.
Pa tsiku lachisanu ndi chinayi pa mwezi wachinayi, njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti anthu analibe chakudya.
4 Og byens mur blev gjennembrutt, og alle krigsmennene flyktet om natten gjennem porten mellem begge murene ved kongens have, mens kaldeerne lå leiret mot byen rundt omkring; og han tok veien til ødemarken.
Pamenepo khoma la mzindawo linabowoledwa ndipo gulu lonse la ankhondo linathawa usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Iwo anathawira cha ku Araba,
5 Men kaldeernes hær satte efter kongen og nådde ham igjen på Jerikos ødemarker; og hele hans hær spredte sig og forlot ham.
koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.
6 Og de grep kongen og førte ham op til Babels konge i Ribla og avsa dom over ham.
Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula, kumene anagamula mlandu wa Zedekiyayo.
7 De drepte Sedekias' sønner for hans øine, og han lot Sedekias selv blinde og lot ham binde med to kobberlenker; så førte de ham til Babel.
Iwo anapha ana a Zedekiya iyeyo akuona. Kenaka anakolowola maso a Zedekiya namumanga ndi unyolo wamkuwa ndi kupita naye ku Babuloni.
8 I den femte måned, på den syvende dag i måneden - det var Babels konge Nebukadnesars nittende år - kom Nebusaradan, høvdingen over livvakten, en av Babels konges menn, til Jerusalem.
Mwezi wachisanu, pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi, mʼchaka cha 19 cha Nebukadinezara, mfumu ya Babuloni, Nebuzaradani, mkulu wa asilikali oteteza mfumu, nduna ya mfumu ya Babuloni, anabwera ku Yerusalemu.
9 Han brente op Herrens hus og kongens hus, og alle Jerusalems hus - alle stormennenes hus - brente han op med ild.
Iye anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu pamodzi ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse yofunika.
10 Og hele den hær av kaldeere som høvdingen over livvakten hadde med sig, rev ned murene rundt omkring Jerusalem.
Gulu lonse la ankhondo la ku Babuloni limene linali ndi mkulu wa asilikali oteteza mfumu ija, linagumula malinga ozungulira Yerusalemu.
11 Nebusaradan, høvdingen over livvakten, bortførte resten av folket, dem som var blitt tilbake i byen, og overløperne som var gått over til kongen i Babel, og resten av hopen.
Nebuzaradani mkulu wa asilikali uja anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, ndi ena amene anathawira kwa mfumu ya Babuloni, pamodzi ndi ena onse kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
12 Bare nogen av de ringeste i landet lot høvdingen over livvakten bli tilbake som vingårdsmenn og jordbrukere.
Koma mkulu wa asilikaliyo anasiya anthu ena osauka kwambiri mʼdzikomo kuti azisamalira minda ya mpesa ndi minda ina.
13 Kaldeerne slo i stykker kobbersøilene i Herrens hus og fotstykkene og kobberhavet i Herrens hus og førte kobberet av dem til Babel.
Ababuloni anaphwanya zipilala zamkuwa, maphaka ndiponso mbiya ya mkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndipo anatenga mkuwawo napita nawo ku Babuloni.
14 De tok også askebøttene og ildskuffene og knivene og røkelseskålene og alle kobberkarene som hadde vært brukt til tjenesten.
Iwo anatenganso miphika, mafosholo, mbaniro za nyale, mbale ndi ziwiya zonse zamkuwa zimene ankagwiritsa ntchito potumikira mʼNyumbayo.
15 Også fyrfatene og skålene til å sprenge blod med, alt hvad det var av gull og alt hvad det var av sølv, det tok høvdingen over livvakten.
Mkulu wa asilikali uja anatenganso zofukizira lubani ndi mbale zowazira magazi. Zonsezi zinali zopangidwa ndi golide wabwino kwambiri kapena siliva.
16 De to søiler, det ene hav og fotstykkene som Salomo hadde latt gjøre for Herrens hus - i alle disse ting var kobberet ikke til å veie.
Mkuwa wochokera ku zipilala ziwiri zija, mbiya ija ndi maphaka aja, zimene Solomoni anapanga mʼNyumba ya Yehova, kuchuluka kwake kunali kosawerengeka.
17 Atten alen høi var den ene søile, og det var et søilehode på den av kobber, og søilehodet var tre alen høit, og det var nettverk og granatepler på søilehodet rundt omkring, alt sammen av kobber, og likedan var det med den andre søile ved nettverket.
Chipilala chilichonse chinali chotalika mamita asanu ndi atatu. Mutu wa mkuwa umene unali pamwamba pa chipilalacho unali mita imodzi ndi theka ndipo unakongoletsedwa ndi ukonde wa makangadza a mkuwa amene anazungulira mutuwo. Chipilala chachiwiri chinali chofanana ndi chinacho, ndipo chinali ndi ukonde.
