< 2 Krønikebok 23 >
1 Men i det syvende år tok Jojada mot til sig og gjorde en pakt med nogen av høvedsmennene over hundre; det var Asarja, Jerohams sønn, og Ismael, Johanans sønn, og Asarja, Obeds sønn, og Ma'aseja, Adajas sønn, og Elisafat, Sikris sønn.
Mʼchaka chachisanu ndi chiwiri Yehoyada anaonetsa mphamvu zake. Iye anachita pangano ndi olamulira magulu a anthu 100: Azariya mwana wa Yerohamu, Ismaeli mwana wa Yehohanani, Azariya mwana wa Obedi, Maaseya mwana wa Adaya ndi Elisafati mwana wa Zikiri.
2 Så drog de omkring i Juda og samlet levittene fra alle Judas byer og Israels familiehoder; og da de kom til Jerusalem,
Iwo anayendayenda mʼdziko la Yuda ndipo anasonkhanitsa Alevi ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli ochokera mʼmizinda yonse. Atabwera ku Yerusalemu,
3 gjorde hele forsamlingen en pakt med kongen i Guds hus, og Jojada sa til dem: Kongens sønn skal nu være konge, således som Herren har sagt om Davids sønner.
msonkhano wonse unachita pangano ndi mfumu mu Nyumba ya Mulungu. Yehoyada anawawuza kuti, “Mwana wa mfumu adzalamulira monga ananenera Yehova zokhudza ana a Davide.
4 Hør nu hvad I skal gjøre: Den ene tredjedel av eder, de prester og levitter som tiltreder vakttjenesten på sabbaten, skal stå vakt ved dørtresklene,
Tsopano zimene muti muchite ndi izi: Limodzi mwa magawo atatu a ansembe ndi Alevi amene mudzakhale pa ntchito pa Sabata muzikalondera pa khomo,
5 og den annen tredjedel ved kongeboligen og den tredje tredjedel ved Jesod-porten, og alt folket i forgårdene ved Herrens hus.
ndi limodzi la magawo atatu likakhale ku nyumba yaufumu ndipo limodzi la magawo atatu likakhale ku chipata cha Maziko ndipo anthu ena onse akakhale mʼmabwalo a Nyumba ya Yehova.
6 Men ingen må komme inn i Herrens hus uten prestene og de av levittene som gjør tjeneste; de kan gå inn, for de er hellige; men alle de andre av folket skal holde sig efter det Herren har foreskrevet.
Musalole aliyense kulowa mʼNyumba ya Yehova kupatula ansembe ndi Alevi amene akutumikira. Iwo atha kutero chifukwa apatulidwa koma anthu ena onse ayenera kumvera zimene Yehova walamula.
7 Levittene skal stille sig rundt omkring kongen, hver mann med våben i hånd, og den som kommer inn i huset, skal drepes; I skal være om kongen, både når han går inn, Og når han går ut.
Alevi akhale mozungulira mfumu, munthu aliyense ali ndi chida chake mʼmanja. Aliyense amene alowe mʼNyumba ya Mulungu ayenera kuphedwa. Mukhale nayo pafupi mfumu kulikonse kumene izipita.”
8 Levittene og hele Juda gjorde aldeles som presten Jojada hadde befalt; de tok hver sine menn, både dem som tiltrådte på sabbaten, og dem som trådte av på sabbaten; for presten Jojada hadde ikke latt skiftene få hjemlov.
Alevi ndi anthu onse a ku Yuda anachita monga momwe wansembe Yehoyada anawalamulira. Aliyense anatenga anthu ake amene ankagwira ntchito pa Sabata ndi amene amapita kukapuma, pakuti wansembe Yehoyada sanalole gulu lililonse kuti lipite.
9 Og presten Jojada gav høvedsmennene de spyd og små og store skjold som hadde tilhørt kong David, og som var i Guds hus.
Ndipo Yehoyada anapereka kwa atsogoleri a magulu a anthu 100 mikondo ndi zishango zazikulu ndi zazingʼono zimene zinali za Davide ndipo zinali mʼNyumba ya Mulungu.
10 Og han stilte alt folket op, hver mann med våben i hånd, fra husets høire side til husets venstre side bortimot alteret Og bortimot huset rundt omkring kongen.
Iye anayika anthu onse, aliyense ali ndi chida mʼdzanja lake mozungulira mfumu pafupi ndi guwa ndi Nyumba ya Mulungu, kuyambira mbali ya kummwera mpaka kumpoto kwa Nyumba ya Mulungu.
11 Så førte de kongesønnen ut og satte kronen på ham og overgav ham vidnesbyrdet, og de gjorde ham til konge; og Jojada og hans sønner salvet ham og ropte: Kongen leve!
