< 2 Kongebok 1 >
1 Efter Akabs død falt Moab fra Israel.
Atamwalira Ahabu, Mowabu anawukira Israeli.
2 Akasja falt ut gjennem gitteret i sin sal i Samaria og blev syk. Da skikket han nogen sendebud avsted og sa til dem: Gå og spør Ba'al-Sebub, Ekrons gud, om jeg skal komme mig av denne sykdom!
Ndipo Ahaziya anagwa kuchokera pa khonde la chipinda chake chammwamba ku Samariya, ndipo anavulala kwambiri. Choncho iye anatuma amithenga nawawuza kuti, “Pitani mukafunse kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, ngati ndichire matendawa.”
3 Men Herrens engel sa til tisbitten Elias: Gjør dig rede og gå sendebudene fra Samarias konge i møte og si til dem: Er det fordi det ingen Gud er i Israel, at I går avsted og spør Ba'al-Sebub, Ekrons gud?
Koma mngelo wa Yehova anawuza Eliya wa ku Tisibe kuti, “Nyamuka, pita ukakumane ndi amithenga a mfumu ya ku Samariya ndipo ukawafunse kuti, ‘Kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake inu mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni?’
4 Derfor sier Herren så: Du skal ikke stige ned fra den seng du er steget op i; du skal dø. Dermed gikk Elias.
Tsono Yehova akuti, ‘Iweyo sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’” Ndipo Eliya ananyamuka.
5 Da sendebudene vendte tilbake til ham, spurte han dem: Hvorfor er I vendt tilbake?
Amithenga aja atabwerera kwa mfumu, mfumuyo inawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwabwerera?”
6 De svarte: En mann kom oss i møte og sa til oss: Gå tilbake til kongen som har sendt eder, og si til ham: Så sier Herren: Er det fordi det ingen Gud er i Israel, at du sender bud for å spørre Ba'al-Sebub, Ekrons gud? Derfor skal du ikke stige ned fra den seng du er steget op i; du skal dø.
Iwo anayankha kuti, “Munthu wina anabwera kudzakumana nafe, ndipo anatiwuza kuti, bwererani kwa mfumu imene inakutumani ndipo mukayiwuze kuti, ‘Yehova akuti, kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni? Tsono sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’”
7 Han spurte dem: Hvorledes så den mann ut som kom eder i møte og talte således til eder?
Mfumu inafunsa amithengawo kuti, “Kodi munthu amene anabwera kudzakumana nanuyo ndi kukuwuzani zimenezi amaoneka bwanji?”
8 De svarte: Det var en mann i en lodden kjortel, med et lærbelte bundet om lendene. Da sa han: Det var tisbitten Elias.
Iwo anayankha kuti, “Munthuyo anavala zovala zaubweya ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake.” Mfumu inati, “Munthu ameneyo ndi Eliya wa ku Tisibe.”
9 Og han sendte til ham en høvedsmann over femti med sine menn; og han gikk op til ham, der han satt på toppen av fjellet, og han sa til ham: Du Guds mann! Kongen sier: Kom ned!
Pamenepo mfumu inatuma mtsogoleri wa ankhondo ndi anthu ake makumi asanu kwa Eliya. Mtsogoleriyo anapita kwa Eliya, amene anali atakhala pamwamba pa phiri, ndipo anati, “Munthu wa Mulungu, mfumu ikuti, ‘Tsikani!’”
10 Men Elias svarte høvedsmannen over femti: Er jeg en Guds mann, så fare ild ned fra himmelen og fortære dig og dine femti mann! Da fór det ild ned fra himmelen og fortærte ham og hans femti mann.
Eliya anayankha mtsogoleriyo kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu makumi asanu akowo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
11 Så sendte han til ham en annen høvedsmann over femti med sine menn; og han tok til orde og sa til ham: Du Guds mann! Så sier kongen: Kom straks ned!
Zitachitika izi, mfumu inatumanso mtsogoleri wina pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleriyo anati kwa Eliya, “Munthu wa Mulungu, zimene mfumu ikunena ndi izi, ‘Tsikani msangamsanga!’”
12 Men Elias svarte dem: Er jeg en Guds mann, så fare ild ned fra himmelen og fortære dig og dine femti mann! Da fór Guds ild ned fra himmelen og fortærte ham og hans femti mann.
Eliya anayankha kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu ako makumi asanuwo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
13 Så sendte han igjen en tredje høvedsmann over femti med sine menn; og denne tredje høvedsmann gikk op til Elias og falt på kne for ham og bønnfalt ham og sa til ham: Du Guds mann! La mitt liv og disse dine femti tjeneres liv være dyrt i dine øine!
Ndipo mfumu inatumanso mtsogoleri wachitatu pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleri wachitatuyu anakwera pa phiripo ndi kugwada pamaso pa Eliya. Iye anayankhula mopemba kuti, “Munthu wa Mulungu, chonde musandiwononge ineyo pamodzi ndi atumiki makumi asanu anuwa!
14 Ild fór ned fra himmelen og fortærte begge de første høvedsmenn over femti med sine menn; men la nu mitt liv være dyrt i dine øine!
Taonani, moto unatsika kuchokera kumwamba ndi kupsereza atsogoleri awiri pamodzi ndi anthu awo onse. Koma tsopano musawononge moyo wanga!”
15 Da sa Herrens engel til Elias: Gå ned med ham, og vær ikke redd ham! Så stod han op og gikk med ham ned til kongen.
Mngelo wa Yehova anati kwa Eliya, “Pita naye, usamuope.” Choncho Eliya ananyamuka natsika naye limodzi kupita kwa mfumu.
16 Og han sa til ham: Så sier Herren: Fordi du skikket sendebud og vilde spørre Ba'al-Sebub, Ekrons gud, som om det ingen Gud var i Israel som du kunde spørre derom - derfor skal du ikke stige ned fra den seng du er steget op i; du skal dø.
Eliya anawuza mfumu kuti, “Yehova akuti, ‘Chifukwa chiyani munatumiza amithenga kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, kukafunsa ngati muti muchire? Kodi mu Israeli mulibe Mulungu woti nʼkukuyankhani funso lanu? Choncho, popeza mwachita izi, simudzadzuka pamene mwagonapo; mudzafa ndithu.’”
17 Og han døde efter det Herrens ord som Elias hadde talt, og Joram blev konge i hans sted i Judas konge Jorams, Josafats sønns annet år; for han hadde ikke nogen sønn.
Motero Ahaziya anafadi, monga mwa mawu a Yehova amene Eliya anayankhula. Tsono popeza Ahaziya analibe mwana, Yoramu analowa ufumu mʼmalo mwake mʼchaka chachiwiri cha Yehoramu mwana wa Yehosafati mfumu ya ku Yuda.
18 Hvad som ellers er å fortelle om Akasja og det han gjorde, det er opskrevet i Israels kongers krønike.
Ntchito zina zonse zimene Ahaziya anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?