18 Høvdingen over livvakten tok ypperstepresten Seraja og Sefanja, en prest av annen rang, og de tre voktere ved dørtreskelen,
Mkulu wa asilikali uja anagwira ukapolo mkulu wa ansembe Seraya, Zefaniya wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apakhomo.
19 og fra byen tok han en hoffmann som var høvedsmann over krigsfolkene, og fem menn som ennu fantes i byen av dem som stadig hadde adgang til kongen, og skriveren hos hærføreren, han som utskrev landets folk til krigstjeneste, og seksti menn av landets folk som fantes i byen -
Mwa anthu amene anali mu mzindamo, anatenga mkulu amene ankalamulira ankhondo ndiponso alangizi asanu a mfumu. Anatenganso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo amene ankalemba anthu ntchito ya usilikali mʼdzikomo pamodzi ndi anthu ake 60 amene anali mu mzindamo.
20 dem tok Nebusaradan, høvdingen over livvakten, og førte til Babels konge i Ribla,
Nebuzaradani mkulu wa asilikali uja anawatenga onsewo napita nawo kwa mfumu ya Babuloni ku Ribula.
21 og Babels konge lot dem slå ihjel i Ribla i Hamat-landet. Således blev Juda bortført fra sitt land.
Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloni inalamula kuti awakwapule ndi kuwapha. Choncho Ayuda anatengedwa ukapolo kuwachotsa mʼdziko lawo.
22 Over de folk som blev tilbake i Juda land, dem som kongen i Babel Nebukadnesar lot bli tilbake, satte han Gedalja, sønn av Akikam, Safans sønn.
Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu, mwana wa Safani, kukhala woyangʼanira anthu amene anatsala ku Yuda.
23 Da alle høvedsmennene for hærflokkene og deres menn hørte at kongen i Babel hadde satt Gedalja over landet, kom de til ham i Mispa - det var Ismael, Netanjas sønn, og Johanan, Kareahs sønn, og Seraja, Tanhumets sønn, fra Netofat og Ja'asanja, ma'akatittens sønn, med sine menn.
Atsogoleri onse ankhondo ndi anthu awo atamva kuti mfumu ya Babuloni yasankha Gedaliya kukhala bwanamkubwa, anabwera kwa Gedaliya ku Mizipa. Atsogoleriwo mayina awo anali awa: Ismaeli mwana wa Netaniya, Yohanani mwana wa Kareya, Seraya mwana wa Tanihumeti wa ku Netofa ndi Yaazaniya mwana wa Maakati, pamodzi ndi anthu awo.
24 Og Gedalja gav dem og deres menn sin ed og sa til dem: Vær ikke redd kaldeernes menn, bli i landet og tjen kongen i Babel! Så skal det gå eder vel.
Gedaliya analumbira powatsimikizira iwo ndi anthu awo. Iye anati, “Musachite mantha ndi atsogoleri Ababuloniwa. Khalani mʼdziko muno ndipo tumikirani mfumu ya Babuloni. Mukatero zinthu zidzakuyenderani bwino.”
25 Men i den syvende måned kom Ismael, sønn av Netanja, Elisamas sønn, en mann av kongelig ætt, og ti andre menn med ham, og de slo Gedalja ihjel, og likeså de jøder og kaldeere som var hos ham i Mispa.
Koma pa mwezi wachisanu ndi chiwiri, Ismaeli mwana wa Netaniya, mwana wa Elisama, wa banja laufumu, anabwera ndi anthu khumi ndipo anapha Gedaliya pamodzi ndi Ayuda ndi anthu a ku Babuloni amene anali naye limodzi ku Mizipa.
26 Da brøt alt folket op, både store og små, og høvedsmennene for hærflokkene, og de drog til Egypten; for de var redd kaldeerne.
Chifukwa cha zimenezi, anthu onse kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo anathawira ku Igupto chifukwa choopa Ababuloni.
27 I det syv og trettiende år efterat Judas konge Jojakin var bortført, i den tolvte måned, på den syv og tyvende dag i måneden, tok kongen i Babel Evilmerodak - i det år han blev konge - Judas konge Jojakin til nåde og førte ham ut av fengslet.
Pa chaka cha 37 cha ukapolo wa Yehoyakini mfumu ya Yuda, chaka chimene Evili-Merodaki anakhala mfumu ya Babuloni, anamasula Yehoyakini mʼndende pa mwezi wa 12 pa tsiku la 27.
28 Og han talte vennlig med ham og satte hans stol ovenfor stolene til de andre konger som var hos ham i Babel.
Anamukomera mtima namukweza kupambana mafumu ena onse amene anali naye ku Babuloni.
29 Han la sin fangedrakt av og åt stadig ved hans bord, så lenge han levde.
Choncho Yoyakini anavula zovala zake za ku ndende, ndipo ankadya ndi mfumu masiku onse a moyo wake.
30 Og han fikk sitt stadige underhold fra kongen, hver dag det han den dag tiltrengte, så lenge han levde.
Mfumu inkamupatsa Yehoyakini chakudya tsiku lililonse pa moyo wake wonse.