Yehoyada ndi ana ake anatulutsa mwana wa mfumu ndipo anamumveka chipewa chaufumu ndipo anamupatsa Buku la Chipangano namulonga ufumu. Yehoyada ndi ana ake anamudzoza ndipo anafuwula kuti, “Ikhale ndi moyo wautali mfumu!”
12 Da Atalja hørte ropet fra folket som sprang frem og hyldet kongen, gikk hun inn i Herrens hus til folket.
Ataliya atamva phokoso la anthu akuthamanga ndi kukondwerera mfumu, anapita ku Nyumba ya Yehova komwe kunali anthuko.
13 Der fikk hun se at kongen stod på sin forhøining i inngangen, og høvedsmennene og trompetblåserne stod hos ham, og hele folkemengden gledet sig og støtte i trompetene, og sangerne var der med sine instrumenter og sang Herrens lov og pris; da sønderrev Atalja sine klær og ropte: Oprør, oprør!
Iye anayangʼana, ndipo anaona mfumu itayima pa chipilala chake chapakhomo. Atsogoleri ndi oyimba malipenga anali pafupi ndi mfumuyo, ndipo anthu onse a mʼderali amakondwerera ndi kuyimba malipenga ndiponso oyimba ndi zida amatsogolera matamando. Pamenepo Ataliya anangʼamba mkanjo wake ndipo anafuwula kuti, “Kuwukira! Kuwukira!”
14 Men presten Jojada lot høvedsmennene, dem som var satt over hæren, gå ut og sa til dem: Før henne ut mellem rekkene, og om nogen følger henne, så skal han drepes med sverd. For presten hadde sagt: I skal ikke drepe henne i Herrens hus.
Wansembe Yehoyada anatumiza olamulira magulu a anthu 100 aja, amene amayangʼanira asilikali ndipo anawawuza kuti, “Mutulutseni ameneyu pakati pa mizere yanu ndipo muphe aliyense amene adzamutsata.” Pakuti ansembe anati, “Musamuphere mʼNyumba ya Mulungu wa Yehova,”
15 Så gjorde de plass for henne til begge sider, og da hun kom dit hvor Hesteporten fører inn til kongens hus, drepte de henne.
choncho anamugwira pamene amafika pa chipata cha Kavalo pa bwalo la nyumba yaufumu, ndipo anamuphera pamenepo.
16 Og Jojada gjorde en pakt mellem sig og alt folket og kongen at de skulde være Herrens folk.
Tsono Yehoyada anachita pangano, iye mwini ndi anthu onse ndiponso mfumu kuti adzakhala anthu a Yehova.
17 Og alt folket gikk inn i Ba'als hus og rev det ned; hans altere og hans billeder knuste de, og Ba'als prest Mattan drepte de foran alterne.
Anthu onse anapita ku kachisi wa Baala ndipo anamugwetsa. Iwo anaphwanya maguwa ndi mafano ndi kupha Matani wansembe wa Baala patsogolo pa maguwawo.
18 Og Jojada overlot tilsynet i Herrens hus til de levittiske prester, som David hadde inndelt i skifter for tjenesten i Herrens hus, til å ofre Herrens brennoffere, som skrevet er i Mose lov, med glede og sang efter Davids forskrift.
Kenaka Yehoyada anayika ansembe, omwe anali Alevi kukhala oyangʼanira Nyumba ya Yehova, amene Davide anawapatsa ntchito yoti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova mʼNyumba ya Mulungu, monga zinalembedwa mʼmalamulo a Mose kuti azitero akukondwera ndi kuyimba monga Davide analamulira.
19 Og han satte dørvoktere ved portene til Herrens hus, forat ingen som var blitt uren på nogen måte, skulde komme inn der.
Ndipo anayika alonda a pa khomo pa zipata za Nyumba ya Yehova kuti aliyense amene ndi odetsedwa asalowe.
20 Så tok han med sig høvedsmennene over hundre og de fornemste og de mektige blandt folket og hele folkemengden og førte kongen ned fra Herrens hus, og de gikk gjennem den øvre port inn i kongens hus og satte kongen på kongetronen.
Iye anatenga olamulira magulu a anthu 100, anthu otchuka, olamulira anthu ndi anthu onse a mʼderalo ndipo anabweretsa mfumu kuchokera ku Nyumba ya Mulungu. Iwo anapita ku nyumba yaufumu kudzera ku Chipata Chakumitu ndipo anayikira mfumu mpando wolemekezeka,
21 Og hele folkemengden gledet sig, og byen var rolig; men Atalja hadde de drept med sverd.
ndipo anthu onse a mʼderali anakondwera. Tsono mu mzinda munali bata chifukwa Ataliya anaphedwa ndi lupanga.